< 2 Corinthiens 9 >

1 Car de vous écrire touchant la collecte qui se fait pour les Saints, ce me serait une chose superflue.
Nʼkosafunika kuti ndikulembereni za utumiki othandiza anthu a Mulungu.
2 Vu que je sais la promptitude de votre zèle, en quoi je me glorifie de vous devant ceux de Macédoine, [leur faisant entendre] que l'Achaïe est prête dès l'année passée; et votre zèle en a excité plusieurs.
Popeza ndikudziwa mtima wanu wofuna kuthandiza, ndipo ndakhala ndikuwawuza monyadira a ku Makedoniya za chimenechi. Ndimawawuza kuti inu a ku Akaya munakonzeka kale chaka chatha kuti mupereke. Ndipo changu chanu chapatsa chidwi ambiri mwa iwo kuti nawonso achitepo kanthu.
3 Or j'ai envoyé ces frères, afin que ce en quoi je me suis glorifié de vous, ne soit pas vain en cette occasion, et que vous soyez prêts, comme j'ai dit.
Koma ndikutumiza abalewo kuti kukunyadirani kwathu pa zimenezi kutsimikizike kuti si kwachabe ndi kuti mukhale okonzeka monga ndinanenera.
4 De peur que ceux de Macédoine venant avec moi, et ne vous trouvant pas prêts, nous n'ayons de la honte, (pour ne pas dire vous-mêmes) de l'assurance avec laquelle nous nous sommes glorifiés de vous.
Pakuti nditabwera kumeneko ndi abale ena a ku Makedoniya, ndikukupezani kuti simunakonzeke, tingadzachite manyazi chifukwa chokudalirani. Koma amene angadzachite manyazi kwambiri ndi inuyo.
5 C'est pourquoi j'ai estimé qu'il était nécessaire de prier les frères d'aller premièrement vers vous, et d'achever de préparer votre bénéficence que vous avez déjà promise; afin qu'elle soit prête comme une bénéficence, et non pas comme une chicheté.
Choncho ndinaganiza kuti nʼkofunika kupempha abale kuti adzakuchezereni ineyo ndisanafike, ndikuti adzatsirize kukonzekera mphatso zomwe munalonjeza kupereka mowolowamanja. Motero mphatsoyo idzakhala yokonzeratu, ndipo idzakhala mphatso yoperekedwa mowolowamanja, osati mokakamizidwa.
6 Or je vous dis ceci: que celui qui sème chichement, recueillera aussi chichement; et que celui qui sème libéralement, recueillera aussi libéralement.
Takumbukirani mawu awa: Amene adzala pangʼono, adzakololanso pangʼono, ndipo amene adzala zochuluka, adzakololanso zochuluka.
7 [Mais] que chacun [contribue] selon qu'il se l'est proposé en son cœur, non point à regret, ou par contrainte; car Dieu aime celui qui donne gaiement.
Munthu aliyense apereke chimene watsimikiza mu mtima mwake kuti apereka, osati monyinyirika kapena mokakamizidwa, pakuti Mulungu amakonda wopereka mokondwera.
8 Et Dieu est puissant pour faire abonder toute grâce en vous, afin qu'ayant toujours tout ce qui suffit en toute chose, vous soyez abondants en toute bonne œuvre:
Ndipo Mulungu akhoza kukudalitsani kwambiri, kuti inuyo nthawi zonse mukhale ndi zinthu zokukwanirani, ndiponso ndi zina zochuluka kuti muthandize pa ntchito zonse zabwino.
9 Selon ce qui est écrit: il a répandu, il a donné aux pauvres; sa justice demeure éternellement. (aiōn g165)
Paja analemba kuti, “Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya.” (aiōn g165)
10 Or celui qui fournit de la semence au semeur, veuille aussi vous donner du pain à manger, et multiplier votre semence, et augmenter les revenus de votre justice.
Tsono Mulungu amene amapereka mbewu kwa wofesa, ndiponso chakudya kuti adye, adzaperekanso mbewu mʼnkhokwe zanu ndi kuzichulukitsa. Iye adzachulukitsanso zipatso za chilungamo chanu.
11 Etant pleinement enrichis pour [exercer] une parfaite libéralité, laquelle fait que nous en rendons grâces à Dieu.
Adzakulemeretsani pa zonse kuti mukhale owolowamanja pa nthawi zonse. Ndipo kuwolowamanja kwanu kudzera mwa ife, kudzakhala kuthokoza kwa Mulungu.
12 Car l'administration de cette oblation n'est pas seulement suffisante pour subvenir aux nécessités des Saints, mais elle abonde aussi de telle sorte, que plusieurs ont de quoi en rendre grâces à Dieu.
Ntchito imene mukugwirayi siyongothandiza kokha anthu a Mulungu kupeza zosowa, komanso ikuthandiza kuti anthu ambiri ayamike Mulungu.
13 Glorifiant Dieu pour l'épreuve qu'ils font de cette assistance, en ce que vous vous soumettez à l'Évangile de Christ; et de votre prompte et libérale communication envers eux, et envers tous.
Chifukwa cha ntchito imene mwawatsimikizira nokha, anthu ena onse adzayamika Mulungu chifukwa cha kumvera kwanu kumene kumaonekera pamene mukuvomereza Uthenga Wabwino wa Khristu, ndiponso chifukwa chowagawira mowolowamanja iwowo pamodzi ndi wina aliyense.
14 Ils prient Dieu pour vous, et ils vous aiment très affectueusement à cause de la grâce excellente que Dieu vous a accordée.
Ndipo iwowo adzakupemphererani mwachikondi chifukwa cha chisomo choposa chimene Ambuye wakupatsani.
15 Or grâces soient rendues à Dieu à cause de son don inexprimable.
Tiyamike Mulungu chifukwa cha mphatso zake zosaneneka!

< 2 Corinthiens 9 >