< Jacques 4 >

1 D'où viennent parmi vous les disputes et les querelles? n'est-ce point de vos voluptés, qui combattent dans vos membres?
Nʼchiyani chimene chimayambitsa ndewu ndi mapokoso pakati panu? Kodi sizichokera ku zilakolako zimene zimalimbana mʼkati mwanu?
2 Vous convoitez, et vous n'avez point [ce que vous désirez]; vous avez une envie mortelle, vous êtes jaloux, et vous ne pouvez obtenir [ce que vous enviez]; vous vous querellez, et vous disputez, et vous n'avez point [ce que vous désirez], parce que vous ne le demandez point.
Mumalakalaka zinthu koma simuzipeza, choncho mumapha. Mumasirira zinthu koma simutha kuzipeza zimene mukufuna, choncho mumakangana ndi kumenyana. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.
3 Vous demandez, et vous ne recevez point; parce que vous demandez mal, [et] afin de l'employer dans vos voluptés.
Koma ngakhale mumapempha simulandira, chifukwa mumapempha ndi zolinga zoyipa. Mumapempha kuti muzigwiritse ntchito pa zokusangalatsani nokha.
4 Hommes et femmes adultères, ne savez-vous pas que l'amitié du monde est inimitié contre Dieu? celui donc qui voudra être ami du monde, se rend ennemi de Dieu.
Inu anthu achigololo, kodi simukudziwa kuti kuchita ubwenzi ndi dziko lapansi ndi kudana ndi Mulungu? Choncho, aliyense wosankha kukhala bwenzi la dziko lapansi amasanduka mdani wa Mulungu.
5 Pensez-vous que l'Ecriture parle en vain; l'Esprit qui a habité en nous, vous inspire-t-il l'envie?
Kapena mukuganiza kuti Malemba amanena popanda chifukwa kuti Mulungu amafunitsitsa mwansanje mzimu umene Iye anayika kuti uzikhala mwa ife?
6 Il vous donne au contraire une plus grande grâce; c'est pourquoi [l'Ecriture] dit: Dieu résiste aux orgueilleux, mais il fait grâce aux humbles.
Koma amatipatsa chisomo chochuluka. Nʼchifukwa chake Malemba amati, “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma apereka chisomo kwa odzichepetsa.”
7 Soumettez-vous donc à Dieu. Résistez au Démon, et il s'enfuira de vous.
Dziperekeni nokha kwa Mulungu. Mukaneni Mdierekezi ndipo adzakuthawani.
8 Approchez-vous de Dieu, et il s'approchera de vous; pécheurs, nettoyez vos mains; et vous qui êtes doubles de cœur, purifiez vos cœurs.
Sendezani kufupi ndi Mulungu ndipo Iye adzasendeza kwa inu. Sambani mʼmanja mwanu, inu anthu ochimwa. Yeretsani mitima yanu, inu anthu okayikira.
9 Sentez vos misères, et lamentez, et pleurez; que votre ris se change en pleurs, et votre joie en tristesse.
Chitani chisoni chifukwa cha zimene mwachita, lirani misozi. Kuseka kwanu kusanduke kulira, ndipo chimwemwe chanu chisanduke chisoni.
10 Humiliez-vous en la présence du Seigneur, et il vous élèvera.
Dzichepetseni pamaso pa Ambuye ndipo Iye adzakukwezani.
11 Mes frères ne médisez point les uns des autres; celui qui médit de son frère, et qui condamne son frère, médit de la Loi, et condamne la Loi; or si tu condamnes la Loi, tu n'es point l'observateur de la Loi, mais le juge.
Abale musamanenane. Aliyense wonenera zoyipa mʼbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo. Pamene muweruza malamulo, ndiye kuti simukusunga malamulowo, koma mukuwaweruza.
12 Il n'y a qu'un seul Législateur, qui peut sauver et qui peut perdre; [mais] toi qui es-tu, qui condamnes les autres?
Pali mmodzi yekha Wopereka Malamulo ndi Woweruza. Ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuwononga. Kodi ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?
13 Or maintenant, vous qui dites: Allons aujourd'hui ou demain en une telle ville, et demeurons là un an, et y trafiquons et gagnons;
Tsono tamverani, inu amene mumati, “Lero kapena mawa tipita ku mzinda wakutiwakuti, tikatha chaka chimodzi tikuchita malonda ndi kupanga ndalama.”
14 (Qui toutefois ne savez pas ce qui arrivera le lendemain car qu'est-ce que votre vie? ce n'est certes qu'une vapeur qui parait pour un peu de temps, et qui ensuite s'évanouit; )
Chifukwa chiyani mukutero? Inu simukudziwa zimene ziti zichitike mawa. Kodi moyo wanu ndi wotani? Inu muli ngati nkhungu imene imangooneka kwa kanthawi kochepa ndipo kenaka ndikuzimirira.
15 Au lieu que vous deviez dire: si le Seigneur le veut, et si nous vivons, nous ferons ceci, ou cela.
Koma inuyo muyenera kunena kuti, “Ambuye akalola, tikadzakhala ndi moyo, tidzachita zakutizakuti.”
16 Mais maintenant vous vous vantez en vos pensées orgueilleuses; toute vanterie de cette nature est mauvaise.
Koma mmene zililimu mumangodzitama ndi kudzikuza. Kudzitama konse kotereku ndi koyipa.
17 Il y a donc du péché en celui qui sait faire le bien, et qui ne le fait pas.
Aliyense amene amadziwa zabwino zimene amayenera kuchita koma osazichita, ndiye kuti wachimwa.

< Jacques 4 >