< Psalms 113 >

1 Praise the LORD! Praise, you servants of the LORD, praise the LORD’s name.
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 Blessed be the LORD’s name, from this time forward and forever more.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 From the rising of the sun to its going down, the LORD’s name is to be praised.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 The LORD is high above all nations, his glory above the heavens.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Who is like the LORD, our God, who has his seat on high,
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 who stoops down to see in heaven and in the earth?
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 He raises up the poor out of the dust, and lifts up the needy from the ash heap,
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 that he may set him with princes, even with the princes of his people.
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 He settles the barren woman in her home as a joyful mother of children. Praise the LORD!
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Psalms 113 >