< 2 Corinthiens 6 >

1 Ainsi donc étant ouvriers avec lui, nous vous prions aussi que vous n'ayez point reçu la grâce de Dieu en vain.
Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe.
2 Car il dit: je t'ai exaucé au temps favorable et t'ai secouru au jour du salut; voici maintenant le temps favorable, voici maintenant le jour du salut.
Pakuti akunena kuti, “Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera, ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza. Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”
3 Ne donnant aucun scandale en quoi que ce soit, afin que [notre] ministère ne soit point blâmé.
Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke.
4 Mais nous rendant recommandables, en toutes choses, comme ministres de Dieu, en grande patience, en afflictions, en nécessités, en angoisses,
Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa.
5 En blessures, en prisons, en troubles, en travaux,
Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya;
6 En veilles, en jeûnes, en pureté; par la connaissance, par un esprit patient, par la douceur, par le Saint-Esprit, par une charité sincère,
pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi
7 Par la parole de la vérité, par la puissance de Dieu, par les armes de justice que l'on porte à la main droite et à la main gauche.
ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo.
8 Parmi l'honneur et l'ignominie, parmi la calomnie et la bonne réputation.
Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza.
9 Comme séducteurs, et toutefois étant véritables; comme inconnus, et toutefois étant reconnus; comme mourants, et voici nous vivons; comme châtiés, et toutefois non mis à mort;
Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa.
10 Comme attristés, et toutefois toujours joyeux; comme pauvres, et toutefois enrichissant plusieurs; comme n'ayant rien, et toutefois possédant toutes choses.
Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.
11 Ô Corinthiens! notre bouche est ouverte pour vous, notre cœur s'est élargi.
Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu.
12 Vous n'êtes point à l'étroit au-dedans de nous, mais vous êtes à l'étroit dans vos entrailles.
Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife.
13 Or pour nous traiter de la même manière ( je vous parle comme à mes enfants) élargissez-vous aussi [à notre égard].
Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.
14 Ne portez pas un même joug avec les infidèles; car quelle participation y a-t-il de la justice avec l'iniquité? et quelle communication y a-t-il de la lumière avec les ténèbres?
Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima?
15 Et quel accord y a-t-il de Christ avec Bélial? ou quelle part a le fidèle avec l'infidèle?
Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira?
16 Et quelle convenance y a-t-il du Temple de Dieu avec les idoles? car vous êtes le Temple du Dieu vivant, selon ce que Dieu a dit: j'habiterai au milieu d'eux, et j'y marcherai; et je serai leur Dieu, et ils seront mon peuple.
Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti, “Ndidzakhala mwa iwo ndipo ndidzayendayenda pakati pawo, ndipo ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo adzakhala anthu anga.”
17 C'est pourquoi sortez du milieu d'eux, et vous en séparez, dit le Seigneur; et ne touchez à aucune chose souillée et je vous recevrai;
Nʼchifukwa chake “Tulukani pakati pawo ndi kudzipatula, akutero Ambuye. Musakhudze chodetsedwa chilichonse, ndipo ndidzakulandirani.”
18 Et je vous serai pour père, et vous me serez pour fils et pour filles, dit le Seigneur Tout-puissant.
Ndipo “Ndidzakhala Atate anu, ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi, akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”

< 2 Corinthiens 6 >