< Colossiens 3 >

1 Si donc vous êtes ressuscités avec Christ, cherchez les choses qui sont en haut, où Christ est assis à la droite de Dieu.
Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.
2 Pensez aux choses qui sont en haut, et non point à celles qui sont sur la terre.
Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi.
3 Car vous êtes morts, et votre vie est cachée avec Christ en Dieu.
Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.
4 Quand Christ, qui est votre vie, apparaîtra, vous paraîtrez aussi alors avec lui en gloire.
Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.
5 Mortifiez donc vos membres qui sont sur la terre, la fornication, la souillure, les affections déréglées, la mauvaise convoitise, et l'avarice, qui est une idolâtrie;
Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano.
6 Pour lesquelles choses la colère de Dieu vient sur les enfants rebelles;
Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera.
7 Et dans lesquelles vous avez marché autrefois, quand vous viviez en elles.
Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja.
8 Mais rejetez maintenant toutes ces choses, la colère, l'animosité, la médisance; et qu'aucune parole déshonnête ne sorte de votre bouche.
Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa.
9 Ne mentez point l'un à l'autre ayant dépouillé le vieil homme avec ses actions,
Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake
10 Et ayant revêtu le nouvel homme, qui se renouvelle en connaissance, selon l'image de celui qui l'a créé.
ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake.
11 En qui il n'y a ni Grec, ni Juif, ni Circoncision, ni Prépuce, ni Barbare, ni Scythe, ni esclave, ni libre; mais Christ y est tout, et en tous.
Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.
12 Soyez donc, comme étant des élus de Dieu, saints et bien-aimés, revêtus des entrailles de miséricorde, de bonté, d'humilité, de douceur, d'esprit patient;
Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira.
13 Vous supportant les uns les autres, et vous pardonnant les uns aux autres; [et] si l'un a querelle contre l'autre, comme Christ vous a pardonné, vous aussi faites-en de même.
Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu.
14 Et outre tout cela, [soyez revêtus] de la charité, qui est le lien de la perfection.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.
15 Et que la paix de Dieu, à laquelle vous êtes appelés pour être un seul corps, tienne le principal lieu dans vos cœurs; et soyez reconnaissants.
Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.
16 Que la parole de Christ habite en vous abondamment en toute sagesse, vous enseignant et vous exhortant l'un l'autre par des Psaumes, des hymnes et des cantiques spirituels, avec grâce, chantant de votre cœur au Seigneur.
Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika.
17 Et quelque chose que vous fassiez, soit par parole ou par œuvre, faites tout au Nom du Seigneur Jésus, rendant grâces par lui à [notre] Dieu et Père.
Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.
18 Femmes, soyez soumises à vos maris, comme il est convenable selon le Seigneur.
Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
19 Maris, aimez vos femmes, et ne vous aigrissez point contre elles.
Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.
20 Enfants, obéissez à vos pères et à vos mères en toutes choses; car cela est agréable au Seigneur.
Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.
21 Pères, n'irritez point vos enfants, afin qu'ils ne perdent pas courage.
Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.
22 Serviteurs, obéissez en toutes choses à ceux qui sont vos maîtres selon la chair, ne servant point seulement sous leurs yeux, comme voulant complaire aux hommes, mais en simplicité de cœur, craignant Dieu.
Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye.
23 Et quelque chose que vous fassiez, faites tout de bon cœur, comme [le faisant] pour le Seigneur, et non pas pour les hommes;
Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu.
24 Sachant que vous recevrez du Seigneur le salaire de l'héritage: car vous servez Christ le Seigneur.
Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira.
25 Mais celui qui agit injustement, recevra ce qu'il aura fait injustement; car [en Dieu] il n'y a point d'égard à l'apparence des personnes.
Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.

< Colossiens 3 >