< 1 Samuel 6 >

1 Therfor the arke of the Lord was in the cuntrei of Filisteis bi seuene monethis;
Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
2 and aftir these thingis Filisteis clepiden preestis and false dyuynours, and seiden, What schulen we do of the arke of God? Shewe ye to vs, hou we schulen sende it in to his place.
Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
3 Whiche seiden, If ye senden ayen the arke of God of Israel, nyle ye delyuere it voide, but yelde ye to hym that, that ye owen for synne; and thanne ye schulen be heelid, and ye schulen wite, whi `his hond goith not awei fro you.
Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
4 And thei seiden, What is it, that we owen to yelde to hym for trespas?
Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
5 And thei answeriden to hem, Bi the noumbre of prouynces of Filisteis ye schulen make fyue goldun ersis, and fyue goldun myis; for o veniaunce was to alle you and to youre `wise men, ether princes. And ye schulen make the licnesse of youre ersis, and the licnesse of myis that distriede youre lond; and ye schulen yyue glorie to God of Israel, if in hap he withdrawe his hond fro you, and fro youre goddis, and fro youre lond.
Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
6 Whi maken ye heuy youre hertis, as Egipt, and Farao `made heuy his herte? Whether not after that he was smytun, thanne he delyuerede hem, and thei yeden forth?
Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
7 Now therfor take ye, and make o newe wayn, and ioyne ye twei kien hauynge caluys, on whiche kyen no yok was put; and close ye her calues at hoome.
“Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
8 And ye schulen take the arke of the Lord, and ye schulen sette in the wayn; and ye schulen put in a panyere at the side therof the goldun vessels, whiche ye payeden to hym for trespas; and delyuere ye the arke, that it go.
Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
9 And ye schulen biholde, and sotheli if it stieth ayens Bethsames bi the weie of `hise coostis, `he dide to you this greet yuel; but if nay, we schulen wite `for his hond touchide not vs, but `if it bifelde bi hap.
Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
10 Therfor thei diden in this manere; and thei token twei kien that yauen mylk to caluys, and ioyneden to the wayn; and thei closiden her caluys at hoome.
Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
11 And thei puttiden the arke of God on the wayn, and `thei puttiden the panyere, that hadde the goldun myis, and the licnesse of ersis `on the wayn.
Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
12 Sotheli the kien yeden streiytli bi the weie that ledith to Bethsames; and tho yeden in o weie goynge and lowynge, and bowiden not nether to the riyt side nether to the left side; but also the wise men of Filisteis sueden `til to the termes of Bethsames.
Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
13 Forsothe men of Bethsames repiden whete in the valey, and thei reisiden the iyen, and sien the arke, and thei weren ioyful, whanne thei hadden sien `the arke.
Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
14 And the wayn cam in to the feelde of Josue of Bethsames, and stood there. Forsothe a greet stoon was there; and thei kittiden `the trees of the wayn, and puttiden the kien `on tho trees, a brent sacrifice to the Lord.
Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
15 Sotheli dekenes token doun the arke of God, and the panyere, that was bisidis it, where ynne the goldun vessels weren; and thei settiden on the greet stoon. Forsothe the men of Bethsames offriden brent sacrifices, and offriden slayn sacrifices in that dai `to the Lord.
Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
16 And fyue princes of Filisteis sien, and turneden ayen in to Accoron in that dai.
Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
17 Sotheli these ben the goldun ersis, whiche the Filisteis yeldiden to the Lord for trespas; Azotus yeldide oon; Gaza yeldide oon; Ascolon yeldide oon; Geth yeldide oon; Accaron yeldide oon;
Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
18 and Filisteis yeldiden golden myis bi the noumbre of `citees of Filisteis of fyue prouynces, fro a wallid citee `til to `a town that was with out wal, and `til to the greet Abel, `on which thei puttiden the arke of the Lord, that was there `til in that dai in the feeld of Josue of Bethsames.
Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
19 Forsothe the Lord smoot of the men of Bethsames, for thei hadden seyn the arke of the Lord, and he smoot of the puple seuenti men, and fifty thousynde of the porail. And the puple morenyde, for the Lord hadde smyte `the puple with greet veniaunce.
Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
20 And men of Bethsames seiden, Who schal now stonde in the siyt of the Lord God of this hooli thing, and to whom schal it stie fro vs?
Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
21 And thei senten messangeris to the dwelleris of Cariathiarym, and seiden, Filisteis han brouyt ayen the arke of the Lord; come ye doun, and lede it ayen to you.
Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”

< 1 Samuel 6 >