< 1 Samuel 7 >

1 Therfor men of Cariathiarym camen, and ledden ayen the arke of the Lord, and brouyten it in to the hows of Amynadab in Gabaa. Sotheli thei halewiden Eleazar his sone, that he schulde kepe the ark of the Lord.
Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
2 And it was doon, fro which dai `the arke of the Lord dwellide in Caryathiarym, daies weren multiplied; for the twentithe yeer was now, after that Samuel bigan to teche the puple; and al Israel restide aftir the Lord.
Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
3 Forsothe Samuel spak to al the hows of Israel, and seide, If in al youre herte ye turnen ayen to the Lord, do ye awei alien goddis, Balym and Astaroth, fro the myddis of you; and make ye redi youre hertis to the Lord, and serue ye hym aloone; and he schal delyuere you fro the hond of Filisteis.
Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
4 Therfor the sones of Israel diden awey Baalym and Astoroth, and serueden the Lord aloone.
Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
5 Forsothe Samuel seide, Gadere ye al Israel in to Masphat, that Y preie the Lord for you.
Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
6 And thei camen togidere in to Masphat, and thei drowen watir, and shedden out in the `siyt of the Lord; and thei fastiden in that day, and seiden, Lord, we synneden to thee. And Samuel demyde the sones of Israel in Masphat.
Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
7 And Filisteis herden that the sones of Israel weren gaderid in Masphat; and the princes of Filisteis stieden to Israel. And whanne the sones of Israel hadden herd this, thei dredden of the face of Filisteis.
Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
8 And `thei seiden to Samuel, Ceesse thou not to crye for vs to oure Lord God, that he saue vs fro the `hoond of Filisteis.
Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
9 Forsothe Samuel took o soukynge lomb, and offride that hool in to brent sacrifice to the Lord. And Samuel criede to the Lord for Israel; and the Lord herde hym.
Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
10 Forsothe it was doon, whanne Samuel offryde brent sacrifice, that Filisteis bigunnen batel ayens Israel. Sotheli the Lord thundride with greet thundur in that dai on Filisteis, and made hem aferd; and thei weren slayn of the sones of Israel.
Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
11 And the sones of Israel yeden out of Masphat, and pursueden Filisteis, and smytiden hem `til to the place that was vndur Bethachar.
Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
12 Forsothe Samuel took o stoon, and puttide it bitwixe Masphat, and bitwixe Sen; and he clepide the name of that place The stoon of help. And he seide, Hidir to the Lord helpide vs.
Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
13 And Filisteis weren maad low, and addiden no more to come in to the termes of Israel. And so the `hond of the Lord was maad on Filisteis in alle the daies of Samuel.
Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
14 And the citees whiche the Filisteis token fro Israel, weren yoldun to Israel, fro Accaron `til to Geth and `hise termes; and the Lord delyuerede Israel fro the hond of Filisteis; and pees was bitwixe Israel and Ammorrey.
Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
15 Also Samuel demyde Israel in alle the daies of his lijf, that is, `til to the ordeynyng `and confermyng of Saul;
Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
16 and he yede bi `alle yeeris, and cumpasside Bethel, and Galgal, and Masphat, and he demyde Israel in the forseid places.
Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
17 And he turnede ayen in to Ramatha, for his hows was there; and he demyde Israel there, and he bildide there also an auter to the Lord.
Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 7 >