< Psalms 1 >

1 BOOK I HAPPY IS the man that hath not walked in the counsel of the wicked, nor stood in the way of sinners, nor sat in the seat of the scornful.
Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 But his delight is in the law of the LORD; and in His law doth he meditate day and night.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 And he shall be like a tree planted by streams of water, that bringeth forth its fruit in its season, and whose leaf doth not wither; and in whatsoever he doeth he shall prosper.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Not so the wicked; but they are like the chaff which the wind driveth away.
Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 Therefore the wicked shall not stand in the judgment, nor sinners in the congregation of the righteous.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 For the LORD regardeth the way of the righteous; but the way of the wicked shall perish.
Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

< Psalms 1 >