< Luc 20 >

1 Et il arriva un de ces jours-là, comme il enseignait le peuple dans le Temple, et qu'il évangélisait, que les principaux Sacrificateurs et les Scribes survinrent avec les Anciens.
Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
2 Et ils lui parlèrent, en disant: dis-nous par quelle autorité tu fais ces choses, ou qui est celui qui t'a donné cette autorité?
Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
3 Et Jésus répondant leur dit: je vous interrogerai aussi sur un article, et répondez-moi.
Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
4 Le Baptême de Jean était-il du ciel, ou des hommes?
‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
5 Or ils disputaient entre eux, disant: si nous disons: du ciel; il dira: pourquoi donc ne l'avez-vous point cru?
Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
6 Et si nous disons: des hommes, tout le peuple nous lapidera; car ils sont persuadés que Jean était un Prophète;
Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
7 C'est pourquoi ils répondirent qu'ils ne savaient d'où il était.
Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
8 Et Jésus leur dit: je ne vous dirai point aussi par quelle autorité je fais ces choses.
Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
9 Alors il se mit à dire au peuple cette parabole: Un homme planta une vigne, et la loua à des vignerons, et fut longtemps dehors.
Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
10 Et dans la saison [du fruit], il envoya un serviteur vers les vignerons, afin qu'ils lui donnassent du fruit de la vigne, mais les vignerons l'ayant battu, le renvoyèrent à vide.
Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
11 Il leur envoya encore un autre serviteur; mais ils le battirent aussi, et après l'avoir traité indignement, ils le renvoyèrent à vide.
Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
12 Il en envoya encore un troisième, mais ils le blessèrent aussi, et le jetèrent dehors.
Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
13 Alors le seigneur de la vigne dit: que ferai-je? j'y enverrai mon fils, le bien aimé; peut-être que quand ils le verront, ils le respecteront.
“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
14 Mais quand les vignerons le virent, ils raisonnèrent entre eux, en disant: celui-ci est l'héritier; venez, tuons-le, afin que l'héritage soit à nous.
“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
15 Et ils le jetèrent hors de la vigne, et le tuèrent. Que leur fera donc le maître de la vigne?
Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
16 Il viendra, et fera périr ces vignerons-là, et il donnera la vigne à d'autres. Ce qu'eux ayant entendu, ils dirent: à Dieu ne plaise!
Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
17 Alors il les regarda, et dit: que veut donc dire ce qui est écrit: la pierre que ceux qui bâtissent ont rejetée, est devenue la maîtresse pierre du coin?
Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
18 Quiconque tombera sur cette pierre, sera brisé; et elle écrasera celui sur qui elle tombera.
Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
19 Les principaux Sacrificateurs et les Scribes cherchèrent dans ce même instant à mettre les mains sur lui: car ils connurent bien qu'il avait dit cette parabole contre eux, mais ils craignirent le peuple.
Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
20 Et l'observant ils envoyèrent des gens concertés, qui contrefaisaient les gens de bien, pour le surprendre en paroles, afin de le livrer à la domination et à la puissance du Gouverneur,
Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
21 Lesquels l'interrogèrent, en disant: Maître, nous savons que tu parles et que tu enseignes conformément à la justice, et que tu ne regardes point à l'apparence des personnes, mais que tu enseignes la voie de Dieu en vérité.
Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
22 Nous est-il permis de payer le tribut à César, ou non?
Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
23 Mais lui ayant aperçu leur ruse, leur dit: pourquoi me tentez-vous?
Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
24 Montrez-moi un denier; de qui a-t-il l'image et l'inscription? ils lui répondirent: de César.
“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
25 Et il leur dit: rendez donc à César les choses qui sont à César; et à Dieu les choses qui sont à Dieu.
Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
26 Ainsi ils ne purent rien trouver à redire dans sa réponse en présence du peuple; mais tout étonnés de sa réponse, ils se turent.
Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
27 Alors quelques-uns des Sadducéens, qui nient formellement la résurrection, s'approchèrent, et l'interrogèrent,
Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
28 Disant: Maître, Moïse nous a laissé par écrit, que si le frère de quelqu'un est mort ayant une femme, et qu'il soit mort sans enfants, son frère prenne sa femme, et qu'il suscite des enfants à son frère.
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
29 Or il y eut sept frères, dont l'aîné prit une femme, et mourut sans enfants.
Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
30 Et le second la prit, et mourut aussi sans enfants.
Wachiwiri
31 Puis le troisième la prit, et de même tous les sept; et ils moururent sans avoir laissé des enfants.
ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
32 Et après tous la femme aussi mourut.
Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
33 Duquel d'eux donc sera-t-elle femme en la résurrection? car les sept l'ont eue pour femme.
Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
34 Et Jésus répondant leur dit: les enfants de ce siècle prennent et sont pris en mariage. (aiōn g165)
Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn g165)
35 Mais ceux qui seront faits dignes d'obtenir ce siècle-là et la résurrection des morts, ne prendront ni ne seront pris en mariage; (aiōn g165)
Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn g165)
36 Car ils ne pourront plus mourir, parce qu'ils seront semblables aux Anges, et qu'ils seront fils de Dieu, étant fils de la résurrection.
Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
37 Or que les morts ressuscitent, Moïse même l'a montré auprès du buisson, quand il appelle le Seigneur le Dieu d'Abraham, et le Dieu d'Isaac, et le Dieu de Jacob.
Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
38 Or il n'est point le Dieu des morts, mais des vivants: car tous vivent en lui.
Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
39 Et quelques-uns des Scribes prenant la parole, dirent: Maître, tu as bien dit.
Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
40 Et ils ne l'osèrent plus interroger de rien.
Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
41 Mais lui leur dit: comment dit-on que le Christ est Fils de David.
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
42 Car David lui-même dit au Livre des Psaumes: le Seigneur a dit à mon Seigneur: assieds-toi à ma droite,
Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
43 Jusqu'à ce que j'aie mis tes ennemis pour le marchepied de tes pieds.
mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
44 [Puis] donc que David l'appelle [son] Seigneur, comment, est-il son Fils?
Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
45 Et comme tout le peuple écoutait, il dit à ses Disciples:
Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
46 Donnez-vous garde des Scribes, qui se plaisent à se promener en robes longues, et qui aiment les salutations dans les marchés, et les premières chaires dans les Synagogues, et les premières places dans les festins;
“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
47 Et qui dévorent entièrement les maisons des veuves, même sous prétexte de faire de longues prières; car ils en recevront une plus grande condamnation.
Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”

< Luc 20 >