< Jacques 5 >

1 Or maintenant, vous riches, pleurez, et poussez de grands cris à cause des malheurs, qui s’en vont tomber sur vous.
Tsono tamverani, inu anthu achuma, lirani ndi kufuwula chifukwa cha zovuta zimene zidzakugwereni.
2 Vos richesses sont pourries; vos vêtements sont rongés par les vers.
Chuma chanu chawola ndipo njenjete zadya zovala zanu.
3 Votre or et votre argent sont rouillés, et leur rouille sera en témoignage [contre] vous, et dévorera votre chair comme le feu; vous avez amassé un trésor pour les derniers jours.
Golide ndi siliva wanu zachita dzimbiri. Dzimbirilo lidzakhala umboni wokutsutsani ndi kuwononga mnofu wanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano otsiriza.
4 Voici, le salaire des ouvriers qui ont moissonné vos champs, [et] duquel ils ont été frustrés par vous, crie; et les cris de ceux qui ont moissonné, sont parvenus aux oreilles du Seigneur des armées.
Taonani, ndalama za malipiro zimene munakanika kulipira aganyu aja ankasenga mʼmunda mwanu zikulira mokutsutsani. Kulira kwa okololawo kwamveka mʼmakutu mwa Ambuye Wamphamvuzonse.
5 Vous avez vécu dans les délices sur la terre, vous vous êtes livrés aux voluptés, [et] vous avez rassasié vos cœurs comme en un jour de sacrifices.
Mwakhala pa dziko lapansi pano moyo ofewa ndipo mwalidyera dziko lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lokaphedwa.
6 Vous avez condamné, [et] mis à mort le juste, [qui] ne vous résiste point.
Mwaweruza kuti ndi wolakwa ndipo mwapha munthu wosalakwa, amene sakutsutsana nanu.
7 Or donc, mes frères, attendez patiemment jusqu'à la venue du Seigneur; voici, le laboureur attend le fruit précieux de la terre, patientant, jusqu'à ce qu'il reçoive la pluie de la première, et de la dernière saison.
Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza.
8 Vous [donc] aussi attendez patiemment, [et] affermissez vos cœurs; car la venue du Seigneur est proche.
Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera.
9 Mes frères, ne vous plaignez point les uns des autres, afin que vous ne soyez point condamnés; voilà, le juge se tient à la porte.
Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!
10 Mes frères, prenez pour un exemple d'affliction et de patience les Prophètes qui ont parlé au Nom du Seigneur.
Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira.
11 Voici, nous tenons pour bienheureux ceux qui ont souffert; vous avez appris [quelle a été] la patience de Job, et vous avez vu la fin du Seigneur; car le Seigneur est plein de compassion, et pitoyable.
Monga mukudziwa, tinawatenga ngati odalitsika anthu amene anapirira. Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mwaona zimene Ambuye anamuchitira potsiriza pake. Ambuye ndi wodzaza ndi chisoni ndi chifundo.
12 Or sur toutes choses, mes frères, ne jurez ni par le Ciel, ni par la terre, ni par quelque autre serment; mais que votre oui soit Oui, et votre non, Non: afin que vous ne tombiez point dans la condamnation.
Koposa zonse, abale anga, musamalumbire. Polumbira osamatchula kumwamba kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. “Inde” wanu azikhala “Inde,” ndipo “Ayi” wanu azikhala “Ayi,” kuopa kuti mungadzapezeke olakwa.
13 y a-t-il quelqu'un parmi vous qui souffre? qu'il prie. Y en a-t-il quelqu'un qui ait l'esprit content? qu'il psalmodie.
Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Ayimbe nyimbo zolemekeza.
14 Y a-t-il quelqu'un parmi vous qui soit malade? qu’il appelle les Anciens de l'Eglise, et qu'ils prient pour lui, et qu'ils l’oignent d'huile au Nom du Seigneur.
Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye.
15 Et la prière faite avec foi sauvera le malade, et le Seigneur le relèvera; et s'il a commis des péchés, ils lui seront pardonnés.
Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa.
16 Confessez vos fautes l'un à l'autre, et priez l'un pour l'autre; afin que vous soyez guéris; car la prière du juste faite avec véhémence est de grande efficace.
Choncho, ululiranani machimo anu ndi kupemphererana wina ndi mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama ndi lamphamvu ndipo limagwira ntchito.
17 Elie était un homme sujet à de semblables infirmités que nous, et cependant ayant prié avec grande instance qu'il ne plût point, il ne tomba point de pluie sur la terre durant trois ans et six mois.
Eliya anali munthu ngati ife. Iye anapemphera mwamphamvu kuti mvula isagwe ndipo sinagwedi kwa zaka zitatu ndi theka.
18 Et ayant encore prié, le Ciel donna de la pluie, et la terre produisit son fruit.
Kenaka anapempheranso, ndipo kumwamba kunagwetsa mvula, ndipo dziko lapansi linatulutsa zomera zake.
19 Mes frères, si quelqu'un d'entre vous s'égare de la vérité, et que quelqu'un l'y ramène;
Abale anga, ngati mmodzi wa inu apatuka pa choonadi ndipo wina wake ndi kumubweza,
20 Qu'il sache que celui qui aura ramené un pécheur de son égarement, sauvera une âme de la mort, et couvrira une multitude de péchés.
kumbukirani izi: Aliyense wobweza wochimwa kuchoka ku cholakwa chake, adzamupulumutsa ku imfa ndi kukwirira machimo ambiri.

< Jacques 5 >