< Hosea 1 >

1 The word of the Lord that was maad to Osee, the sone of Bery, in the daies of Osie, Joathan, Achas, Ezechie, kingis of Juda, and in the daies of Jeroboam, sone of Joas, the kyng of Israel.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 The bigynnyng of the spekyng to the Lord in Osee. And the Lord seide to Osee, Go thou, take to thee a wijf of fornycaciouns, and make to thee sones of fornycaciouns, for the lond doynge fornicacioun schal do fornicacioun fro the Lord.
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 And he yede, and took Gomer, the douyter of Debelaym; and sche conseyuede, and childide a sone to hym.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 And the Lord seide to hym, Clepe thou the name of hym Jesrael; for yit a litil and Y schal visite the blood of Jesrael on the hous of Hieu, and Y schal make to reste the rewme of the hous of Israel.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 And in that dai Y schal al to-breke the bowe of Israel in the valei of Jesrael.
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 And sche conseyuede yit, and childide a douyter. And the Lord seide to hym, Clepe thou the name of hir With out merci, for Y schal no more leye to, for to haue merci on the hous of Israel, but bi foryetyng Y schal foryete hem.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 And Y schal haue merci on the hous of Juda, and Y schal saue hem in her Lord God; and Y schal not saue hem in bowe, and swerd, and batel, and in horsis, and in horse men, ether kniytis.
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 And he wenyde hir that was With out merci. And sche conseyuede, and childide a sone to hym.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 And he seide, Clepe thou his name Not my puple, for ye schulen not be my puple, and Y schal not be youre God.
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 And the noumbre of the sones of Israel schal be as grauel of the see, which grauel is with out mesure, and it schal not be noumbrid; and it schal be in the place, where it schal be seid to hem, Ye ben not my puple; it schal be seid to hem, Ye ben the sones of God lyuynge.
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 And the sones of Juda and the sones of Israel schulen be gaderid togidere, and thei schulen sette oon heed to hem silf, and thei schulen stie fro erthe, for the dai of Jesrael is greet.
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”

< Hosea 1 >