< 1 Kings 1 >

1 And kyng Dauid wax eld, and hadde ful many daies of age; and whanne he was hilid with clothis, he was not maad hoot.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Therfor hise seruauntis seiden to hym, Seke we to oure lord the kyng a yong wexynge virgyn; and stonde sche bifor the kyng, and nursche sche hym, and slepe in his bosum, and make hoot oure lord the kyng.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Therfor thei souyten a yong wexyng virgyn, fair in alle the coostis of Israel; and thei founden Abisag of Sunam, and thei brouyten hir to the kyng.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Forsothe the damysel was ful fair, and sche slepte with the kyng, and mynystride to hym; forsothe the king knew not hir fleischli.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 Sotheli Adonye, sone of Agith, was reisid, and seide, Y schal regne. And he made to hym a chare, and knyytis, and fifti men, that runnen bifor hym.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 Nether his fadir repreuyde hym ony tyme, and seide, Whi `didist thou this? Forsothe also he was ful fair, the secounde child aftir Absolon; and his word was with Joab,
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 sone of Saruye, and with `Abiathar, preest, that helpiden the partis of Adonye.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Sotheli Sadoch, the preest, and Banaie, sone of Joiada, and Nathan, the prophete, and Semey, and Cerethi, and Ferethi, and al the strengthe of the oost of Dauid, weren not with Adonye.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Therfor whanne rammes weren offrid, and caluys, and alle fatte thingis, bisidis the stoon Zoelech, that was nyy the welle of Rogel, Adonye clepide alle hise britheren, sones of the kyng, and alle the men of Juda, seruauntis of the kyng.
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Sotheli `he clepide not Nathan, the profete, and Banaie, and alle stronge men, and Salomon, his brothir.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Therfor Nathan seide to Bersabee, modir of Salomon, Whether thou herdist, that Adonye, sone of Agith, regnede, and oure lord Dauid knoweth not this?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Now therfor come thou, take thou counsel of me, and saue thi lijf, and of Salomon thi sone.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Go thou, and entre to kyng Dauid, and seie thou to hym, Whether not thou, my lord the kyng, hast swore to me, thin handmaide, and seidist, that Salomon thi sone schal regne aftir me, and he schal sitte in my trone?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Whi therfor regneth Adonye? And yit while thou schalt speke there with the kyng, Y schal come aftir thee, and `Y schal fille thi wordis.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 Therfor Bersabee entride to the kyng in the closet; forsothe the kyng was ful eeld, and Abisag of Sunam `mynystride to hym.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Bersabee bowide hir silf, and worschipide the kyng; to whom the kyng seide, What wolt thou to thee?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 And sche answeride, and seide, My lord the kyng, thou hast swore to thin handmaide bi thi Lord God, Salomon thy sone schal regne aftir me, and he schal sitte in my trone;
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 and lo! Adonye hath regnede now, `while thou, my lord the kyng, knowist not;
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 he hath slayn oxis, and alle fatte thingis, and ful many rammes; and he clepide alle the sones of the king, also `Abiathar preest, and Joab, the prince of chyualri; but he clepide not Salomon, thi seruaunt.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Netheles, my lord the kyng, the iyen of al Israel biholden in to thee, that thou schewe to hem, who owith to sitte in thi trone, my lord the kyng, aftir thee;
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 and it schal be, whanne my lord the kyng hath slepte with hise fadris, Y and my sone Salomon schulen be synneris.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 `While sche spak yit with the king, Nathan, the prophete, cam.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 And thei telden to the kyng, and seiden, Nathan, the prophete, is present. And whanne he hadde entrid in the siyt of the kyng, and hadde worschipide hym lowli to erthe,
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Nathan seide, My lord the kyng, seidist thou, Adonye regne aftir me, and sitte he on my trone?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 For he cam doun to dai, and offride oxis, and fatte thingis, and ful many wetheris; and he clepide alle the sones of the kyng, also Abiathar, preest; and whanne thei eten, and drunken bifor hym, and seiden, Kyng Adonye lyue;
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 he clepide not me, thi seruaunt, and Sadoch, preest, and Banaie, sone of Joiada, and Salomon, thi sone.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Whether this word yede out fro my lord the kyng, and thou schewidist not to me, thi seruaunt, who schulde sitte on the trone of my lord the king after hym?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 And kyng Dauid answeride, and seide, Clepe ye Bersabee to me. And whanne sche hadde entrid bifor the kyng, and hadde stonde bifor hym, the kyng swoor,
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 and seide, The Lord lyueth, that delyueryde my lijf fro al angwisch;
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 for as Y swore to thee bi the Lord God of Israel, and seide, Salomon, thi sone, schal regne after me, and he schal sitte on my trone for me, so Y schal do to dai.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 And Bersabee, with the cheer cast doun in to erthe, worschipide the kyng, and seide, My lord the kyng Dauid lyue with outen ende.
