< 2 Corinthiens 11 >

1 Plût à Dieu que vous me supportassiez un peu dans mon imprudence; mais encore supportez-moi.
Ndikukhulupirira kuti mupirira nako pangʼono kupusa kwanga. Chonde tandipirirani!
2 Car je suis jaloux de vous d'une jalousie de Dieu; parce que je vous ai unis à un seul mari, pour vous présenter à Christ [comme] une vierge chaste.
Nsanje imene ndimakuchitirani ndi yofanana ndi ya Mulungu. Ndinakulonjezani mwamuna mmodzi yekha, mwamunayo ndiye Khristu, kuti ndidzakuperekeni inuyo kwa Iyeyo monga namwali wangwiro.
3 Mais je crains, que comme le serpent séduisit Eve par sa ruse, vos pensées aussi ne se corrompent, [en se détournant] de la simplicité qui est en Christ.
Koma ndikuopa kuti monga Hava ananyengedwa ndi kuchenjera kwa njoka, mitima yanunso ingasocheretsedwe kuleka nʼkudzipereka moona mtima ndi modzipereka kwenikweni kwa Khristu.
4 Car si quelqu'un venait qui vous prêchât un autre Jésus que nous n'avons prêché; ou si vous receviez un autre Esprit que celui que vous avez reçu, ou un autre Evangile que celui que vous avez reçu, feriez-vous bien de l'endurer?
Pakuti ngati wina abwera kwa inu nalalikira Yesu wina wosiyana ndi Yesu amene tinamulalikira, kapena ngati mulandira mzimu wina wosiyana ndi Mzimu amene munalandira, kapena uthenga wabwino wina wosiyana ndi umene munawuvomereza, inuyo mumangolandira mosavuta.
5 Mais j'estime que je n'ai été en rien moindre que les plus excellents Apôtres.
Komatu sindikuganiza kuti ndine wotsika kwambiri kwa “atumwi apamwamba.”
6 Que si je suis comme quelqu'un du vulgaire par rapport au langage, je ne [le suis] pourtant pas en connaissance; mais nous avons été entièrement manifestés en toutes choses envers vous.
Mwina ndikhoza kukhala wosaphunzitsidwa kayankhulidwe, koma ndili ndi chidziwitso. Izi tinakufotokozerani momveka bwinobwino.
7 Ai-je commis une faute en ce que je me suis abaissé moi-même, afin que vous fussiez élevés, parce que sans rien prendre je vous ai annoncé l'Évangile de Dieu?
Kodi linali tchimo kwa ine kudzichepetsa nʼcholinga chakuti ndikukwezeni pamene ndinkalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu kwa inu mwaulere?
8 J'ai dépouillé les autres Églises, prenant de quoi m'entretenir pour vous servir.
Ndinkalanda mipingo ina pomalandira thandizo kwa iwo kuti ndikutumikireni.
9 Et lorsque j'étais avec vous, et que j'ai été en nécessité, je ne me suis point relâché du travail afin de n'être à charge à personne; car les frères qui étaient venus de Macédoine ont suppléé à ce qui me manquait; et je me suis gardé de vous être à charge en aucune chose, et je m'en garderai encore.
Ndipo pamene ndinali pakati panu, nditasowa kanthu, sindinalemetse munthu aliyense, pakuti abale ena amene anachokera ku Makedoniya anandipatsa zonse zimene ndinkazisowa. Ndayesetsa kuti ndisakhale cholemetsa kwa inu mʼnjira ina iliyonse, ndipo ndidzapitiriza kutero.
10 La vérité de Christ est en moi, que cette gloire ne me sera point ravie dans les contrées de l'Achaïe.
Kunena moona mtima molingana ndi chilungamo cha Khristu chimene chili mwa ine, palibe amene angandiletse kudzitamandira mʼzigawo za ku Akaya.
