< Job 41 >

1 “Can you draw out Leviathan with a fish hook, or press down his tongue with a cord?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Can you put a rope into his nose, or pierce his jaw through with a hook?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Will he make many petitions to you, or will he speak soft words to you?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Will he make a covenant with you, that you should take him for a servant forever?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Will you play with him as with a bird? Or will you bind him for your girls?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Will traders barter for him? Will they part him among the merchants?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Can you fill his skin with barbed irons, or his head with fish spears?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Lay your hand on him. Remember the battle, and do so no more.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Behold, the hope of him is in vain. Won’t one be cast down even at the sight of him?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 None is so fierce that he dare stir him up. Who then is he who can stand before me?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Who has first given to me, that I should repay him? Everything under the heavens is mine.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 “I will not keep silence concerning his limbs, nor his mighty strength, nor his goodly frame.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Who can strip off his outer garment? Who will come within his jaws?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Who can open the doors of his face? Around his teeth is terror.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Strong scales are his pride, shut up together with a close seal.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 One is so near to another, that no air can come between them.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 They are joined to one another. They stick together, so that they can’t be pulled apart.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 His sneezing flashes out light. His eyes are like the eyelids of the morning.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Out of his mouth go burning torches. Sparks of fire leap out.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Out of his nostrils a smoke goes, as of a boiling pot over a fire of reeds.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 His breath kindles coals. A flame goes out of his mouth.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 There is strength in his neck. Terror dances before him.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 The flakes of his flesh are joined together. They are firm on him. They can’t be moved.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 His heart is as firm as a stone, yes, firm as the lower millstone.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 When he raises himself up, the mighty are afraid. They retreat before his thrashing.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 If one attacks him with the sword, it can’t prevail; nor the spear, the dart, nor the pointed shaft.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 He counts iron as straw, and bronze as rotten wood.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 The arrow can’t make him flee. Sling stones are like chaff to him.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Clubs are counted as stubble. He laughs at the rushing of the javelin.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 His undersides are like sharp potsherds, leaving a trail in the mud like a threshing sledge.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 He makes the deep to boil like a pot. He makes the sea like a pot of ointment.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 He makes a path shine after him. One would think the deep had white hair.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 On earth there is not his equal, that is made without fear.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 He sees everything that is high. He is king over all the sons of pride.”
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Job 41 >