< Proverbs 27 >

1 Don’t boast about tomorrow; for you don’t know what a day may bring.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Let another man praise you, and not your own mouth; a stranger, and not your own lips.
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 A stone is heavy, and sand is a burden; but a fool’s provocation is heavier than both.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Wrath is cruel, and anger is overwhelming; but who is able to stand before jealousy?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Better is open rebuke than hidden love.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 The wounds of a friend are faithful, although the kisses of an enemy are profuse.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 A full soul loathes a honeycomb; but to a hungry soul, every bitter thing is sweet.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 As a bird that wanders from her nest, so is a man who wanders from his home.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Perfume and incense bring joy to the heart; so does earnest counsel from a man’s friend.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Don’t forsake your friend and your father’s friend. Don’t go to your brother’s house in the day of your disaster. A neighbor who is near is better than a distant brother.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Be wise, my son, and bring joy to my heart, then I can answer my tormentor.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 A prudent man sees danger and takes refuge; but the simple pass on, and suffer for it.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Take his garment when he puts up collateral for a stranger. Hold it for a wayward woman!
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 He who blesses his neighbor with a loud voice early in the morning, it will be taken as a curse by him.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 A continual dropping on a rainy day and a contentious wife are alike:
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 restraining her is like restraining the wind, or like grasping oil in his right hand.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Iron sharpens iron; so a man sharpens his friend’s countenance.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 Whoever tends the fig tree shall eat its fruit. He who looks after his master shall be honored.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Like water reflects a face, so a man’s heart reflects the man.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 Sheol and Abaddon are never satisfied; and a man’s eyes are never satisfied. (Sheol h7585)
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
21 The crucible is for silver, and the furnace for gold; but man is refined by his praise.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Though you grind a fool in a mortar with a pestle along with grain, yet his foolishness will not be removed from him.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Know well the state of your flocks, and pay attention to your herds,
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 for riches are not forever, nor does the crown endure to all generations.
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 The hay is removed, and the new growth appears, the grasses of the hills are gathered in.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 The lambs are for your clothing, and the goats are the price of a field.
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 There will be plenty of goats’ milk for your food, for your family’s food, and for the nourishment of your servant girls.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

< Proverbs 27 >