< Jean 19 >

1 Pilate fit donc alors prendre Jésus, et le fit fouetter.
Kenaka Pilato anatenga Yesu namukwapula mwankhanza.
2 Et les soldats firent une couronne d'épines qu'ils mirent sur sa tête, et le vêtirent d'un vêtement de pourpre.
Asilikali analuka nkhata yaminga ndi kumuveka pamutu pake. Kenaka anamuveka mkanjo wapepo
3 Puis ils lui disaient: Roi des Juifs, nous te saluons; et ils lui donnaient des coups avec leurs verges.
ndipo ankapita kwa Iye mobwerezabwereza ndi kumanena kuti, “Moni mfumu ya Ayuda?” Ndipo amamumenya makofi.
4 Et Pilate sortit encore dehors, et leur dit: voici, je vous l'amène dehors, afin que vous sachiez que je ne trouve aucun crime en lui.
Pilato anatulukanso ndipo anati kwa Ayuda, “Taonani, ine ndikumubweretsa kuti inu mudziwe kuti ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.”
5 Jésus donc sortit portant la couronne d'épines, et le vêtement de pourpre; et Pilate leur dit: voici l'homme.
Pamenepo Yesu anatuluka atavala nkhata yaminga ndi mkanjo wapepo ndipo Pilato anawawuza kuti, “Nayu munthu uja!”
6 Mais quand les principaux Sacrificateurs et leurs huissiers le virent, ils s'écrièrent, en disant: crucifie, crucifie. Pilate leur dit: prenez-le vous-mêmes, et le crucifiez: car je ne trouve point de crime en lui.
Atangomuona Iye akulu a ansembe ndi akuluakulu ena anafuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!” Koma Pilato anayankha kuti, “Inu mutengeni ndi kumupachika. Koma ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.”
7 Les Juifs lui répondirent: nous avons une loi, et selon notre loi il doit mourir, car il s'est fait Fils de Dieu.
Ayuda anayimirira nati, “Ife tili ndi lamulo, ndipo molingana ndi lamulolo, Iyeyu ayenera kuphedwa chifukwa akudzitcha kuti ndi Mwana wa Mulungu.”
8 Or quand Pilate eut ouï cette parole, il craignit encore davantage.
Pilato atamva zimenezi, anachita mantha kwambiri,
9 Et il rentra dans le Prétoire, et dit à Jésus: d'où es-tu? Mais Jésus ne lui donna point de réponse.
ndipo anabwereranso mʼnyumba yaufumu. Iye anafunsa Yesu kuti, “Kodi umachokera kuti?” Koma Yesu sanayankhe.
10 Et Pilate lui dit: ne me parles-tu point? ne sais-tu pas que j'ai le pouvoir de te crucifier, et le pouvoir de te délivrer?
Pilato anati, “Kodi ukukana kundiyankhula ine? Kodi sukuzindikira kuti ine ndili ndi mphamvu yokumasula ndiponso mphamvu yokupachika?”
11 Jésus lui répondit: tu n'aurais aucun pouvoir sur moi, s'il ne t'était donné d'en haut; c'est pourquoi celui qui m'a livré à toi, a fait un plus grand péché.
Yesu anayankha kuti, “Inu simukanakhala ndi mphamvu pa Ine akanapanda kukupatsani kumwamba. Nʼchifukwa chake amene wandipereka Ine kwa inu ndiye wochimwa kwambiri.”
12 Depuis cela Pilate tâchait à le délivrer; mais les Juifs criaient, en disant: si tu délivres celui-ci tu n'es point ami de César; car quiconque se fait Roi, est contraire à César.
Kuyambira pamenepo Pilato anayesa kuti amumasule Yesu, koma Ayuda anapitirira kufuwula kuti, “Ngati mumumasula munthuyu kuti apite, inu si bwenzi la Kaisara.”
13 Quand Pilate eut ouï cette parole, il amena Jésus dehors, et s'assit au Siège judicial, dans le lieu qui est appelé [le Pavé], et en Hébreu Gabbatha.
Pilato atamva zimenezi, iye anamutulutsa Yesu kunja ndi kukhala pansi pa mpando wa woweruza pamalo otchedwa Mwala Wowaka (umene pa Chiaramaiki ndi Gabata).
14 Or c'était la préparation de la Pâque, et [il était] environ six heures; et [Pilate] dit aux Juifs: voilà votre Roi.
Linali tsiku lokonzekera Sabata la Paska ndipo nthawi inali ora lachisanu ndi chimodzi masana. Pilato anati kwa Ayuda, “Nayi mfumu yanu.”
15 Mais ils criaient: ôte, ôte, crucifie-le. Pilate leur dit: crucifierai-je votre Roi? Les principaux Sacrificateurs répondirent: nous n'avons point d'autre Roi que César.