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 And kyng Dauid seide, Clepe ye Sadoch, the preest, to me, and Nathan, the prophete, and Banaie, sone of Joiada. And whanne thei hadden entrid bifor the kyng,
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 the kyng seide to hem, Take with you the seruauntis of youre lord, and putte ye my sone Salomon on my mule, and lede ye hym in to Gyon.
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 And Sadoch, the preest, and Nathan, the profete, anoynte hym in to kyng on Israel and Juda; and ye schulen synge with a clarioun, and ye schulen seie, Lyue kyng Salomon!
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Ye schulen stie aftir hym, and ye schulen come to Jerusalem; and he schal sitte on my trone, and he schal regne for me; and Y schal comaunde to hym, that he be duyk on Israel and on Juda.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 And Banaie, sone of Joiada, answeride to the kyng, and seide, Amen, `that is, so be it, ether verili, ether feithfuli; so speke the Lord God of my lord the kyng.
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 As the Lord was with my lord the kyng, so be he with Salomon, and make he the trone of Salomon heiyere than the trone of my lord the kyng Dauid.
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Therfor Sadoch, the preest, yede doun, and Nathan, the prophete, and Banaie, sone of Joiada, and Cerethi, and Ferethi; and thei puttiden Salomon on the mule of Dauid, the kyng, and thei brouyten hym in to Gion.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 And Sadoch, the preest, took an horn of oile of the tabernacle, and anoyntide Salomon; and thei sungen with a clarioun; and al the puple seide, Lyue kyng Salomon!
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 And al the multitude stiede after hym, and the puple of men syngynge with pipis, and `of men beynge glad with greet ioye, `stiede aftir hym; and the erthe sownede of the cry of hem.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 Forsothe Adonye herde, and alle that weren clepid of hym to feeste; and thanne the feeste was endid. But also Joab seide, whanne the vois of trumpe was herd, What wole it to it silf the cry of the citee makynge noise?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 Yit the while he spak, Jonathan, sone of Abiathar, the preest, cam; to whom Adonye seide, Entre thou, for thou art a strong man, and tellynge goode thingis.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 And Jonathan answeride to Adonye, Nay; for oure lord the kyng Dauid hath ordeyned Salomon kyng;
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 and Dauid sente with Salomon Sadoch, the preest, and Nathan, the prophete, and Banaie, sone of Joiada, and Cerethi, and Ferethi; and thei puttiden Salomon on the mule of the kyng.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 And Sadoch, the preest, and Nathan, the prophete, anoyntiden hym kyng in Gion; and thei camen doun fro thennus beynge glad, and the citee sownede; this is the vois which ye herden.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 But also Salomon sittith on the trone of rewme;
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 and the seruauntis of the kyng entriden, and blessiden oure lord the kyng Dauid, and seiden, God make large the name of Salomon aboue thi name, and magnyfye his trone aboue thi trone. And kyng Dauid worschipide in his bed;
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 and ferthermore he spak these thingis, Blessid be the Lord God of Israel, that yaf to dai a sittere in my trone, while myn iyen seen.
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Therfor alle, that weren clepid of Adonye to feeste, weren aferd, and risiden, and ech man yede in to his weie.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Sotheli Adonye dredde Salomon, and roos, and yede in to the tabernacle of the Lord, and helde the horn of the auter.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 And thei telden to Salomon, and seiden, Lo! Adonye dredith the kyng Salomon, and holdith the horn of the auter, and seith, Kyng Salomon swere to me to dai, that he schal not sle his seruaunt bi swerd.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 And Salomon seide, If he is a good man, sotheli not oon heer of hym schal falle in to erthe; but if yuel be foundun in hym, he schal die.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Therfor kyng Salomon sente, and ledde `hym out fro the auter; and he entride, and worschipide kyng Salomon; and Salomon seide to hym, Go in to thin hows.
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Kings 1 >