< Psalm 115 >

1 Nicht uns, nicht uns, nein, Deinem Namen gib die Ehre, Herr, und Deiner Huld und Deiner Treue!
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Was sollten schon die Heiden sagen: "Wo ist ihr Gott?"
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Im Himmel ist er, unser Gott, der alles, was er will, vollbringt. -
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Doch ihre Götzen sind von Gold und Silber, ein Werk von Menschenhänden.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Sie haben einen Mund und reden nicht; Sie haben Augen, doch sie sehen nicht.
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 Nicht hören sie mit ihren Ohren; nicht riechen sie mit ihrer Nase.
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 Nicht tasten sie mit ihren Händen; nicht gehen sie mit ihren Füßen; sie bringen keinen Laut aus ihrer Kehle.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Wie sie, so werden ihre Schöpfer und alle, die auf sie vertrauen. -
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Hat aber Israel fest auf den Herrn gebaut, dann ist er ihm ein Schutz und Schild.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Baut Aarons Haus fest auf den Herrn, dann ist er ihnen Schutz und Schild.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Und bauen, die den Herren fürchten, auf den Herrn, dann ist er ihnen Schutz und Schild.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 So segne unsern Fortbestand der Herr! Er segne das Haus Israel! Er segne Aarons Haus!
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 Er segne, die den Herren fürchten, die Kleinen mit den Großen!
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Der Herr vermehre euch, euch selbst und eure Kinder!
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 So seid gesegnet von dem Herrn, dem Schöpfer Himmels und der Erde! -
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Der Himmel ist ein Himmel für den Herrn; die Erde nur gibt er den Menschenkindern.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Die Toten loben nicht den Herrn, nicht die ins stille Reich Gesunkenen.
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 Dagegen wollen wir den Herrn lobpreisen von nun an bis in Ewigkeit. Alleluja!
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Psalm 115 >