< 1 Timothée 3 >

1 Cette parole est certaine, qui si quelqu'un désire d'être Evêque, il désire une œuvre excellente.
Mawu woona ndi awa: Ngati munthu akufunitsitsa atakhala woyangʼanira, ndiye kuti akufuna ntchito yabwino.
2 Mais il faut que l'Evêque soit irrépréhensible, mari d'une seule femme, vigilant, modéré, honorable, hospitalier, propre à enseigner;
Tsono woyangʼanira ayenera kukhala munthu wopanda chotsutsika nacho, mwamuna wa mkazi mmodzi yekha, woganiza bwino, wodziretsa, waulemu, wosamala bwino alendo, wodziwa kuphunzitsa.
3 Non sujet au vin, non batteur, non convoiteux d'un gain déshonnête, mais doux, non querelleur, non avare.
Asakhale chidakwa, asakhale wandewu, koma wofatsa, asakhale wokonda mikangano, kapena wokonda ndalama.
4 Conduisant honnêtement sa propre maison, tenant ses enfants soumis en toute pureté de mœurs.
Akhale wodziwa kusamala bwino banja lake ndi kulera ana ake bwino, kuti akhale omvera ndi aulemu weniweni.
5 Car si quelqu'un ne sait pas conduire sa propre maison, comment pourra-t-il gouverner l'Eglise de Dieu?
(Ngati munthu sadziwa kusamala banja lake lomwe, angathe bwanji kusamala mpingo wa Mulungu?)
6 Qu'il ne soit point nouvellement converti; de peur qu'étant enflé d'orgueil, il ne tombe dans la condamnation du calomniateur.
Asakhale wongotembenuka mtima kumene kuopa kuti angadzitukumule napezeka pa chilango monga Satana.
7 Il faut aussi qu'il ait un bon témoignage de ceux de dehors, qu'il ne tombe point dans des fautes qui puissent lui être reprochées, et dans le piége du Démon.
Ayeneranso kukhala munthu wambiri yabwino ndi akunja, kuti anthu asamutonze nagwa mu msampha wa Satana.
8 Que les Diacres aussi soient graves, non doubles en parole, non sujets à beaucoup de vin, non convoiteux d'un gain déshonnête.
Momwemonso atumiki, akhale anthu oyenera ulemu, woona mtima, osakhala okonda zoledzeretsa, osakonda kupeza zinthu mwachinyengo.
9 Retenant le mystère de la foi dans une conscience pure.
Ayenera kugwiritsa mozama choonadi cha chikhulupiriro ndi kukhala ndi chikumbumtima chabwino.
10 Que ceux-ci aussi soient premièrement éprouvés, et qu'ensuite ils servent, après avoir été trouvés sans reproche.
Ayambe ayesedwa kaye, ndipo ngati palibe kanthu kowatsutsa, aloleni akhale atumiki.
11 De même, que leurs femmes soient honnêtes, non médisantes, sobres, fidèles en toutes choses.
Momwemonso, akazi akhale olemekezeka, osasinjirira koma oganiza bwino ndi odalirika pa chilichonse.
12 Que les Diacres soient maris d'une seule femme, conduisant honnêtement leurs enfants, et leurs propres familles.
Mtumiki akhale wokhulupirika kwa mkazi wake ndipo ayenera kukhala wosamalira bwino ana ake ndi onse a pa khomo pake.
13 Car ceux qui auront bien servi, acquièrent un bon degré pour eux, et une grande liberté dans la foi qui est en Jésus-Christ.
Iwo amene atumikira bwino amakhala ndi mbiri yabwino ndipo amakhala chitsimikizo chachikulu cha chikhulupiriro chawo mwa Khristu Yesu.
14 Je t'écris ces choses espérant que j'irai bientôt vers toi;
Ngakhale ndili ndi chiyembekezo choti ndifika komweko posachedwapa, ndikukulemberani malangizo awa.
15 Mais en cas que je tarde, [je t'écris ces choses] afin que tu saches comment il faut se conduire dans la Maison de Dieu, qui est l'Eglise du Dieu vivant, la Colonne et l'appui de la vérité.
Ine zina zikandichedwetsa kubwera, mudziwe za mmene anthu ayenera kukhalira mʼNyumba ya Mulungu, imene ndi mpingo wa Mulungu wamoyo, mzati ndi maziko achoonadi.
16 Et sans contredit, le mystère de la piété est grand, [savoir], que Dieu a été manifesté en chair, justifié en Esprit, vu des Anges, prêché aux Gentils, cru au monde, et élevé dans la gloire.
Mosakayikira, chinsinsi cha chikhulupiriro chathu chachikulu: Khristu anaonekera ali ndi thupi la munthu, Mzimu anamuchitira umboni, angelo anamuona, analalikidwa pakati pa mitundu yonse, dziko lapansi linamukhulupirira, anatengedwa kupita kumwamba mwa ulemerero.

< 1 Timothée 3 >