< Joel 3 >

1 For lo! in tho daies, and in that tyme, whanne Y schal turne the caitifte of Juda and of Jerusalem,
“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
2 Y schal gadere alle folkis, and Y schal lede hem in to the valei of Josephat; and Y schal dispute there with hem on my puple, and myn eritage Israel, whiche thei scateriden among naciouns; and thei departiden my lond, and senten lot on my puple;
ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
3 and thei settiden a knaue child in the bordel hous, and seelden a damesel for wyn, that thei schulden drynke.
Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
4 But what to me and to you, thou Tire, and Sidon, and ech ende of Palestyns? Whethir ye schulen yelde vengyng to me? and if ye vengen you ayens me, soone swiftli Y schal yelde while to you on youre heed.
“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
5 Ye token awey my siluer and gold, and ye brouyten my desirable thingis and faireste thingis in to youre templis of idols.
Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
6 And ye selden the sones of Juda, and the sones of Jerusalem to the sones of Grekis, that ye schulden make hem fer fro her coostis.
Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
7 Lo! Y schal reise hem fro the place in which ye seelden hem; and Y schal turne youre yeldyng in to youre heed.
“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
8 And Y schal sille youre sones and youre douytris in the hondis of the sones of Juda, and thei schulen selle hem to Sabeis, a fer folc, for the Lord spak.
Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
9 Crye ye this thing among hethene men, halewe ye batel, reise ye stronge men; alle men werriours, neiy, and stie.
Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
10 Beete ye togydere youre plowis in to swerdis, and youre mattokkis in to speeris; a sijk man seie, that Y am strong.
Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
11 Alle folkis, breke ye out, and come fro cumpas, and be ye gaderid togidere; there the Lord schal make thi stronge men to die.
Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
12 Folkis rise togidere, and stie in to the valei of Josofat; for Y schal sitte there, to deme alle folkis in cumpas.
“Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
13 Sende ye sikelis, `ether sithis, for ripe corn wexide; come ye, and go ye doun, for the pressour is ful; pressouris ben plenteuouse, for the malice of hem is multiplied.
Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
14 Puplis, puplis in the valei of kittyng doun; for the dai of the Lord is nyy in the valei of kittyng doun.
Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
15 The sunne and the moone ben maad derk, and sterris withdrowen her schynyng.
Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
16 And the Lord schal rore fro Sion, and schal yyue his vois fro Jerusalem, and heuenes and erthe schulen be mouyd; and the Lord is the hope of his puple, and the strengthe of the sones of Israel.
Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
17 And ye schulen wite, that Y am youre Lord God, dwellynge in Sion, in myn hooli hil; and Jerusalem schal be hooli, and aliens schulen no more passe bi it.
“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
18 And it schal be, in that dai mounteyns schulen droppe swetnesse, and litle hillis schulen flowe with mylke, and watris schulen go bi alle the ryueris of Juda; and a welle schal go out of the hous of the Lord, and schal moiste the stronde of thornes.
“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
19 Egipt schal be in to desolacioun, and Idume in to desert of perdicioun; for that that thei diden wickidli ayens the sones of Juda, and schedden out innocent blood in her lond.
Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
20 And Judee schal be enhabited with outen ende, and Jerusalem in to generacioun and in to generacioun.
Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
21 And Y schal clense the blood of hem, which Y hadde not clensid; and the Lord schal dwelle in Syon.
Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”

< Joel 3 >