< Psalm 114 >

1 Als Israel Ägypten und Jakobs Haus das fremde Volk verließ,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 da ward Juda sein Heiligtum und Israel sein Reich.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Dies sah das Meer und floh; der Jordan ging zurück.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Die Berge hüpften gleich den Widdern, die Hügel wie die Lämmer. -
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Was ist dir, Meer? Du fliehst. Was, Jordan, dir? Du gehst zurück.
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Euch Bergen, daß ihr gleich den Widdern, euch Hügeln, daß ihr gleich den Lämmern hüpfet; -
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Erbebe, Erde, vor dem Herrn, vor Jakobs Gott,
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 der Fels in See und Kies in Quellgrund wandelt!
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalm 114 >