Koma iwo anafuwula kuti, “Choka nayeni! Choka nayeni! Mpachikeni!” Pilato anafunsa kuti, “Kodi ine ndipachike mfumu yanuyi?” Akulu a ansembe anayankha kuti, “Ife tilibe mfumu ina koma Kaisara.”
16 Alors donc il le leur livra pour être crucifié. Ils prirent donc Jésus, et l'emmenèrent.
Pomaliza Pilato anamupereka kwa iwo kuti akapachikidwe. Choncho asilikali anamutenga Yesu.
17 Et [Jésus] portant sa croix, vint au lieu appelé le Calvaire, et en Hébreu Golgotha;
Atanyamula mtanda wake, anapita kumalo otchedwa “Malo a Bade” (mʼChiaramaiki amatchedwa Gologota).
18 Où ils le crucifièrent, et deux autres avec lui, un de chaque côté, et Jésus au milieu.
Pamenepo iwo anamupachika Iye pamodzi ndi anthu ena awiri, mmodzi mbali ina ndi wina mbali inanso ndipo Yesu pakati.
19 Or Pilate fit un écriteau, qu'il mit sur la croix, où étaient écrits ces mots: JESUS NAZARIEN LE ROI DES JUIFS.
Pilato analemba chikwangwani chomwe anachikhoma pa mtandapo. Panalembedwa mawu akuti, yesu wa ku nazareti, mfumu ya ayuda.
20 Et plusieurs des Juifs lurent cet écriteau, parce que le lieu où Jésus était crucifié, était près de la ville; et cet écriteau était en Hébreu, en Grec, [et] en Latin.
Ayuda ambiri anawerenga chikwangwanichi, pakuti pamalo pamene Yesu anapachikidwapo panali pafupi ndi mzinda ndipo chikwangwanicho chinalembedwa mu Chiaramaiki, Chilatini ndi Chigriki.
21 C'est pourquoi les principaux Sacrificateurs des Juifs dirent à Pilate: n'écris point, le Roi des Juifs; mais, que celui-ci a dit: je suis le Roi des Juifs.
Kenaka mkulu wa ansembe wa Ayuda anakadandaula kwa Pilato nati, “Musalembe kuti ‘Mfumu ya Ayuda,’ koma kuti munthuyu amadzitcha kuti ndi mfumu ya Ayuda.”
22 Pilate répondit: ce que j'ai écrit, je l'ai écrit.
Pilato anayankha kuti, “Chimene ine ndalemba, ndalemba.”
23 Or quand les soldats eurent crucifié Jésus, ils prirent ses vêtements, et en firent quatre parts, une part pour chaque soldat; [ils prirent] aussi la tunique; mais elle était sans couture, tissue depuis le haut jusqu'en bas.
Asilikali atamupachika Yesu, anatenga zovala zake ndi kuzigawa zigawo zinayi, gawo limodzi la aliyense wa iwo, ndi kutsala mwinjiro wamʼkati wokha. Chovala ichi chinawombedwa kuyambira pamwamba mpaka pansi wopanda msoko.
24 Et ils dirent entre eux: ne la mettons point en pièces, mais jetons-la au sort, [pour savoir] à qui elle sera. Et [cela arriva ainsi], afin que l'Ecriture fût accomplie, disant: ils ont partagé entre eux mes vêtements, et ils ont jeté au sort ma robe; les soldats donc firent ces choses.
Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni tisachingʼambe koma tichite maere kuti tione amene achitenge.” Izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe amene anati, “Iwo anagawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.” Choncho izi ndi zimene asilikali anachita.
25 Or près de la croix de Jésus étaient sa mère, et la sœur de sa mère, [savoir] Marie [femme] de Cléopas, et Marie Magdelaine.
Pafupi ndi mtanda wa Yesu panayima amayi ake, mngʼono wa amayi ake, Mariya mkazi wa Kaliyopa ndi Mariya wa ku Magadala.
26 Et Jésus voyant sa mère, et auprès d'elle le Disciple qu'il aimait, il dit à sa mère: femme, voilà ton Fils.
Yesu ataona amayi ake pamenepo ndi wophunzira amene Iye anamukonda atayima pafupipo, Iye anati kwa amayi ake, “Amayi nayu mwana wanu.”
27 Puis il dit au Disciple: voilà ta Mère; et dès cette heure-là ce Disciple la reçut chez lui.
Anawuzanso wophunzirayo kuti, “Nawa amayi ako.” Kuyambira nthawi imeneyo, wophunzirayo anatenga amayiwo kupita nawo kwawo.
28 Après cela Jésus sachant que toutes choses étaient déjà accomplies, il dit, afin que l'Ecriture fût accomplie: j'ai soif.
