< Psalms 122 >

1 A Song of Ascents. By David. I was glad when they said to me, “Let’s go to the LORD’s house!”
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Our feet are standing within your gates, Jerusalem!
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 Jerusalem is built as a city that is compact together,
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 where the tribes go up, even the LORD’s tribes, according to an ordinance for Israel, to give thanks to the LORD’s name.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 For there are set thrones for judgment, the thrones of David’s house.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Pray for the peace of Jerusalem. Those who love you will prosper.
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Peace be within your walls, and prosperity within your palaces.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 For my brothers’ and companions’ sakes, I will now say, “Peace be within you.”
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 For the sake of the house of the LORD our God, I will seek your good.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

< Psalms 122 >