< 2 Samuel 10 >

1 Forsothe it was doon aftir these thingis, that Naas, kyng of the sones of Amon, diede; and Anoon, his sone, regnede for hym. And Dauid seide,
Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Y schal do mercy with Anon, the sone of Naas, as his fadir dide mercy with me. Therfor Dauid sente coumfortynge hym by hise seruauntis on the deeth of the fadir. Sotheli whanne the seruauntis of Dauid hadden come in to the lond of the sones of Amon,
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
3 princes of the sones of Amon seiden to Anon, her lord, Gessist thou that for the onour of thi fadir Dauid sente coumfortouris to thee; and not herfor Dauid sente hise seruauntis to thee, that he schulde aspie, and enserche the citee, and distrie it?
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Therfor Anoon took the seruauntis of Dauid, and schauyde half the part of `the beerd of hem, and he kittide awey the myddil clothis of hem `til to the buttokis; and lefte hem.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
5 And whanne this was teld to Dauid, he sente in to the comyng of hem, for the men weren schent ful vilensly. And Dauid comaundide to hem, Dwelle ye in Jerico, til youre beerd wexe, and thanne turne ye ayen.
Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Sotheli the sones of Amon sien, that thei hadden do wrong to Dauid, and thei senten, and hiriden bi meede Roob of Sirye, and Soba of Sirie, twenti thousynde of foot men, and of kyng Maacha, a thousynde men, and of Istob twelue thousynde of men.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
7 And whanne Dauid hadde herd this, he sent Joab and al the oost of fiyteris.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
8 Therfor the sones of Amon yeden out, and dressiden scheltrun bifor hem in the entryng of the yate. Forsothe Soba, and Roob of Sirie, and Istob, and Maacha weren asidis half in the feeld.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
9 Therfor Joab siy, that batel was maad redi ayens hym, bothe euene ayens and bihynde the bak; and he chees to hym silf of alle the chosun men of Israel, and ordeynede scheltrun ayens Sirus.
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
10 Forsothe he bitook to Abisai, his brothir, the tother part of the puple, which dresside scheltrun ayens the sones of Amon.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
11 And Joab seide, If men of Sirie han the maistrie ayens me, thou schalt be to me in to help; sotheli if the sones of Amon han the maistrie ayens thee, Y schal helpe thee;
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
12 be thou a strong man, and fiyte we for oure puple, and for the citee of oure God; forsothe the Lord schal do that, that is good in his siyt.
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
13 Therfor Joab and his puple that was with hym, bigan batel ayens men of Sirie, whiche fledden anoon fro his face.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
14 Forsothe the sones of Amon sien, that men of Sirie hadden fled; and thei fledden also fro the face of Abisai, and entriden in to the citee; and Joab turnede ayen fro the sones of Amon, and cam in to Jerusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
15 Forsothe men of Sirye sien that thei hadden feld bifor Israel, and thei weren gaderid to gidere.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
16 And Adadezer sente, and ledde out men of Sirie that weren biyende the flood, and he brouyte the oost of hem; sotheli Sobach, mayster of the chyualrie of Adadezer, was the prince of hem.
Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
17 And whanne this was teld to Dauid, he drow togidere al Israel, and passide Jordan, and cam in to Helama. And men of Sirie dressiden scheltrun ayens Dauid, and fouyten ayens hym.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
18 And Sireis fledden fro the face of Israel; and Dauid killide of Sireis seuene hundrid charis, and fourti thousynde of knyytis; and he smoot Sobach, the prince of chyualrie, which was deed anoon.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
19 Forsothe alle kyngis, that weren in the help of Adadezer, siyen that thei weren ouercomun of Israel, and thei maden pees with Israel, and serueden hem; and Sireis dredden to yyue help to the sones of Amon.
Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< 2 Samuel 10 >