< Hébreux 4 >

1 Craignons donc que quelqu'un d'entre vous négligeant la promesse d'entrer dans son repos ne s'en trouve privé:
Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo.
2 Car il nous a été évangélisé, comme [il le fut] à ceux-là; mais la parole de la prédication ne leur servit de rien, parce qu'elle n'était point mêlée avec la foi dans ceux qui l'ouïrent.
Pakuti Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa ife, monganso iwo aja; koma iwo sanapindule nawo uthengawo chifukwa anangomva koma osakhulupirira.
3 Mais pour nous qui avons cru, nous entrerons dans le repos, suivant ce qui a été dit: c'est pourquoi j'ai juré en ma colère, si [jamais] ils entrent en mon repos; quoique ses ouvrages fussent déjà achevés dès la fondation du monde.
Tsono ife amene takhulupirira talowa mu mpumulo, monga momwe Mulungu akunenera kuti, “Ndili wokwiya ndinalumbira kuti, ‘Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.’” Ananena zimenezi ngakhale anali atatsiriza kale ntchito yolenga dziko lapansi.
4 Car il a été dit ainsi en quelque lieu touchant le septième [jour]: Et Dieu se reposa de tous ses ouvrages au septième jour.
Pena pake wayankhula za tsiku lachisanu ndi chiwiri mʼmawu awa: “Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, Mulungu anapumula ku ntchito zake zonse.”
5 Et encore en ce passage: Si [jamais] ils entrent en mon repos.
Pa ndime inonso akunena za zomwezo pamene akuti, “Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.”
6 Puis donc qu'il reste que quelques-uns y entrent, et que ceux à qui premièrement il a été évangélisé n'y sont point entrés, à cause de leur incrédulité,
Popeza kwatsalabe kuti ena adzalowe mu mpumulowo, koma aja anayamba kumva Uthenga Wabwino sanalowe chifukwa cha kusamvera kwawo.
7 [Dieu] détermine encore un certain jour, [qu'il appelle] aujourd'hui, en disant par David si longtemps après, selon ce qui a été dit: aujourd'hui, si vous entendez sa voix, n'endurcissez point vos cœurs.
Nʼchifukwa chake Mulungu anayikanso tsiku lina limene analitcha “Lero.” Patapita nthawi yayitali Iye anayankhula za tsiku lomweli kudzera mwa Davide, monga ndinanena kale kuti, “Lero mukamva mawu ake, musawumitse mitima yanu.”
8 Car si Josué les eût introduits dans le repos, jamais après cela il n'eût parlé d'un autre jour.
Ngati Yoswa akanalowetsa anthu mu mpumulo, Mulungu sakananena pambuyo pake za tsiku lina.
9 Il reste donc un repos pour le peuple de Dieu.
Kotero tsono kwatsala mpumulo wa Sabata kwa anthu a Mulungu;
10 Car celui qui est entré en son repos, s'est reposé aussi de ses œuvres, comme Dieu [s'était reposé] des siennes.
Pakuti aliyense amene analowa mu mpumulo wa Mulungu anapuma pa ntchito zake, monga momwe Mulungu anachitira.
11 Etudions-nous donc d'entrer dans ce repos-là, de peur que quelqu'un ne tombe en imitant une semblable incrédulité.
Tiyeni tsono tiyesetse kulowa mu mpumulo, kuti pasapezeke wina aliyense wolephera potsatira chitsanzo chawo cha kusamvera.
12 Car la Parole de Dieu est vivante et efficace, et plus pénétrante que nulle épée à deux tranchants, et elle atteint jusques à la division de l'âme, de l'esprit, des jointures et des mœlles, et elle est juge des pensées et des intentions du cœur.
Paja Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amalowa mpaka molumikizirana moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana fundo ndi mafuta a mʼmafupa. Amaweruza malingaliro ndi zokhumba za mʼmitima.
13 Et il n'y a aucune créature qui soit cachée devant lui: mais toutes choses sont nues et entièrement ouvertes aux yeux de celui devant lequel nous avons affaire.
Palibe kanthu kobisika pamaso pa Mulungu. Zinthu zonse zili poyera ndi zovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.
14 Puis donc que nous avons un souverain et grand Sacrificateur, Jésus Fils de Dieu, qui est entré dans les Cieux, tenons ferme [notre] profession.
Popeza kuti tili ndi Mkulu wa ansembe wopambana, amene analowa kale kumwamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tiyeni tigwiritsitse chikhulupiriro chathu chimene timavomereza.
15 Car nous n'avons pas un souverain Sacrificateur qui ne puisse avoir compassion de nos infirmités, mais [nous avons celui] qui a été tenté comme nous en toutes choses, excepté le péché.
Pakuti sitili ndi Mkulu wa ansembe amene sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofowoka zathu. Koma tili naye amene anayesedwa mʼnjira zonse monga ife, koma sanachimwe.
16 Allons donc avec assurance au trône de la Grâce; afin que nous obtenions miséricorde, et que nous trouvions grâce, pour être aidés dans le besoin.
Tiyeni tsono tiyandikire ku mpando waufumu, wachisomo mopanda mantha, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo chotithandiza pa nthawi yeniyeni.

< Hébreux 4 >