< Psalm 97 >

1 Der Herr ist König. Erde freue dich! Und fröhlich sei'n die Inseln, soviel ihrer sind!
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Gewölk und Dunkel um ihn her; und seines Thrones Stütze ist Gerechtigkeit und Recht.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Auflodere vor ihm ein Feuer und senge ringsum seine Feinde!
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Die Welt erhellen sollen seine Blitze; die Erde schaue es und zittere!
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Die Berge schmelzen vor dem Herrn wie Wachs, vor ihm, dem Herrn der ganzen Erde!
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Die Himmel sollen künden seinen Sieg; die Völker alle schauen seinen Ruhm!
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Zuschanden sollen werden alle Bildanbeter, die stolz auf Götzen sind; hinsinken sollen in den Staub vor ihm die Götter alle!
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Mit Freuden hör es Sion, und Judas Töchter sollen jubeln ob Deiner Strafgerichte, Herr!
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Für alle Welt bist Du der Höchste, Herr, hoch erhaben über alle Götter.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Die ihr den Herren liebet, haßt das Böse! Er schirmt die Seelen seiner Frommen und reißt sie aus der Bösen Hand.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Den Frommen wird ein Licht bereitet und Freude denen, die geraden Herzens.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Ihr Frommen, freut euch an dem Herrn! Preist seinen heiligen Namen!
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< Psalm 97 >