11 Pourquoi? est-ce parce que je ne vous aime point? Dieu le sait!
Nʼchifukwa chiyani ndikutero? Kodi nʼchifukwa choti sindikukondani? Mulungu akudziwa kuti ndimakukondani!
12 Mais ce que je fais, je le ferai encore, pour retrancher l'occasion à ceux qui cherchent l'occasion; afin qu'en ce de quoi ils se glorifient, ils soient aussi trouvés tout tels que nous sommes.
Ndipo ndipitiriza kuchita zomwe ndikuchitazi nʼcholinga chakuti ndisapereke mpata kwa amene akufuna kupezera mwayi woti afanane nafe pa zinthu zimene iwowo amadzitamandira.
13 Car tels faux Apôtres sont des ouvriers trompeurs, qui se déguisent en Apôtres de Christ.
Pakuti anthu oterewa ndi atumwi onama, antchito achinyengo, odzizimbayitsa ngati atumwi a Khristu.
14 Et cela n'est pas étonnant: car satan lui-même se déguise en Ange de lumière.
Sizododometsa zimenezi, pakuti Satana mwini amadzizimbayitsa kuoneka ngati mngelo wowunikira anthu.
15 Ce n'est donc pas un grand sujet d'étonnement si ses ministres aussi se déguisent en ministres de justice; [mais] leur fin sera conforme à leurs œuvres.
Nʼzosadabwitsa tsono ngati atumiki ake akudzizimbayitsa ngati otumikira chilungamo. Matsiriziro awo adzalandira zoyenerana ndi ntchito zawo.
16 Je le dis encore, afin que personne ne pense que je sois imprudent; ou bien supportez-moi comme un imprudent, afin que je me glorifie aussi un peu.
Ndibwereze kunena kuti, wina aliyense asandiyese chitsiru. Koma ngati mutero, mundilandire monga mmene mukhoza kulandirira chitsiru, kuti ndinyadirepo pangʼono.
17 Ce que je vais dire, en rapportant les sujets que j'aurais de me glorifier, je ne le dirai pas selon le Seigneur, mais comme par imprudence.
Kudzinyadira kwangaku, sindikuyankhula monga mmene Ambuye akufunira koma ngati chitsiru.
18 Puis [donc] que plusieurs se vantent selon la chair, je me vanterai moi aussi.
Popeza ambiri akudzitama monga dziko lapansi limachitira, inenso ndidzitamanso.
19 Car vous souffrez volontiers les imprudents, parce que vous êtes sages.
Inu mumalolera kukhala ndi zitsiru mokondwera chifukwa mumati ndinu anzeru!
20 Même si quelqu'un vous asservit, si quelqu'un vous mange, si quelqu'un prend [votre bien], si quelqu'un s'élève [sur vous], si quelqu'un vous frappe au visage, vous le souffrez.
Kunena zoona mumangololera aliyense; amene amakusandutsani akapolo, kapena amene amakudyerani masuku pamutu, kapena amene amakupezererani, kapena amene amadzitukumula, kapena amene amakumenyani khofi.
21 Je le dis avec honte, même comme si nous avions été sans aucune force; mais si en quelque chose quelqu'un ose [se glorifier] (je parle en imprudent) j'ai la même hardiesse.
Ndikuvomera mwamanyazi kuti ife sitinali olimba mtima kuti nʼkuchita zinthu zimenezi. Ndikuyankhula ngati chitsiru kuti chimene wina aliyense akhoza kudzitama nacho, Inenso ndikhoza kudzitama nachonso.
22 Sont-ils Hébreux? je le suis aussi. Sont-ils Israélites? je le suis aussi. Sont-ils de la semence d'Abraham? je le suis aussi.
Kodi iwo ndi Ahebri? Inenso ndine Mhebri. Kodi iwo ndi Aisraeli? Inenso ndine Mwisraeli. Kodi iwo ndi zidzukulu za Abrahamu? Inenso ndine mdzukulu wa Abrahamu.
