< Hébreux 8 >

1 Or l'abrégé de notre discours, [c'est que] nous avons un tel souverain Sacrificateur qui est assis à la droite du trône de la Majesté [de Dieu] dans les Cieux,
Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba.
2 Ministre du Sanctuaire, et du vrai Tabernacle, que le Seigneur a dressé et non pas les hommes.
Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.
3 Car tout souverain Sacrificateur est ordonné pour offrir des dons et des sacrifices, c'est pourquoi il est nécessaire que celui-ci aussi ait eu quelque chose pour offrir.
Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka.
4 Vu même que s'il était sur la terre il ne serait pas Sacrificateur, pendant qu'il y aurait des Sacrificateurs qui offrent des dons selon la Loi;
Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo.
5 Lesquels font le service dans le lieu qui n'est que l'image et l'ombre des choses célestes, selon que Dieu le dit à Moïse, quand il devait achever le Tabernacle: Or prends garde, lui dit-il, de faire toutes choses selon le modèle qui t'a été montré sur la montagne.
Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.”
6 Mais maintenant [notre souverain Sacrificateur] a obtenu un ministère d'autant plus excellent, qu'il est Médiateur d'une plus excellente alliance, qui est établie sous de meilleures promesses.
Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.
7 Parce que s'il n'y eût eu rien à redire dans la première, il n'eût jamais été cherché de lieu à une seconde.
Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake.
8 Car en censurant [les Juifs, Dieu] leur dit: Voici, les jours viendront, dit le Seigneur, que je traiterai avec la maison d'Israël et avec la maison de Juda une Nouvelle alliance:
Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati, “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
9 Non selon l'alliance que je traitai avec leurs pères, le jour que je les pris par la main pour les tirer du pays d'Egypte, car ils n'ont point persévéré dans mon alliance; c'est pourquoi je les ai méprisés, dit le Seigneur.
Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo, pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija ndipo Ine sindinawasamalire, akutero Ambuye.
10 Mais voici l'alliance que je traiterai après ces jours-là avec la maison d'Israël, dit le Seigneur, [c'est que] je mettrai mes lois dans leur entendement, et je les écrirai dans leur cœur; et je serai leur Dieu, et ils seront mon peuple.
Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli: Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye, Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo, ndi kulemba mʼmitima mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
11 Et chacun n'enseignera point son prochain, ni chacun son frère, en disant: connais le Seigneur; parce qu'ils me connaîtront tous, depuis le plus petit jusqu'au plus grand d'entre eux.
Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake, kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye chifukwa onse adzandidziwa, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.
12 Car je serai apaisé par rapport à leurs injustices, et je ne me souviendrai plus de leurs péchés, ni de leurs iniquités.
Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo, ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
13 En disant une nouvelle [alliance], il envieillit la première: or, ce qui devient vieux et ancien, est près d'être aboli.
Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

< Hébreux 8 >