< Hébreux 11 >

1 Or la foi rend présentes les choses qu'on espère, et elle est une démonstration de celles qu'on ne voit point.
Tsopano chikhulupiriro ndi kusakayika konse pa zinthu zimene tikuziyembekeza, ndi kutsimikiza kuti zinthu zimene sitiziona zilipo ndithu.
2 Car c'est par elle que les anciens ont obtenu [un bon] témoignage.
Ndi chikhulupiriro chimenechi makolo athu akale anayamikidwa.
3 Par la foi nous savons que les siècles ont été rangés par la parole de Dieu, de sorte que les choses qui se voient, n'ont point été faites de choses qui apparussent. (aiōn g165)
Ndi chikhulupiriro timazindikira kuti dziko lapansi ndi la mmwamba zinapangidwa ndi Mawu a Mulungu, ndikuti zinthu zoonekazi zinachokera ku zinthu zosaoneka. (aiōn g165)
4 Par la foi Abel offrit à Dieu un plus excellent sacrifice que Caïn, [et] par elle il obtint le témoignage d'être juste, à cause que Dieu rendait témoignage de ses dons; et lui étant mort parle encore par elle.
Ndi chikhulupiriro Abele anapereka kwa Mulungu nsembe yoposa imene Kaini anapereka. Ndi chikhulupiriro anatchedwa munthu wolungama Mulungu atayamikira zopereka zake. Ngakhale iye anafa, akuyankhulabe chifukwa cha chikhulupiriro chakecho.
5 Par la foi Enoch fut enlevé pour ne point passer par la mort; et il ne fut point trouvé, parce que Dieu l'avait enlevé; car avant qu'il fût enlevé il a obtenu le témoignage d'avoir été agréable à Dieu.
Ndi chikhulupiriro Enoki anatengedwa wamoyo, motero iye sanalawe imfa; sanapezeke chifukwa Mulungu anamutenga. Pakuti asanatengedwe anayamikiridwa kuti ankakondweretsa Mulungu.
6 Or il est impossible de lui être agréable sans la foi; car il faut que celui qui vient à Dieu, croie que Dieu est, et qu'il est le rémunérateur de ceux qui le cherchent.
Ndipo popanda chikhulupiriro nʼkosatheka kukondweretsa Mulungu, chifukwa aliyense amene amabwera kwa Iye ayenera kukhulupirira kuti Mulungu alipodi ndi kuti Iye amapereka mphotho kwa amene akumufunitsitsa.
7 Par la foi Noé ayant été divinement averti des choses qui ne se voyaient point encore, craignit, et bâtit l'Arche pour la conservation de sa famille, et par [cette Arche] il condamna le monde, et fut fait héritier de la justice qui est selon la foi.
Ndi chikhulupiriro, Nowa atachenjezedwa za zinthu zimene zinali zisanaoneke, anachita mantha napanga chombo kuti apulumutsire banja lake. Ndi chikhulupiriro chake anatsutsa dziko lapansi ndipo analandira chilungamo chimene chimabwera ndi chikhulupiriro.
8 Par la foi Abraham étant appelé, obéit, pour aller en la terre, qu'il devait recevoir en héritage, et il partit sans savoir où il allait.
Ndi chikhulupiriro Abrahamu atayitanidwa kuti apite ku dziko limene anamulonjeza kuti lidzakhala lake, anamvera ndi kupita, ngakhale sanadziwe kumene ankapita.
9 Par la foi il demeura comme étranger en la terre, qui lui avait été promise, comme si elle ne lui eût point appartenu, demeurant sous des tentes avec Isaac et Jacob, qui étaient héritiers avec lui de la même promesse.
Ndi chikhulupiriro chomwecho anakhala ngati mlendo mʼdziko lija limene Mulungu anamulonjeza. Anakhala mʼmatenti monganso anachitira Isake ndi Yakobo, amene nawonso analonjezedwanso.
10 Car il attendait la cité qui a des fondements, et de laquelle Dieu [est] l'architecte, et le fondateur.
Pakuti amadikira mudzi wokhala ndi maziko, umene mmisiri ndi womanga wake ndi Mulungu.
11 Par la foi aussi Sara reçut la vertu de concevoir un enfant, et elle enfanta hors d'âge, parce qu'elle fut persuadée que celui qui [le lui] avait promis, était fidèle.
Ndi chikhulupiriro Sara analandira mphamvu zokhala ndi pakati ngakhale kuti zaka zake zobala mwana zinali zitapita kale, popeza anamutenga amene analonjeza kukhala wokhulupirika.