23 Sont-ils ministres de Christ? (je parle comme un imprudent) je le suis plus qu'eux; en travaux davantage, en blessures plus qu'eux, en prison davantage, en morts plusieurs fois.
Kodi iwo ndi atumiki a Khristu? Ndikuyankhula ngati wamisala. Ine ndine woposa iwowo. Ndagwira ntchito kwambiri kupambana iwo, ndakhala ndikuyikidwa mʼndende kawirikawiri, ndakwapulidwapo kwambiri, kawirikawiri ndinali pafupi kufa.
24 J'ai reçu des Juifs par cinq fois quarante coups, moins un.
Andikwapulapo kasanu zikoti zija za Ayuda, makumi anayi kuchotsapo chimodzi.
25 J'ai été battu de verges trois fois; j'ai été lapidé une fois; j'ai fait naufrage trois fois; j'ai passé un jour et une nuit en la profonde mer.
Katatu anandimenya ndi ndodo. Kamodzi anandigendapo miyala. Katatu sitima yathu ya panyanja inasweka, ndipo ndinakhala usiku ndi usana ndi kuyandama pa nyanja.
26 En voyages souvent, en périls des fleuves, en périls des brigands, en périls de [ma] nation, en périls des Gentils, en périls dans les villes, en périls dans les déserts, en périls en mer, en périls parmi de faux frères;
Ndakhala ndikuyenda maulendo ataliatali. Moyo wanga wakhala ukukumana ndi zoopsa pa mitsinje, zoopsa za achifwamba, zoopsa zochokera kwa abale anga Ayuda, zoopsa zochokera kwa anthu akunja. Ndinakumana ndi zoopsa mʼmizinda, mʼmidzi, pa nyanja, ndi pakati pa abale onyenga.
27 En peine et en travail, en veilles souvent, en faim et en soif, en jeûnes souvent, dans le froid et dans la nudité.
Ndakhala ndikugwira ntchito molimbika ndipo kawirikawiri ndakhala ndikuchezera usiku wonse osagona. Ndakhala ndikumva njala ndi ludzu ndipo kawirikawiri ndakhala wopanda chakudya. Ndakhala ndi kuzizidwa ndi wosowa zovala.
28 Outre les choses de dehors ce qui me tient assiégé tous les jours, c'est le soin que j'ai de toutes les Églises.
Kuwonjezera pa zonsezi, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa chipsinjo cha nkhawa ya mipingo yonse.
29 Qui est-ce qui est affaibli, que je ne sois aussi affaibli? qui est-ce qui est scandalisé, que je n'en sois aussi brûlé?
Ndani ali wofowoka, ine wosakhala naye mʼkufowoka kwakeko? Ndani amene mnzake amuchimwitsa, ine wosavutika mu mtima?
30 S'il faut se glorifier, je me glorifierai des choses qui sont de mon infirmité.
Ngati nʼkoyenera kudzitamandira, ndidzadzitamandira pa zinthu zimene zimaonetsa kufowoka kwanga.
31 Dieu, qui est le Père de notre Seigneur Jésus-Christ, et qui est béni éternellement, sait que je ne mens point. (aiōn g165)
Mulungu, Atate a Ambuye Yesu, amene tiyenera kumutamanda nthawi zonse, akudziwa kuti sindikunama. (aiōn g165)
32 A Damas, le Gouverneur pour le roi Arétas avait mis des gardes dans la ville des Damascéniens pour me prendre;
Ku Damasiko, bwanamkubwa woyimira Mfumu Areta, anayika alonda kuzungulira mzinda wonse kuti andigwire.
33 Mais on me descendit de la muraille dans une corbeille par une fenêtre, et ainsi j'échappai de ses mains.
Koma abale anandiyika mʼdengu nanditsitsira pa chipupa kudzera pa zenera la mpandawo, motero ndinapulumuka mʼmanja mwake.

< 2 Corinthiens 11 >