< Job 9 >

1 Then Job answered,
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 “Truly I know that it is so, but how can man be just with God?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 If he is pleased to contend with him, he can’t answer him one time in a thousand.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 God is wise in heart, and mighty in strength. Who has hardened himself against him and prospered?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 He removes the mountains, and they don’t know it, when he overturns them in his anger.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 He shakes the earth out of its place. Its pillars tremble.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 He commands the sun and it doesn’t rise, and seals up the stars.
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 He alone stretches out the heavens, and treads on the waves of the sea.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 He makes the Bear, Orion, and the Pleiades, and the rooms of the south.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 He does great things past finding out; yes, marvelous things without number.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Behold, he goes by me, and I don’t see him. He passes on also, but I don’t perceive him.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Behold, he snatches away. Who can hinder him? Who will ask him, ‘What are you doing?’
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 “God will not withdraw his anger. The helpers of Rahab stoop under him.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 How much less will I answer him, and choose my words to argue with him?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Though I were righteous, yet I wouldn’t answer him. I would make supplication to my judge.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 If I had called, and he had answered me, yet I wouldn’t believe that he listened to my voice.
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 For he breaks me with a storm, and multiplies my wounds without cause.
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 He will not allow me to catch my breath, but fills me with bitterness.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 If it is a matter of strength, behold, he is mighty! If of justice, ‘Who,’ says he, ‘will summon me?’
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Though I am righteous, my own mouth will condemn me. Though I am blameless, it will prove me perverse.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 I am blameless. I don’t respect myself. I despise my life.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 “It is all the same. Therefore I say he destroys the blameless and the wicked.
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 If the scourge kills suddenly, he will mock at the trial of the innocent.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 The earth is given into the hand of the wicked. He covers the faces of its judges. If not he, then who is it?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 “Now my days are swifter than a runner. They flee away. They see no good.
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 They have passed away as the swift ships, as the eagle that swoops on the prey.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 If I say, ‘I will forget my complaint, I will put off my sad face, and cheer up,’
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 I am afraid of all my sorrows. I know that you will not hold me innocent.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 I will be condemned. Why then do I labor in vain?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 If I wash myself with snow, and cleanse my hands with lye,
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 yet you will plunge me in the ditch. My own clothes will abhor me.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 For he is not a man, as I am, that I should answer him, that we should come together in judgment.
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 There is no umpire between us, that might lay his hand on us both.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Let him take his rod away from me. Let his terror not make me afraid;
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 then I would speak, and not fear him, for I am not so in myself.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.

< Job 9 >