12 C'est pourquoi d'un seul, et qui même [était] amorti, sont nés [des gens] qui égalent en nombre les étoiles du ciel, et le sable qui est sur le rivage de la mer, lequel ne se peut nombrer.
Nʼchifukwa chake mwa munthu mmodzi, amene anali ngati wakufa, munatuluka mibado yochuluka ngati nyenyezi ndi yosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
13 Tous ceux-ci sont morts en la foi, sans avoir reçu [les choses dont ils avaient eu] les promesses, mais ils les ont vues de loin, crues, et saluées, et ils ont fait profession qu'ils étaient étrangers et voyageurs sur la terre.
Onsewa anakhalabe mwachikhulupiriro mpaka anafa. Iwo sanalandire zimene Mulungu anawalonjeza; iwo anangozionera chapatali ndi kuzilandira. Ndipo iwo anavomereza kuti analidi alendo ndi osakhazikika pa dziko lapansi.
14 Car ceux qui tiennent ces discours montrent clairement qu'ils cherchent encore [leur] pays.
Anthu amene amanena zinthu zotere amaonekeratu kuti akufuna dziko lawo lenileni.
15 Et certes, s'ils eussent rappelé dans leur souvenir celui dont ils étaient sortis, ils avaient du temps pour y retourner.
Akanakhala kuti akuganizira za dziko limene analisiya akanapeza mpata obwerera kwawo.
16 Mais ils en désiraient un meilleur, c'est-à-dire, le céleste; c'est pourquoi Dieu ne prend point à honte d'être appelé leur Dieu, parce qu'il leur avait préparé une Cité.
Mʼmalo mwake, iwo amafunitsitsa dziko labwino, ndilo lakumwamba. Nʼchifukwa chake Mulungu sachita manyazi kutchedwa Mulungu wawo, pakuti Iye anawalonjeza mudzi.
17 Par la foi, Abraham étant éprouvé, offrit Isaac; celui, [dis-je], qui avait reçu les promesses, offrit même son fils unique.
Ndi chikhulupiriro Abrahamu, Mulungu atamuyesa, anapereka Isake ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu anamulonjeza, anakhala wokonzeka kupereka nsembe mwana wake mmodzi yekhayo.
18 A l'égard duquel il lui avait été dit: les descendants d'Isaac seront ta véritable postérité.
Za mwana ameneyu Mulungu anamuwuza iye kuti, “Zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.”
19 Ayant estimé que Dieu le pouvait même ressusciter d'entre les morts; c'est pourquoi aussi il le recouvra par une espèce [de résurrection].
Abrahamu amazindikira kuti Mulungu angathe kuukitsa akufa, ndipo tingathe kunena mofanizira kuti iye analandiranso Isake ngati wouka kwa akufa.
20 Par la foi Isaac donna à Jacob et à Esaü une bénédiction qui regardait l'avenir.
Ndi chikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau pa zatsogolo lawo.
21 Par la foi Jacob en mourant bénit chacun des fils de Joseph, et se prosterna [devant Dieu] étant appuyé sur le bout de son bâton.
Ndi chikhulupiriro, pamene Yakobo ankamwalira anadalitsa ana awiri a Yosefe, ndipo anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
22 Par la foi Joseph en mourant fit mention de la sortie des enfants d'Israël, et donna un ordre touchant ses os.
Ndi chikhulupiriro Yosefe ali pafupi kumwalira anayankhula za kutuluka kwa Aisraeli mu Igupto ndipo anawawuza zoti adzachite ndi mafupa ake.
23 Par la foi Moïse étant né fut caché trois mois par ses père et mère, parce que c'était un très bel enfant, et ils ne craignirent point l'Edit du Roi.
Ndi chikhulupiriro Mose atabadwa makolo ake anamubisa miyezi itatu, chifukwa iwo anaona kuti mwanayo anali wokongola ndipo sanaope konse lamulo la mfumu.
24 Par la foi Moïse étant déjà grand, refusa d'être nommé fils de la fille de Pharaon.
Ndi chikhulupiriro Mose atakula, anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao.
25 Choisissant plutôt d'être affligé avec le peuple de Dieu, que de jouir pour un peu de temps [des délices] du péché.
Iye anasankha kuzunzika nawo limodzi anthu a Mulungu kuposa kusangalala ndi zokondweretsa za uchimo kwa nthawi yochepa.
26 [Et] ayant estimé que l'opprobre de Christ était un plus grand trésor que les richesses de l'Egypte; parce qu'il avait égard à la rémunération.
Anaona kuti kuzunzika chifukwa cha Khristu kunali kwa mtengowapatali kuposa chuma cha ku Igupto, chifukwa amaona mphotho ya mʼtsogolo.
