< Hébreux 3 >

1 C'est pourquoi, mes frères saints, qui êtes participants de la vocation céleste, considérez attentivement Jésus-Christ l'Apôtre et le souverain Sacrificateur de notre profession.
Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza.
2 Qui est fidèle à celui qui l'a établi comme Moïse aussi [était fidèle] en toute sa maison.
Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu.
3 Or Jésus-Christ a été jugé digne d'une gloire d'autant plus grande que celle de Moïse, que celui qui a bâti la maison, est d'une plus grande dignité que la maison même.
Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo.
4 Car toute maison est bâtie par quelqu'un: or celui qui a bâti toutes ces choses, c'est Dieu.
Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu.
5 Et quant à Moïse, il a bien été fidèle dans toute la maison de Dieu, comme serviteur, pour témoigner des choses qui devaient être dites;
Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo.
6 Mais Christ comme Fils est sur sa maison; et nous sommes sa maison, pourvu que nous retenions ferme jusques à la fin l'assurance, et la gloire de l'espérance.
Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.
7 C'est pourquoi, comme dit le Saint-Esprit: aujourd'hui, si vous entendez sa voix,
Tsono monga Mzimu Woyera akuti, “Lero mukamva mawu ake,
8 N'endurcissez point vos cœurs, comme [il arriva] dans [le lieu de] l'irritation, au jour de la tentation au désert:
musawumitse mitima yanu ngati munachitira pamene munawukira, pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.
9 Où vos pères m'ont tenté et m'ont éprouvé, et [où] ils ont vu mes œuvres durant quarante ans.
Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa, ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.
10 C'est pourquoi j'ai été ennuyé de cette génération, et j'ai dit: leur cœur s'égare toujours et ils n'ont point connu mes voies.
Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo, ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera, ndipo iwo sadziwa njira zanga.’
11 Aussi j'ai juré en ma colère: si [jamais] ils entrent en mon repos.
Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti, ‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’”
12 Mes frères, prenez garde qu'il n'y ait en quelqu'un de vous un mauvais cœur d'incrédulité, pour se révolter du Dieu vivant.
Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo.
13 Mais exhortez-vous l'un l'autre chaque jour, pendant que ce jour nous éclaire; de peur que quelqu'un de vous ne s'endurcisse par la séduction du péché.
Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo.
14 Car nous avons été faits participants de Christ, pourvu que nous retenions ferme jusqu'à la fin le commencement de notre subsistance.
Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi.
15 Pendant qu'il est dit: aujourd'hui si vous entendez sa voix n'endurcissez point vos cœurs, comme il [arriva] dans [le lieu de] l'irritation.
Monga kunanenedwa kuti, “Lero ngati mumva mawu ake, musawumitse mitima yanu ngati momwe munachitira pamene munawukira.”
16 Car quelques-uns l'ayant entendue, le provoquèrent à la colère; mais ce ne furent pas tous ceux qui étaient sortis d'Egypte par Moïse.
Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto?
17 Mais desquels fut-il ennuyé durant quarante ans? ne fut-ce pas de ceux qui péchèrent, et dont les corps tombèrent dans le désert?
Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja?
18 Et auxquels jura-t-il qu'ils n'entreraient point en son repos, sinon à ceux qui furent rebelles?
Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja.
19 Ainsi nous voyons qu'ils n'y purent entrer à cause de leur incrédulité.
Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

< Hébreux 3 >