< Psalm 37 >

1 Von David. - Ereifere dich nicht der Bösewichte wegen! Beneide nicht die Übeltäter!
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 Sie welken schnell wie Gras, verdorren wie das grüne Kraut.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Vertrau dem Herrn! Tu Gutes! Verbleib im Land, dich redlich nährend!
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Wie ein verwöhntes Kind komm zu dem Herrn! Er gibt dir, was dein Herz sich wünscht.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Befiehl du deinen Weg dein Herrn! Auf ihn vertrau! Er wird's schon machen.
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 Er bringt ans Licht, daß du gerecht, und an den Tag, daß du im Recht.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Und schweig zum Herrn und harre sein! Ereifere über den dich nicht, der sich Erfolg erzwingt, nicht über einen Mann, der Schwindel treibt!
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Gib auf den Ärger! So ereifere dich nicht, daß selbst du Böses tätest!
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Denn ausgerottet werden Übeltäter; die auf den Herrn vertrauen, bleiben im Besitz des Landes.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Noch kurze Zeit! Dann ist der Bösewicht dahin! Du schaust nach seiner Stätte. Er ist nicht mehr.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Die Dulder bleiben im Besitz des Landes an reichem Glücke sich erlabend.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Dem Frommen plant zuleid der Frevler Arges und fletscht die Zähne wider ihn.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 Der Herr lacht seiner; schon sieht er seinen Tag sich nahen.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Die Frevler zücken zwar ihr Schwert und spannen ihren Bogen, um Elende und Arme zu erlegen und hinzuwürgen, die geraden Wandels.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Allein ihr Schwert dringt in ihr eigen Herz, und ihre Bogen splittern.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Das Wenige bekommt dem Frommen besser, als Frevlern großer Reichtum.
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 Zerbrochen werden ja der Frevler Arme; die Frommen aber stützt der Herr.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Der Herr sorgt für die Tage lauterer Menschen, und ihr Besitztum dauert immerfort.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Sie werden nicht in böser Zeit zuschanden; sie werden satt in Hungertagen.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Denn nur die Frevler gehn zugrunde, des Herrn Feinde gleich der Auen Pracht; sie schwinden hin wie Rauch; sie schwinden.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Der Frevler borgt, kann's aber nicht zurückerstatten; freigebig, milde kann der Fromme sein.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 Denn die von ihm Gesegneten verbleiben im Besitz des Landes; doch die von ihm Verfluchten werden ausgerottet.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 Sind eines Mannes Schritte recht im Hinblick auf den Herrn, dann kümmert dieser sich um seinen Weg.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 Und wankt er auch, so stürzt er nicht; ihn stützt der Herr mit seiner Hand.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Ich war ein Jüngling, ward ein Greis; doch ganz verlassen habe ich den Frommen nie gesehen, noch sein Geschlecht um Nahrung betteln.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 Stets milde, leiht es allezeit; zum Segen sät es aus.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Dem Laster gram, der Tugend hold, so bleibst du immerdar.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Der Herr liebt ja das Recht; von seinen Frommen läßt er nicht. Sie sind für alle Zeit geschützt; der Frevler Brut wird ausgerottet.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Den Frommen wird das Land zu eigen, sie bleiben ewiglich darin.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 Des Frommen Mund spricht Weises; nur Rechtes redet seine Zunge.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 Im Herzen trägt er seines Gottes Lehre, und seine Schritte schwanken nie.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 Der Frevler lauert auf dem Frommen, begierig, ihn zu morden.
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Doch überläßt der Herr ihn nimmer seiner Hand, läßt vor Gericht ihn nicht verdammen.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Dem Herrn vertrau! Halt dich an seinen Weg! Dann gibt er dir das Land zu eigen; der Frevler Untergang erlebst du noch.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 Ich habe einen Frevler voller Trotz gesehen, so kahl gemacht wie Gras im Felde.
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 Man schaute um; er war nicht mehr. Ich suchte ihn; er war nicht mehr zu finden.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Merk auf die Lauteren! Schau auf die Redlichen, wie's jedem gut am Ende geht!
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 Die Missetäter aber werden all vertilgt; der Frevler Zukunft wird vernichtet.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 Der Frommen Heil dagegen kommt vom Herrn; er ist ihr Schutz zur Zeit der Not.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Der Herr steht ihnen bei und rettet sie; er schirmt und schützt sie vor dem Bösen; denn sie vertraun auf ihn.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psalm 37 >