< Job 20 >

1 Da antwortete Sophar von Naama und sprach:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 "Mich bringen die Gedanken wieder auf den gleichen Punkt; mein Eifer wählt in mir.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 Ich höre schmähliche Belehrung; mir antwortet ein Geist, für den ich kein Verständnis habe.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Du weißt das nicht, daß schon von altersher, seit Menschen auf der Erde sind,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 der Frevler Jubel gar nicht lange währt, die Freude des Verruchten höchstens einen Augenblick?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Erhebt er sich bis in den Himmel und streckt sein Haupt bis in die Wolken,
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 mit seinem Unterschlupf verschwindet er für alle Zeit. Die eben ihn gesehen, fragen, wo er sei.
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Traumgleich zerfließt er, ohne Spuren, verschwindet wie ein Nachtgesicht.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 Das Auge, das ihn sah, wird ihn nicht wieder schauen, und seine Heimat sieht ihn nimmer.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Ersatz den Armen seine Kinder leisten; die eignen Hände liefern seine Kinder ab.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Er stand in voller Lebenskraft; nun muß sie mit ihm in den Staub.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Wenn ihm das Böse noch so süß im Munde schmeckt, und birgt er's unter seiner Zunge,
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 und spart er's auf und läßt's nicht los, behält es recht in seinem Gaumen,
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 dann ändert seine Speise sich in seinem Innern, wird Otterngift in seinem Leibe.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Er speit das Gut, das er verschlang; aus seinem Leibe treibt es Gott. -
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 Er saugt der Nattern Gift; der Viper Zunge tötet ihn. -
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 Er labt sich nicht an Strömen, an Bächen voll von Honig und von Milch.
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Er führt zwar sein Erworbenes zum Munde, verschluckt es aber nicht; so, wie's ihm sein Gewinn erlaubt, genießt er's nicht.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Weil er der Armen Hütten eingerissen, so darf er nichts auf dem geraubten Baugrund bauen.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 Er kannte nie für seinen Bauch Zufriedenheit; in seiner Lust bekam er nie genug.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Wen zu verzehren er sich vorgenommen, der ist ihm nicht entgangen; drum ist sein Wohlstand nicht von Dauer.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 In vollem Glück befällt ihn Angst; was Elende an Leid bedrückt, kommt über ihn.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 Wenn er sich anschickt, seinen Leib zu füllen, entsendet gegen ihn er seines Zornes Glut, und macht er sich ans Essen, beschießt er ihn von oben.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 Vom eisernen Geschoß wird er durchbohrt; ihn trifft der eherne Bogen.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 Hinein dringt es und kommt heraus aus seinem Rücken. Ein Strahl von Galle fährt heraus; ein Schrecken lagert sich auf ihn.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 Den Seinigen, die er geborgen glaubt, ist alles Unheil aufgespart. Sie frißt ein Feuer, das von selber brennt. Wer noch in seinem Zelte übrig ist, dem geht es schlimm.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Die Himmel offenbaren seine Schuld; die Erde selbst erhebt sich wider ihn.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Hinschwinden seines Hauses Einkünfte und Ausgaben an seinem Zornestag.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Das ist des Frevlers Los vor Gott, des Widerspenstigen Geschick vom Höchsten."
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Job 20 >