Atadziwa kuti zonse zatha tsopano komanso kuti malemba akwaniritsidwe, Yesu anati, “Ine ndili ndi ludzu.”
29 Et il y avait là un vase plein de vinaigre, ils emplirent donc de vinaigre une éponge, et la mirent au bout d'une branche d'hysope, et la lui présentèrent à la bouche.
Pomwepo panali mtsuko wodzaza ndi vinyo wosasa, choncho iwo ananyika chinkhupule ndi kuchisomeka ku mtengo wa hisope nachifikitsa kukamwa kwa Yesu.
30 Et quand Jésus eut pris le vinaigre, il dit: tout est accompli; et ayant baissé la tête, il rendit l'esprit.
Yesu atalandira chakumwachi anati, “Kwatha.” Ndipo Iye anaweramitsa mutu wake napereka mzimu wake.
31 Alors les Juifs, afin que les corps ne demeurassent point en croix au jour du Sabbat, parce que c'était la préparation, (or c'était un grand jour du Sabbat) prièrent Pilate qu'on leur rompît les jambes, et qu'on les ôtât.
Popeza linali Tsiku Lokonzekera ndipo tsiku linalo linali Sabata lapadera; Ayuda sanafune kuti mitembo ikhale pa mtanda pa Sabata, iwo anapempha Pilato kuti akathyole miyendo ndi kutsitsa mitemboyo.
32 Les soldats donc vinrent, et rompirent les jambes au premier, et de même à l'autre qui était crucifié avec lui.
Chifukwa chake asilikali anabwera ndi kuthyola miyendo ya munthu oyamba amene anapachikidwa ndi Yesu ndipo kenaka ya winayo.
33 Puis étant venus à Jésus, et voyant qu'il était déjà mort, ils ne lui rompirent point les jambes;
Koma atafika pa Yesu ndi kupeza kuti anali atamwalira kale, iwo sanathyole miyendo yake.
34 Mais un des soldats lui perça le côté avec une lance, et d'abord il en sortit du sang et de l'eau.
Mʼmalo mwake, mmodzi wa asilikaliwo anamubaya Yesu ndi mkondo mʼnthiti, ndipo nthawi yomweyo munatuluka magazi ndi madzi.
35 Et celui qui l'a vu, l'a témoigné, et son témoignage est digne de foi; et celui-là sait qu'il dit vrai, afin que vous le croyiez.
Munthu amene anaona izi wapereka umboni ndipo umboni wake ndi woona. Iye akudziwa kuti akunena choonadi kuti inunso mukhulupirire.
36 Car ces choses-là sont arrivées afin que cette Ecriture fût accomplie: pas un de ses os ne sera cassé.
Zinthu izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe: “Palibe limodzi la mafupa limene lidzathyoledwa,”
37 Et encore une autre Ecriture, qui dit: ils verront celui qu'ils ont percé.
ndi monga lemba linanso linena, “Iwo adzayangʼana Iye amene iwo anamubaya.”
38 Or après ces choses, Joseph d'Arimathée, qui était Disciple de Jésus, secret toutefois parce qu'il craignait les Juifs, pria Pilate qu'il lui permît d'ôter le corps de Jésus; et Pilate le lui ayant permis, il vint, et prit le corps de Jésus.
Kenaka, Yosefe wa ku Arimateyu anakapempha mtembo wa Yesu kwa Pilato. Tsono Yosefe anali wophunzira wa Yesu koma mobisa chifukwa iye ankaopa Ayuda. Atalandira chilolezo kwa Pilato, anakatsitsa mtembo wa Yesu.
39 Nicodème aussi, celui qui auparavant était allé de nuit à Jésus, y vint apportant une mixtion de myrrhe et d'aloès d'environ cent livres.
Nekodimo, munthu amene poyamba pake anabwera kwa Yesu usiku, anatenga mafuta osakaniza ndi mure ndi aloe wolemera pafupifupi makilogalamu 32.
40 Et ils prirent le corps de Jésus, et l'enveloppèrent de linges avec des Aromates, comme les Juifs ont coutume d'ensevelir.
Pamenepo anatenga mtembo wa Yesu nawukulunga pamodzi ndi zonunkhiritsa mu nsalu za mtundu woyera monga mwa mwambo wa maliro wa Ayuda.
41 Or il y avait au lieu où il fut crucifié un jardin, et dans le jardin un sépulcre neuf, où personne n'avait encore été mis.
Pamalo pamene anapachikidwa Yesu panali munda ndipo mʼmundamo munali manda atsopano mʼmene munali simunayikidwemo aliyense.
42 Et ils mirent là Jésus, à cause de la préparation des Juifs, parce que le sépulcre était près.
Chifukwa linali Tsiku la Ayuda Lokonzekera ndi kuti mandawo anali pafupipo, iwo anayika Yesu mʼmenemo.

< Jean 19 >