< Psalm 96 >

1 Dem Herrn zu Ehren singt ein neues Lied! Dem Herrn lobsinge alle Welt!
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Lobsingt dem Herrn; lobpreiset seinen Namen! Von Meer zu Meer tut kund sein Heil!
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Verkündet bei den Heiden seinen Ruhm, bei allen Völkern seine Wunder,
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 ist doch der Herr so groß und lobesam, vor allen Göttern ehrfurchtswert!
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Der Völker Götter sind ja alle Götzen; des Himmels Schöpfer ist der Herr.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Vor ihn mit Glanz und Herrlichkeit! Mit Macht und Pracht zu seinem Heiligtum!
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 So bringt dem Herrn, ihr Völkerscharen, herbei bringt Pracht und Macht dem Herrn!
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 So bringt dem Herrn zu seines Namens Ehre Gaben! Betretet mit Geschenken seine Vorhöfe!
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Werft vor den Herrn euch hin mit Schmuck fürs Heiligtum! Vor ihm erzittere die ganze Welt!
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Den Heiden rufet zu: "Der Herr ist König. Darum steht die Welt und wanket nimmer. Er richtet Völker in Gerechtigkeit."
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Der Himmel freue sich! Die Erde jauchze, das Meer und was darin, erbrause!
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Die Flur frohlocke auch mit allem, was darauf! Die Waldesbäume alle jubeln vor dem Herrn:
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 "Er kommt, er kommt, der Erde Richter. Er richtet nach Gerechtigkeit die Welt und die Nationen unparteiisch."
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Psalm 96 >