< 2 Samuel 16 >

1 And whanne Dauid hadde passid a litil the cop of the hil, Siba, the child of Mysphobosech, apperide in to his comyng, with tweyne assis, that weren chargid with twei hundrid looues, and with an hundrid bundels of dried grapis, and with an hundrid gobetis of pressid figus, and with twei vessels of wyn.
Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
2 And the kyng seide to Siba, What wolen these thingis to hem silf? And Siba answeride, My lord the kyng, the assis ben to the meyneals of the kyng, that thei sitte; the looues and `figis pressid ben to thi children to ete; forsothe the wyn is, that if ony man faile in deseert, he drynke.
Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
3 And the kyng seide, Where is the sone of thi lord? And Siba answeride to the kyng, He dwellide in Jerusalem, `and seide, To dai the Lord of the hows of Israel schal restore to me the rewme of my fadir.
Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
4 And the kyng seide to Siba, Alle thingis that weren of Mysphibosech ben thine. And Siba seide, Y preye, fynde Y grace bifor thee, my lord the kyng.
Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
5 Therfor kyng Dauid cam `til to Bahurym, and lo! a man of the meynee of the hows of Saul, Semey bi name, sone of Gera, yede out fro thennus; he yede forth goynge out, and curside.
Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
6 And he sente stoonys ayens Dauid, and ayens alle seruauntis of kyng Dauid; forsothe al the puple, and alle fiyteris yeden at the riytside and at the left side of the king.
Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
7 Sotheli Semey spak so, whanne he curside the kyng, Go out, go out, thou man of bloodis, and man of Belial!
Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
8 The Lord hath yolde to thee al the blood of the hows of Saul, for thou rauyschedist the rewme fro hym; and the Lord yaf the rewme in to the hond of Absolon, thi sone; and lo! thin yuels oppressen thee, for thou art a man of blodis.
Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
9 Forsothe Abisay, the sone of Saruye, seide to the kyng, Whi cursith this dogge, that schal die, my lord the kyng? Y schal go, and Y schal girde of his heed.
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
10 And the kyng seide, Ye sones of Saruye, what is to me and to you? Suffre ye hym, that he curse; for the Lord comaundide to hym, that he schulde curse Dauid; and who is he that dare seie, Whi dide he so?
Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
11 And the kyng seide to Abysay, and to alle hise seruauntis, Lo! my sone, that yede out of my wombe, sekith my lijf; hou myche more now this sone of Gemyny? Suffre ye hym, that he curse bi comaundement of the Lord;
Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
12 if in hap the Lord biholde my turmentyng, and yelde good to me for this `cursyng of this dai.
Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
13 Therfor Dauid yede, and hise felowis, bi the weie with hym; forsothe Semey yede bi the slade of the hil `bi the side ayens hym; and curside, and sente stoonus ayens him, and spreynte erthe.
Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
14 And so `Dauid the king cam, and al the puple weery with hym, and thei weren refreischid there.
Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
15 Forsothe Absolon, and al the puple of Israel entriden in to Jerusalem, but also Achitofel with hym.
Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
16 Sotheli whanne Chusi of Arath, the frend of Dauid, hadde come to Absolon, he spak to Absolon, Heil, kyng! heil, kyng!
Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
17 To whom Absolon seide, This is thi grace to thi freend; whi yedist thou not with thi freend?
Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
18 And Chusi answeride to Absolon, Nay, for Y shal be seruaunt of hym, whom the Lord hath chose, and al this puple, and al Israel; and Y schal dwelle with him.
Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
19 But that Y seie also this, to whom schal Y serue? whethir not to the sone of the kyng? as Y obeiede to thi fadir, so Y schal obeie to thee.
Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
20 Forsothe Absolon seide to Achitofel, Take ye counsel, what we owen to do.
Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
21 And Achytofel seide to Absolon, Entre thou to the concubyns of thi fadir, whiche he lefte to kepe the hows; that whanne al Israel herith, that thou hast defoulid thi fadir, the hondis of hem be strengthid with thee.
Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
22 Therfor thei tildeden Absolon a tabernacle in the soler, and he entride to the concubyns of his fadir bifor al Israel.
Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
23 Sotheli the counsel of Achitofel, which he yaf in tho daies, was as if a man counselide God; so was al the counsel of Achitofel, bothe whanne he was with Dauid, and whanne he was with Absolon.
Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.

< 2 Samuel 16 >