< 2 Samuel 4 >

1 Forsothe Isbosech, the sone of Saul, herde that Abner hadde falde doun in Ebron; and `hise hondis weren discoumfortid, and al Israel was disturblid.
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 Forsothe twei men, princes of theues, weren to the sone of Saul; name to oon was Baana, and name to the tother was Rechab, the sones of Remmon Berothite, of the sones of Beniamyn; for also Beroth is arettid in Beniamyn.
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 And men of Beroth fledden in to Gethaym; and thei weren comelyngis there `til to that tyme.
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 Forsothe a sone feble in feet was to Jonathas, the sone of Saul; forsothe he was fyue yeer eld, whanne the messanger cam fro Saul and Jonathas, fro Jezrael. Therfor his nurse took hym, and fledde; and whanne sche hastide to fle, sche felde doun, and the child was maad lame; and `he hadde a name Myphibosech.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 Therfor Rechab and Baana, sones of Remmon of Beroth, camen, and entriden in the hoot dai in to the hows of Isbosech, that slepte on his bed in myd dai, `and the womman oischer of the hous clensynge wheete, slepte strongli.
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 Forsothe thei entriden into the hows pryueli, and token eeris of whete; and Rechab, and Baana, his brother, smytiden Isbosech in the schar, and fledden.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 Sotheli whanne thei hadden entrid in to the hous, he slepte on his bedde in a closet; and thei smytiden and killiden hym; and whanne `his heed was takun, thei yeden bi the weie of deseert in al the nyyt.
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 And thei brouyten the heed of Isbosech to Dauid, in Ebron, and thei seiden to the kyng, Lo! the heed of Isbosech, sone of Saul, thin enemy, that souyte thi lijf; and the Lord yaf to dai to oure lord the kyng veniaunce of Saul and of his seed.
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 Forsothe Dauid answeride to Rechab, and Baana, his brother, the sones of Remmon of Beroth, and seide to hem, The Lord lyueth, that delyueride my lijf fro al angwisch;
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 for Y helde hym that telde to me, and seide, Saul is deed, which man gesside hym silf to telle prosperitees, and Y killide hym in Sichelech, to whom it bihofte me yyue meede for message;
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 hou myche more now, whanne wickid men han slayn a giltles man in his hows on his bed, schal I not seke his blood of youre hond, and schal Y do awey you fro erthe?
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 Therfor Dauid comaundide to his children, and thei killiden hem; and thei kittiden awei the hondis and `feet of hem, and hangiden hem ouer the cisterne in Ebron. Forsothe thei token the heed of Isbosech, and birieden in the sepulcre of Abner, in Ebron.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.

< 2 Samuel 4 >