< Psalms 72 >

1 By Solomon. God, give the king your justice; your righteousness to the royal son.
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 He will judge your people with righteousness, and your poor with justice.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 The mountains shall bring prosperity to the people. The hills bring the fruit of righteousness.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 He will judge the poor of the people. He will save the children of the needy, and will break the oppressor in pieces.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 They shall fear you while the sun endures; and as long as the moon, throughout all generations.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 He will come down like rain on the mown grass, as showers that water the earth.
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 In his days, the righteous shall flourish, and abundance of peace, until the moon is no more.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 He shall have dominion also from sea to sea, from the River to the ends of the earth.
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 Those who dwell in the wilderness shall bow before him. His enemies shall lick the dust.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 The kings of Tarshish and of the islands will bring tribute. The kings of Sheba and Seba shall offer gifts.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 Yes, all kings shall fall down before him. All nations shall serve him.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 For he will deliver the needy when he cries; the poor, who has no helper.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 He will have pity on the poor and needy. He will save the souls of the needy.
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 He will redeem their soul from oppression and violence. Their blood will be precious in his sight.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 He will live; and Sheba’s gold will be given to him. Men will pray for him continually. They will bless him all day long.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Abundance of grain shall be throughout the land. Its fruit sways like Lebanon. Let it flourish, thriving like the grass of the field.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 His name endures forever. His name continues as long as the sun. Men shall be blessed by him. All nations will call him blessed.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Praise be to the LORD God, the God of Israel, who alone does marvelous deeds.
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 Blessed be his glorious name forever! Let the whole earth be filled with his glory! Amen and amen.
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 This ends the prayers by David, the son of Jesse.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

< Psalms 72 >