< Tite 3 >

1 Avertis-les d'être soumis aux Principautés et aux Puissances, d'obéir aux Gouverneurs, d'être prêts à faire toute sorte de bonnes actions.
Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino.
2 De ne médire de personne; de n'être point querelleurs, [mais] doux, et montrant toute débonnaireté envers tous les hommes.
Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.
3 Car nous étions aussi autrefois insensés, rebelles, abusés, asservis à diverses convoitises et voluptés, vivant dans la malice et dans l'envie, dignes d'être haïs, et nous haïssant l'un l'autre.
Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake.
4 Mais quand la bonté de Dieu notre Sauveur, et son amour envers les hommes ont été manifestés, il nous a sauvés;
Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera,
5 Non par des œuvres de justice que nous eussions faites, mais selon la miséricorde; par le baptême de la régénération, et le renouvellement du Saint-Esprit;
Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera
6 Lequel il a répandu abondamment en nous par Jésus-Christ notre Sauveur.
amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,
7 Afin qu'ayant été justifiés par sa grâce, nous soyons les héritiers de la vie éternelle selon notre espérance. (aiōnios g166)
kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios g166)
8 Cette parole est certaine, et je veux que tu affirmes ces choses, afin que ceux qui ont cru en Dieu, aient soin les premiers de s'appliquer aux bonnes œuvres; voilà les choses qui sont bonnes et utiles aux hommes.
Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.
9 Mais réprime les folles questions, les généalogies, les contestations et les disputes de la Loi; car elles sont inutiles et vaines.
Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake.
10 Rejette l'homme hérétique, après le premier et le second avertissement.
Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe.
11 Sachant qu'un tel homme est perverti, et qu'il pèche, étant condamné par soi-même.
Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.
12 Quand j'enverrai vers toi Artémas, ou Tychique, hâte-toi de venir vers moi à Nicopolis; car j'ai résolu d'y passer l'hiver.
Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira.
13 Accompagne soigneusement Zénas, Docteur de la Loi, et Apollos, afin que rien ne leur manque.
Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu.
14 Que les nôtres aussi apprennent à être les premiers à s'appliquer aux bonnes œuvres, pour les usages nécessaires, afin qu'ils ne soient point sans fruit.
Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.
15 Tous ceux qui sont avec moi te saluent. Salue ceux qui nous aiment en la foi. Grâce soit avec vous tous, Amen!
Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.

< Tite 3 >