< Job 13 >

1 "So ist's. So hat's mein Auge auch gesehen, mein Ohr vernommen und gemerkt.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Soviel ihr wisset, weiß ich auch; ich falle gegen euch nicht ab.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 Nun will ich mit dem Allerhöchsten reden; mit Gott zu rechten ich begehre.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 Ihr freilich, ihr seid Lügenmeister, unnütze Ärzte insgesamt.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 Wenn ihr nur endlich schweigen wolltet und das für euch zur Weisheit würde!
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Auf meine Widerrede hört! Aufmerket auf den Vorwurf meiner Lippen!
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Wollt ihr für Gott Verkehrtes reden und ihm zuliebe Lügen sprechen?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Wollt ihr für ihn Partei ergreifen, gar Anwalt sein für Gott?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Wenn er euch richtet, geht's dann gut? Wollt ihr ihn narren, wie man Menschen narrt?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Er gibt euch scharfen Tadel, wenn hinterrücks Partei ihr nehmet.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Wird euch nicht seine Hoheit betäuben; befällt euch nicht sein Schrecken?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Zerstäubt sind euere Beweise, und euere Bekräftigungen sind gar tönern.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Vor mir nur schweigt! Denn ich muß reden. Es komme über mich, was wolle!
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Warum soll ich mein Fleisch in meine Zähne nehmen? Ich lege auf die flache Hand mein Leben.
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Ja, mag er mich auch töten; ich zittere nicht davor; auf jeden Fall will ich vor ihm verteidigen meinen Wandel.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 Da muß er selber mir zum Sieg verhelfen; vor ihn kommt ja kein Ruchloser.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Aufmerksam hört auf meine Rede! Ich will's euch selbst beweisen.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Ich lege meinen Rechtsfall vor. Ich weiß gewiß, ich werd's gewinnen.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Kann einer etwas gegen mich beweisen, ich würde schweigend willig sterben.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Nur zweierlei tu mir nicht an! Sonst muß ich mich vor Deinem Antlitz bergen:
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Stell Deine Macht vor mir beiseite! Und Deine Furchtbarkeit erschrecke nimmer mich!
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Dann klage Du, und ich will mich verteidigen. Dann rede ich; Du aber widerlege mich!
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Wie groß ist meine Schuld und mein Vergehen? Mein ganzes Unrecht laß mich wissen!
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Warum birgst Du Dein Angesicht, erachtest mich für Deinen Feind?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Ein welkes Blatt, das schreckst Du auf. Dem dürren Strohhalm jagst Du nach.
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 Du rechnest mir Vergangenes auf und weisest mir die Jugendsünden nach.
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 Du legst mir meine Füße in den Block, verwahrst mir alle Schritte; um meine Fußgelenke ziehst Du einen Ring. -
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 Er aber gleicht dem Wurmfraß, der in Stücke fällt, und einem Kleid, an dem die Motte zehrt."
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Job 13 >