< 2 Samuel 1 >

1 Forsothe it was doon, after that Saul was deed, that Dauid turnede ayen fro the sleyng of Amalech, and dwellide twei daies in Sichelech.
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 Forsothe in the thridde dai a man apperide, comynge fro the castels of Saul with the cloth to-rent, and his heed spreynt with dust; and as he cam to Dauid, he felde on his face, and worschipide.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 And Dauid seide to hym, Fro whennus comest thou? Which seide to Dauid, Y fledde fro the castels of Israel.
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 And Dauid seide to hym, What is the word which is doon; schewe thou to me. And he seide, The puple fledde fro the batel, and many of the puple felden, and ben deed; but also Saul, and Jonathas, his sonne, perischyden.
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 And Dauid seide to the yong man, that telde to hym, Wherof woost thou, that Saul is deed, and Jonathas, his sonne?
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 And the yong man seide, that telde to hym, Bi hap Y cam in to the hil of Gelboe, and Saul lenyde on his spere; forsothe charis and knyytis neiyiden to hym;
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 and he turnede bihynde his bak, `and siy me, and clepide. To whom whanne Y hadde answeride, Y am present; he seide to me, Who art thou?
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 And Y seide to hym, Y am a man of Amalech.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 And he spak to me, Stonde thou on me, and sle me; for angwischis holden me, and yit al my lijf is in me.
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 And Y stood on hym, and Y killide hym; for Y wiste that he myyte not lyue aftir the fallyng; and Y took the diademe, that was in his heed, and the bye fro his arm, and Y brouyte hidur to thee, my lord.
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 Forsothe Dauid took and to-rente hise clothis, and the men that weren with hym;
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 and thei weiliden, and wepten, and fastiden `til to euentid, on Saul, and Jonathas, his sone, and on the puple of the Lord, and on the hows of Israel, for thei hadden feld bi swerd.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 And Dauid seide to the yong man, that telde to him, Of whennus art thou? And he answeride, Y am the sone of a man comelyng, of a man of Amalech.
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 And Dauid seide to him, Whi dreddist thou not to sende thine hond, that thou schuldist sle the crist of the Lord?
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 And Dauid clepide oon of hise children, and seide, Go thou, and falle on hym. Which smoot that yong man, and he was deed.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 And Dauid seide to hym, Thi blood be on thin heed; for thi mouth spak ayens thee, and seide, Y killide the crist of the Lord.
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 Forsooth Dauid biweilide sych a weilyng on Saul, and on Jonathas, his sone;
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 and comaundide, that thei schulden teche the sones of Juda weilyng, as it is writun in the Book of Just Men. And Dauid seyde, Israel, biholde thou, for these men that ben deed, woundid on thin hiye placis;
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 the noble men of Israel ben slayn on thin hillis.
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Hou felden stronge men? nyle ye telle in Geth, nether telle ye in the weilottis of Ascolon; lest perauenture the douytris of Filisteis be glad, lest the douytris of vncircumcidid men `be glad.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 Hillis of Gelboe, neither dew nethir reyn come on you, nether the feeldis of firste fruytis be; for the scheeld of stronge men was cast awey there, the scheeld of Saul, as `if he were not anoyntid with oile.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 Of the blood of slayn men, of the fatnesse of strong men, the arewe of Jonathas yede neuer abak, and the swerd of Saul turnede not ayen void.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Saul and Jonathas amyable, and fair in her lijf, weren not departid also in deeth; thei weren swiftere than eglis, strongere than liouns.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 Douytris of Israel, wepe ye on Saul, that clothide you with fyn reed colourid in delicis, that yaf goldun ournementis to youre atyre.
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 Hou `felden doun stronge men in batel?
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Jonathas was slayn in the hiye places. Y make sorewe on thee, my brother Jonathas, ful fair, `and amyable more than the loue of wymmen; as a modir loueth oon aloone sone, so Y louyde thee.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 Hou therfor `felden doun stronge men, and armeris of batel perischide?
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< 2 Samuel 1 >