27 Par la foi il quitta l'Egypte, n'ayant point craint la fureur du Roi; car il demeura ferme, comme voyant celui qui est invisible.
Ndi chikhulupiriro anachoka ku Igupto wosaopa ukali wa mfumu. Iye anapirira chifukwa anamuona Mulungu amene ndi wosaonekayo.
28 Par la foi il fit la Pâque et l'aspersion du sang, afin que celui qui tuait les premiers-nés, ne touchât point à ceux [des Israélites].
Ndi chikhulupiriro anachita Paska ndi kuwaza magazi, kuti mngelo wowononga ana oyamba kubadwa asaphe ana oyamba kubadwa a Aisraeli.
29 Par la foi ils traversèrent la mer Rouge, comme par un lieu sec; ce que les Egyptiens ayant voulu éprouver, ils furent engloutis [dans les eaux].
Ndi chikhulupiriro Aisraeli anawoloka Nyanja Yofiira ngati pa mtunda powuma, koma Aigupto atayesa kutero anamizidwa.
30 Par la foi les murs de Jéricho tombèrent, après qu'on en eut fait le tour durant sept jours.
Ndi chikhulupiriro mpanda wa Yeriko unagwa, Aisraeli atawuzungulira kasanu ndi kawiri.
31 Par la foi Rahab l'hospitalière ne périt point avec les incrédules; ayant reçu les espions [et les ayant renvoyés] en paix.
Ndi chikhulupiriro Rahabe, mkazi wadama sanaphedwe pamodzi ndi osamvera aja chifukwa analandira bwino ozonda aja ku nyumba kwake.
32 Et que dirai-je davantage? car le temps me manquera, si je veux parler de Gédéon, de Barac, de Samson, de Jephté, de David, de Samuel, et des Prophètes,
Kodi ndinenenso chiyani? Nthawi yandichepera yoti ndinene za Gideoni, Baraki, Samsoni, Yefita, Davide, Samueli ndi aneneri,
33 Qui par la foi ont combattu les Royaumes, ont exercé la justice, ont obtenu [l'effet] des promesses, ont fermé les gueules des lions,
amene ndi chikhulupiriro anagonjetsa mafumu, anakhazikitsa chilungamo ndi kulandira zimene zinalonjezedwa. Anatseka pakamwa pa mikango,
34 Ont éteint la force du feu, sont échappés du tranchant des épées; de malades sont devenus vigoureux; se sont montrés forts dans la bataille, [et] ont tourné en fuite les armées des étrangers.
anazimitsa moto waukali, ndipo anapulumuka osaphedwa ndi lupanga. Anali ofowoka koma analandira mphamvu; anasanduka amphamvu pa nkhondo, nathamangitsa magulu a ankhondo a adani awo.
35 Les femmes ont recouvré leurs morts par le moyen de la résurrection; d'autres ont été étendus dans le tourment, ne tenant point compte d'être délivrés, afin d'obtenir la meilleure résurrection.
Amayi ena analandira anthu awo amene anafa, ataukitsidwanso. Enanso anazunzidwa ndipo anakana kumasulidwa, kuti adzaukenso ndi moyo wabwino.
36 Et d'autres ont été éprouvés par des moqueries et par des coups, par des liens, et par la prison.
Ena anawaseka ndi kuwakwapula, pamenenso ena anamangidwa ndi kupita ku ndende.
37 Ils ont été lapidés, ils ont été sciés, ils ont souffert de rudes épreuves, ils ont été mis à mort par le tranchant de l'épée, ils ont été errants çà et là, vêtus de peaux de brebis et de chèvres, réduits à la misère, affligés, tourmentés;
Anagendedwa miyala; anachekedwa pakati; ena anaphedwa ndi lupanga. Iwo anayendayenda atavala zikopa zankhosa ndi zikopa zambuzi, umphawi okhaokha, ozunzidwa ndi kuvutitsidwa.
38 Desquels le monde n'était pas digne; errant dans les déserts, et dans les montagnes, dans les cavernes, et dans les trous de la terre.
Dziko lapansi silinawayenere. Anayendayenda mʼzipululu ndi mapiri, ndiponso mʼmapanga ndi mʼmaenje.
39 Et quoiqu'ils aient tous été recommandables par leur foi, ils n'ont pourtant point reçu [l'effet de] la promesse;
Onsewa anayamikidwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo, komabe palibe wa iwo amene analandira zimene analonjezedwa.
40 Dieu ayant pourvu quelque chose de meilleur pour nous; en sorte qu'ils ne sont point parvenus à la perfection sans nous.
Mulungu anatikonzera ife kanthu koposa, kuti iwo asayesedwe angwiro popanda ife.

< Hébreux 11 >