< Job 34 >

1 Moreover Elihu answered and said:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Hear my words, ye wise men; and give ear unto me, ye that have knowledge.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 For the ear trieth words, as the palate tasteth food.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Let us choose for us that which is right; let us know among ourselves what is good.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 For Job hath said: 'I am righteous, and God hath taken away my right;
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Notwithstanding my right I am accounted a liar; my wound is incurable, though I am without transgression.'
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 What man is like Job, who drinketh up scorning like water?
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Who goeth in company with the workers of iniquity, and walketh with wicked men.
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 For he hath said: 'It profiteth a man nothing that he should be in accord with God.'
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 Therefore hearken unto me, ye men of understanding: Far be it from God, that He should do wickedness; and from the Almighty, that He should commit iniquity.
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 For the work of a man will He requite unto him, and cause every man to find according to his ways.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Yea, of a surety, God will not do wickedly, neither will the Almighty pervert justice.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Who gave Him a charge over the earth? Or who hath disposed the whole world?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 If He set His heart upon man, if He gather unto Himself his spirit and his breath;
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 All flesh shall perish together, and man shall return unto dust.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 If now thou hast understanding, hear this; hearken to the voice of my words.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Shall even one that hateth right govern? And wilt thou condemn Him that is just and mighty —
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Is it fit to say to a king: 'Thou art base'? Or to nobles: 'Ye are wicked'? —
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 That respecteth not the persons of princes, nor regardeth the rich more than the poor? For they all are the work of His hands.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 In a moment they die, even at midnight; the people are shaken and pass away, and the mighty are taken away without hand.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 For His eyes are upon the ways of a man, and He seeth all his goings.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 There is no darkness, nor shadow of death, where the workers of iniquity may hide themselves.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 For He doth not appoint a time unto any man, when he should go before God in judgment.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 He breaketh in pieces mighty men without inquisition, and setteth others in their stead.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Therefore He taketh knowledge of their works; and He overturneth them in the night, so that they are crushed.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 He striketh them as wicked men in the open sight of others;
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Because they turned aside from following Him, and would not have regard to any of His ways;
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 So that they cause the cry of the poor to come unto Him, and He heareth the cry of the afflicted.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 When He giveth quietness, who then can condemn? And when He hideth His face, who then can behold Him? whether it be done unto a nation, or unto a man, alike;
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 That the godless man reign not, that there be none to ensnare the people.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 For hath any said unto God: 'I have borne chastisement, though I offend not;
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 That which I see not teach Thou me; if I have done iniquity, I will do it no more'?
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Shall His recompense be as thou wilt? For thou loathest it, so that thou must choose, and not I; therefore speak what thou knowest.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Men of understanding will say unto me, yea, every wise man that heareth me:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 'Job speaketh without knowledge, and his words are without discernment.'
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Would that Job were tried unto the end, because of his answering like wicked men.
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 For he addeth rebellion unto his sin, he clappeth his hands among us, and multiplieth his words against God.
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >