< Galates 4 >

1 Or je dis que pendant tout le temps que l'héritier est un enfant, il n'est en rien différent du serviteur, quoiqu'il soit Seigneur de tout.
Chimene ndikunena ndi chakuti, ngati mlowamʼmalo akali wamngʼono, sasiyana ndi kapolo, ngakhale kuti chuma chonse ndi chake.
2 Mais il est sous des tuteurs et des curateurs jusqu'au temps déterminé par le père.
Mwanayo ayenera kumvera omulera ndiponso anthu oyangʼanira chuma mpaka nthawi imene abambo ake anakhazikitsa.
3 Nous aussi, lorsque nous étions des enfants, nous étions asservis sous les rudiments du monde.
Chomwechonso, ife pamene tinali ana, tinali akapolo a miyambo ya dziko lapansi.
4 Mais quand l'accomplissement du temps est venu, Dieu a envoyé son Fils, né d'une femme, [et] soumis à la Loi.
Koma nthawi itakwana, Mulungu anatumiza Mwana wake, wobadwa mwa mayi, wobadwa pansi pa lamulo,
5 Afin qu'il rachetât ceux qui étaient sous la Loi, et que nous reçussions l'adoption des enfants.
kudzawombola amene anali pansi pa lamulo, kuti tilandiridwe monga ana.
6 Et parce que vous êtes enfants, Dieu a envoyé l'Esprit de son Fils dans vos cœurs, criant Abba, [c'est-à-dire] Père.
Ndipo popeza ndinu ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wake kuti alowe mʼmitima mwathu, Mzimu amene amafuwula kuti, “Abba, Atate.”
7 Maintenant donc tu n'es plus serviteur, mais fils; or si tu es fils, tu es aussi héritier de Dieu par Christ.
Choncho sindiwenso kapolo, koma mwana wa Mulungu. Tsono popeza ndiwe mwana wake, Mulungu wakusandutsanso mlowamʼmalo.
8 Mais lorsque vous ne connaissiez point Dieu, vous serviez ceux qui de [leur] nature ne sont point Dieux.
Koma poyamba pamene simunkamudziwa Mulungu, munali akapolo a zimene mwachilengedwe si milungu.
9 Et maintenant que vous avez connu Dieu, ou plutôt que vous avez été connus de Dieu, comment retournez-vous encore à ces faibles et misérables éléments, auxquels vous voulez encore servir comme auparavant?
Koma tsopano pakuti mukumudziwa Mulungu, kapena ndinene kuti Mulungu akukudziwani, nʼchifukwa chiyani mukubwereranso ku miyambo yofowoka ndi yomvetsa chisoni? Kodi mukufuna musandukenso akapolo?
10 Vous observez les jours, les mois, les temps et les années.
Mumasunga masiku, miyezi ndi nyengo ndi zaka.
11 Je crains pour vous que peut-être je n'aie travaillé en vain parmi vous.
Ine ndikuopa kuti mwina ntchito zanga pa inu ndinagwira pachabe.
12 Soyez comme moi; car je [suis] aussi comme vous; je vous [en] prie, mes frères; vous ne m'avez fait aucun tort.
Abale, ndikukudandaulirani, mukhale ngati ine, popeza ine ndinakhala ngati inu. Inu simunandilakwire.
13 Et vous savez comment je vous ai ci-devant évangélisé dans l'infirmité de la chair.
Monga inu mukudziwa ndinkakulalikirani Uthenga Wabwino ndili wofowoka.
14 Et vous n'avez point méprisé ni rejeté mon épreuve, telle qu'elle était en ma chair; mais vous m'avez reçu comme un Ange de Dieu, et comme Jésus-Christ même.
Ngakhale kuti matendawo anali ngati mayesero kwa inu, simunandinyoze kapena kunyansidwa nane. Komatu inu munandilandira ngati kuti ndinali mngelo wa Mulungu, ngati kuti ndinali Khristu Yesu mwini.
15 Quelle était donc la déclaration [que vous faisiez] de votre bonheur? car je vous rends témoignage que, s'il eût été possible, vous eussiez arraché vos yeux, et vous me les eussiez donnés.
Kodi chimwemwe chanu chonse chija chili kuti? Ine nditha kuchitira umboni kuti, ngati kukanatheka, inu mukanakolowola maso anu ndi kundipatsa.
16 Suis-je donc devenu votre ennemi, en vous disant la vérité?
Kodi tsopano ine ndasanduka mdani wanu chifukwa ndakuwuzani choonadi?
17 Ils sont jaloux de vous, [mais] ce n'est pas comme il faut; au contraire, ils vous veulent exclure, afin que vous soyez jaloux d'eux.
Anthu amenewo akuchita changu kuti akukopeni, koma changu chawocho sichabwino. Chimene iwo akufuna ndi chakuti akuchotseni inu kwa ife, kuti mukachite changu powathandiza iwowo.
18 Mais il est bon d'être toujours zélé pour le bien, et de ne l'être pas seulement quand je suis présent avec vous.
Nʼkwabwino kuchita changu, ngati cholingacho chili chabwino ndi kukhala otero nthawi zonse osati pokhapo pamene ine ndili ndi inu.
19 Mes petits enfants, pour lesquels enfanter je travaille de nouveau, jusqu'à ce que Christ soit formé en vous:
Ana anga okondedwa, inu amene ine ndikukumveraninso zowawa za kubereka kufikira Khristu atawumbidwa mwa inu,
20 Je voudrais être maintenant avec vous, et changer de langage, car je suis en perplexité sur votre sujet.
ine ndikanakonda ndikanakhala nanu tsopano kuti ndisinthe mawu anga, chifukwa ndathedwa nanu nzeru.
21 Dites-moi, vous qui voulez être sous la Loi, n'entendez-vous point la Loi?
Tandiwuzani, inu, abale amene mukufuna kukhala pansi pa lamulo, kodi simukudziwa chimene lamulo limanena?
22 Car il est écrit qu'Abraham a eu deux fils, l'un de la servante, et l'autre de la [femme] libre.
Pakuti zinalembedwa kuti Abrahamu anali ndi ana aamuna awiri, wina mayi wake anali kapolo ndipo wina mayi wake anali mfulu.
23 Mais celui qui était de la servante, naquit selon la chair; et celui qui était de la [femme] libre, naquit par la promesse.
Mwana wake wobadwa mwa kapolo anabadwa mwathupi; koma mwana wake wobadwa mwa mfulu anabadwa monga mwa lonjezo.
24 Or ces choses doivent être entendues par allégorie: car ce sont les deux alliances; l'une du mont de Sinaï, qui ne produit que des esclaves, et c'est Agar.
Zinthu izi zinali ngati fanizo, pakuti amayi awiriwa akuyimira mapangano awiri. Pangano limodzi ndi lochokera mʼPhiri la Sinai, ndiye Hagara, ndipo amabereka ana amene ndi akapolo.
25 Car ce nom d'Agar veut dire Sinaï; qui est une montagne en Arabie, et correspondante à la Jérusalem de maintenant, laquelle sert avec ses enfants.
Tsono Hagara, akuyimira Phiri la Sinai ku Arabiya amene afanizidwa ndi mzinda wa Yerusalemu wa lero, chifukwa ali mu ukapolo pamodzi ndi ana ake.
26 Mais la Jérusalem d'en haut est [la femme] libre, et c'est la mère de nous tous.
Koma Yerusalemu wakumwamba ndiye mfulu, ndipo ndiye mayi wathu.
27 Car il est écrit: réjouis-toi, stérile, qui n'enfantais point; efforce-toi, et t'écrie, toi qui n'étais point en travail d'enfant; car il y a beaucoup plus d'enfants de [celle qui avait été] laissée, que de celle qui avait un mari.
Pakuti kwalembedwa kuti, “Sangalala, iwe mayi wosabala, amene sunabalepo mwana; imba nthungululu ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa.”
28 Or pour nous, mes frères, nous sommes enfants de la promesse, ainsi qu'Isaac.
Tsono inu abale, ndinu ana alonjezo ngati Isake.
29 Mais comme alors celui qui était né selon la chair, persécutait celui [qui était né] selon l'Esprit, il [en est] de même aussi maintenant.
Nthawi imeneyo mwana wobadwa mwathupi anazunza mwana wobadwa mwamphamvu za Mzimu. Zili chimodzimodzinso lero.
30 Mais que dit l'Ecriture? chasse la servante et son fils: car le fils de la servante ne sera point héritier avec le fils de la [femme] libre.
Kodi Malemba akuti chiyani? “Muchotse kapoloyo pamodzi ndi mwana wake, chifukwa mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wamfulu.”
31 Or mes frères, nous ne sommes point enfants de la servante, mais de la [femme] libre.
Chifukwa chake, abale, ife sindife ana akapolo, koma ana a mfulu.

< Galates 4 >