< 2 Kings 19 >

1 And whanne kyng Ezechie hadde herd these thingis, he to-rente his clothis, and was hilid with a sak; and he entride in to the hous of the Lord.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 And he sente Eliachym, souereyn of the hous, and Sobna, scryueyn, and elde men of the preestis, hilid with sackis, to Ysaie, the prophete, sone of Amos.
Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Whiche seiden, Ezechie seith these thingis, This dai is a dai of tribulacioun, and of blamyng, and of blasfemye; sones camen `til to the childberyng, and the `traueler of childe hath not strengthis.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
4 If perauenture thi Lord God here alle the wordis of Rabsaces, whom the kyng of Assiryens, his lord sente, that he schulde dispise the Lord lyuynge, and repreue bi wordis, whiche thi Lord God herde; and make thou preier for these relikis, that ben foundun.
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
5 Therfor the seruauntis of kyng Ezechie camen to Isaie;
Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 and Isaie seide to hem, Seie ye these thingis to youre lord, The Lord seith these thingis, Nyle thou drede of the face of wordis whiche thou herdist, bi whiche the children of the kyng of Assiriens blasfemeden me.
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Lo! Y schal sende to hym a spirit, and he schal here a messanger, and he schal turne ayen in to his lond; and Y schal caste hym doun bi swerd in his owne lond.
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 Therfor Rabsaces turnede ayen, and foond the kyng of Assiriens fiytynge ayens Lobna; for he hadde herd, that the kyng hadde go awei fro Lachis.
Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 And whanne he hadde herd of Theracha, kyng of Ethiope, `men seyynge, Lo! he yede out, that he fiyte ayens thee; that he schulde go ayens `that kyng, he sente messangeris to Ezechie,
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 and seide, Seie ye these thingis to Ezechie, kyng of Juda, Thi Lord God, in whom thou hast trist, disseyue not thee, nether seie thou, Jerusalem schal not be `bitakun in to the hondis of the kyng of Assiriens;
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 for thou thi silf herdist what thingis the kyngis of Assiriens diden in alle londis, hou thei wastiden tho; whether therfor thou aloone maist be delyuered?
Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
12 Whether the goddis of hethene men delyueriden alle men whiche my fadris distrieden, that is, Gozam, and Aran, and Reseph, and the sones of Eden, that weren in Thelassar?
Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
13 Where is the kyng of Emath, and the kyng of Arphat? and the kyng of the cytee of Sepharuaym, of Ana, and of Aua?
Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
14 Therfor whanne Ezechie hadde take the lettris fro the hond of messangeris, and hadde red tho, he stiede in to the hows of the Lord, and spredde abrood tho bifor the Lord;
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 and preiede in his siyt, and seide, Lord God of Israel, that sittist on cherubym, thou art God aloone of alle kyngis of erthe; thou madist heuene and erthe.
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Bowe thin eere, and here; opyn thin iyen, Lord, and se; and here alle the wordis of Senacherib, which sente, that he schulde dispise `to vs `God lyuynge.
Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
17 Verili, Lord, the kynges of Assiriens distrieden hethene men, and the londis of alle men,
“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
18 and senten the goddis of hem in to fier; for thei weren not goddis, but werkis of `hondis of men, of tre and stoon; and thei losten `tho goddis.
Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
19 Now therfor, oure Lord God, make vs saaf fro the hond of hem, that alle rewmes of erthe wite that thou art the Lord God aloone.
Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
20 Forsothe Isaie, sone of Amos, sente to Ezechie, and seide, The Lord God of Israel seith these thingis, Y haue herd tho thingis, whiche thou preidist me on Sennacherib, king of Assiriens.
Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
21 This is the word, which the Lord spak of hym, Thou virgyn douytir of Syon, he dispiside thee, and scornyde thee; thou douyter of Jerusalem, he mouyde his heed aftir thi bak.
Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Sennacherib, whom `dispisidist thou, and whom `blasfemedist thou? Ayens whom hast thou reisid thi vois, and hast reisid thin iyen an hiye? Ayens the hooli of Israel.
Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Bi the hond of thi seruauntis thou dispisidist the Lord, and seidist, In the multitude of my charys Y stiede in to the hiye thingis of hillis, in the hiynesse of Liban, and kittide doun the hiye cedris therof, and the chosyn beechis therof; and Y entride `til to the termes therof,
Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 and Y kittide doun the forest of Carmele therof; and Y drank alien watris, and Y made drie with the steppis of `the feet of myn `alle watris closid.
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
25 Whether thou herdist not, what Y made at the bigynnyng? Fro elde daies Y made it, and now Y haue brouyt forth; and strengthid citees of fiyteris schulen be in to fallyng of hillis.
“‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
26 And thei that sitten meke of hond in tho, trembliden togidere, and ben schent; thei ben maad as the hei of the feeld, and as grene eerbe of roouys, which is dried, bifor that it cam to ripenesse.
Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
27 And Y bifor knew thi dwellyng, and thi goyng out, and thin entryng, and thi weie, and thi woodnesse ayens me.
“‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 Thou were wood ayens me, and thi pride stide in to myn eeris; therfor Y schal putte a cercle in thi nosethirlis, and a bernacle in thi lippis, and Y schal lede thee ayen in to the weie bi which thou camest.
Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
29 Forsothe, Ezechie, this schal be a signe `to thee; ete thou in this yeer that, that thou fyndist; forsothe in the secounde yeer tho thingis, that growen bi her owne wille; sotheli in the thridde yeer sowe ye, and repe ye, plaunte ye vyneris, and ete the fruytis of tho.
“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 And what euer thing schal be residue of the hows of Juda, it schal sende root dounward, and schal make fruyt vpward.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 For relikis schulen go out of Jerusalem, and that, that schal be sauyd, `schal go out of the hil of Syon; the feruent loue of the Lord of oostis schal do this.
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
32 Wherfor the Lord seith these thingis of the kyng of Assiriens, He schal not entre in to this citee, nethir he schal sende an arowe in to it, nether scheeld shal occupie it, nether strengthing, ethir bisegyng, schal cumpasse it.
“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 He schal turne ayen bi the weie `bi which he cam, and he schal not entre in to this citee, seith the Lord;
Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
34 and Y schal defende this citee, and Y schal saue it for me, and for Dauid, my seruaunt.
Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
35 Therfor it was don, in that niyt the aungel of the Lord cam, and smoot in the castels of Assiryens an hundrid foure score and fyue thousynde. And whanne Sennacherib hadde rise eerli, he siy alle bodies of deed men; and he departide, and yede awei.
Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
36 And Sennacherib, the kyng of Assiriens, turnede ayen, and dwellide in Nynyue.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
37 And whanne he worschipide in the temple Nestrach his god, Adramelech and Sirasar, his sones, killide hym with swerd; and thei fledden in to the lond of Armenyes; and Asaradon, his sone, regnyde for hym.
Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kings 19 >