< 2 Kings 25 >

1 Forsothe it was don in the nynthe yeer of his rewme, in the tenthe moneth, in the tenthe dai of the moneth, Nabugodonosor, kyng of Babiloyne, cam, he, and al his oost, in to Jerusalem; and thei cumpassiden it, and bildiden `stronge thingis in the cumpass therof.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 And the citee was closid, and cumpassid, `til to the eleuenthe yeer of king Sedechie,
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 in the nynthe day of the monethe; and hungur `hadde maistrie in the citee, and `breed was not to the puple of the lond.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 And the citee was brokun, and alle men werriours fledden in the niyt bi the weie of the yate, which is bitwixe the double wal, to the gardyn of the kyng; sotheli Caldeis bisegiden the citee `bi cumpas. Therfor Sedechie fledde bi the weie that ledith to the feeldi placis of the wildirnesse;
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 and the oost of Caldeis pursuede the king, and it took him in the pleyn of Jerico; and alle the werriours, that weren with him, weren scaterid, and leften him.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 Therfor thei ledden the king takun to the king of Babiloyne, in to Reblatha, which spak dom with him, `that is, with Sedechie.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 Sotheli he killide the sones of Sedechie bifor him, and puttide out his iyen, and boond him with chaynes, and ledde him in to Babiloyne.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 In the fifthe monethe, in the seuenthe dai of the monethe, thilke is the nyntenthe yeer of the king of Babiloyne, Nabuzardan, prince of the oost, seruaunt of the king of Babiloyne, cam in to Jerusalem;
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 and he brente the hows of the Lord, and the hows of the king, and the housis of Jerusalem, and he brente bi fier ech hows;
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 and al the oost of Caldeis, that was with the prince of knyytis, distriede the wallis of Jerusalem `in cumpas.
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 Forsothe Nabuzardan, prince of the chyyualrie, translatide the tother part of the puple, that dwellide in the citee, and the fleeris, that hadden fled ouer to the king of Babiloyne, and the residue comyn puple;
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 and he lefte of the pore men of the lond vyntilieris, and erthe tilieris.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 Sotheli Caldeis braken the brasun pilers, that weren in the temple, and the foundementis, and the see of bras, that was in the hous of the Lord; and thei translatiden al the metal in to Babiloyne.
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 And thei token the pottis of bras, and trullis, and fleisch hokis, and cuppis, and morteris, and alle brasun vessels, in whiche thei mynystriden;
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 also and censeris, and violis. The prince of the chyualrie took tho that weren of gold, and tho that weren of siluer,
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 that is, twei pileris, o see, and the foundementis, whiche king Salomon hadde maad `in to the temple of the Lord; and no weiyte was of metal of alle the vessels.
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 O piler hadde eiyten cubitis of hiyte, and a brasun pomel on it of the heiyte of thre cubitis, and a werk lijk a net, and pomgarnadis on the pomel of the piler, alle thingis of bras; and the secounde piler hadde lijk ournyng.
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 Also the prince of the chyualrie took Saraie, the firste preest, and Sophony, the secunde prest,
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 and thre porteris, and oon onest seruaunt of the citee, that was a souereyn ouer men werriours, and fyue men `of hem that stoden bifor the king, whiche he foond in the citee; and he took Sopher, the prince of the oost, that preuide yonge knyytis, `ether men able to batel, of the puple of the lond, and sixe men of the comyns, that weren foundyn in the citee;
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 whiche Nabuzardan, prince of the chyualrie, took, and ledde to the king of Babiloyne, in to Reblatha.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 And the kyng of Babiloyne smoot hem, and killide hem in Reblatha, in the lond of Emath; and Juda was translatid fro his lond.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 Sotheli he made souereyn Godolie, sone of Aicham, sone of Saphan, to the puple that was left in the lond of Juda; which puple Nabugodonosor, king of Babiloyne, hadde left.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 And whanne alle the duykis of knyytis hadde herd these thingis, thei, and the men that weren with hem, that is, that the king of Babiloyne hadde ordeyned Godolie, thei camen `to Godolie, in Maspha, Ismael, sone of Nathanye, and Johannan, sone of Charee, and Saraie, sone of Thenameth of Nechophat, and Jeconye, sone of Machati, thei, and Machat, and the felowis of hem.
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 And Godolie swoor to hem, and to the felowis of hem, and seide, Nyle ye drede to serue the Caldeis; dwelle ye in the lond, and serue ye the king of Babiloyne, and it schal be wel to you.
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 Forsothe it was don in the seuenthe monethe, `that is, sithen Godolie was maad souereyn, Hismael, the sone of Nathanye, sone of Elysama, of the `kyngis seed, cam, and ten men with hym, and thei smytiden Godolie, which diede; but also thei smytiden Jewis and Caldeis, that weren with hym in Maspha.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 And al the puple roos fro litil `til to greet, and the prynces of knyytis, and camen in to Egipt, and dredden Caldeis.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 Therfor it was doon in the seuenthe and threttithe yeer of transmigracioun, `ether passyng ouer, of Joakyn, kyng of Juda, in the tweluethe monethe, in the seuene and twentithe dai of the monethe, Euylmeradach, kyng of Babiloyne, in the yeer in which he bigan to regne, reiside the heed of Joakyn, kyng of Juda,
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 fro prisoun, and spak to hym benygneli; and he settide the trone of Joakyn aboue the trone of kyngis, that weren with hym in Babilonye.
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 And he chaungide `hise clothis, whiche he hadde in prisoun; and he eet breed euer in the siyt of Euylmeradach, in alle the daies of his lijf.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 Also Euylmeradach ordeynede sustenaunce `to hym with out ceessyng; which sustenaunce also was youun of the kyng to hym bi alle daies, and in alle the daies of his lijf.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

< 2 Kings 25 >