< Psalms 94 >

1 God is Lord of veniauncis; God of veniauncis dide freli.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Be thou enhaunsid that demest the erthe; yelde thou yeldinge to proude men.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Lord, hou longe synneris; hou longe schulen synneris haue glorie?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Thei schulen telle out, and schulen speke wickidnesse; alle men schulen speke that worchen vnriytfulnesse.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Lord, thei han maad lowe thi puple; and thei han disesid thin eritage.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Thei killiden a widowe and a comelyng; and thei han slayn fadirles children and modirles.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 And thei seiden, The Lord schal not se; and God of Jacob schal not vndurstonde.
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Ye vnwise men in the puple, vndirstonde; and, ye foolis, lerne sum tyme.
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Schal not he here, that plauntide the eere; ethere biholdith not he, that made the iye?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Schal not he repreue, that chastisith folkis; which techith man kunnyng?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 The Lord knowith the thouytis of men; that tho ben veyne.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Blessid is the man, whom thou, Lord, hast lerned; and hast tauyt him of thi lawe.
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 That thou aswage hym fro yuele daies; til a diche be diggid to the synner.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 For the Lord schal not putte awei his puple; and he schal not forsake his eritage.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Til riytfulnesse be turned in to dom; and who ben niy it, alle that ben of riytful herte.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Who schal rise with me ayens mysdoeris; ether who schal stonde with me ayens hem that worchen wickidnesse?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 No but for the Lord helpide me; almest my soule hadde dwellid in helle.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 If Y seide, My foot was stirid; Lord, thi merci helpide me.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Aftir the multitude of my sorewis in myn herte; thi coumfortis maden glad my soule.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Whether the seete of wickidnesse cleueth to thee; that makist trauel in comaundement?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 Thei schulen take ayens the soule of a iust man; and thei schulen condempne innocent blood.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 And the Lord was maad to me in to refuyt; and my God was maad in to the help of myn hope.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 And he schal yelde to hem the wickidnesse of hem; and in the malice of hem he schal lese hem, oure Lord God schal lese hem.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Psalms 94 >