< Psalm 38 >

1 Ein Lied; von David, zum Erlernen. Bestraf mich nicht in Deinem Zorne, Herr! In Deinem Grimme züchtige mich nicht noch mehr!
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 Denn Deine Pfeile sind gar tief in mich gedrungen, und Deine Hand liegt schwer auf mir.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 An meinem Fleische ist nichts heil ob Deinem Zorn, nichts unversehrt an meinem Leib ob meiner Sünde.
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 Denn meine Sünden übersteigen mir das Haupt, sind mir zu schwer, wie eine ungeheure Last.
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 Und eiternd faulen meine Wunden um meiner Torheit willen.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 Ich winde mich und krümme mich so heftig und allzeit gehe ich betrübt einher.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 In meinem Innern wühlt der Brand; an meinem Leib ist nichts Gesundes.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 Ich bin gelähmt, zermalmt und stöhne; mir klopft das Herz.
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Vor Dir liegt jeder meiner Wünsche offen, Herr; mein Seufzen ist Dir nicht verborgen.
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 Mir pocht das Herz und steht mir still, und meine Kraft, mein Augenlicht versagen mir den Dienst.
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 Die Freunde und Gefährten treten zurück vor meiner Plage; fern stehen die Verwandten mir.
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 Die auf mein Leben lauern, legen Schlingen, und die mein Unglück suchen, drohen mit Verderben und schmieden täglich Ränke.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 Und ich? Ich bin wie taub und höre nichts, bin wie ein Stummer, der den Mund nicht öffnet,
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 bin wie ein Mensch, der nichts versteht und keinen Widerspruch im Munde führt.
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 Denn ich vertraue, Herr, auf Dich; Du Herr, mein Gott, wirst Rede stehen,
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 Weil ich mir sag, sie dürfen meiner nimmer spotten, und glitte aus mein Fuß, nicht über mich frohlocken.
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 Schon bin ich ja dem Falle nah, stets meiner Schwäche mir bewußt.
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 Denn ich bekenne meine Schuld und gräme mich um meine Sünde.
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 Doch zahlreich sind, die unverschuldet mich befeinden, und viele, die mich grundlos hassen,
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 und die mit Bösem Gutes mir vergelten, mich lästern, daß ich nach dem Guten strebe.
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Verlaß mich nicht, o Herr! Mein Gott, entfern Dich nicht von mir!
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Zu meinem Schutze schnell herbei! Zu Hilfe, Herr!
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< Psalm 38 >