< Ezekiel 23 >

1 The worde of the Lord came againe vnto me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
2 Sonne of man, there were two women, the daughters of one mother.
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 And they committed fornication in Egypt, they committed fornication in their youth: there were their breasts pressed, and there they bruised the teates of their virginitie.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 And the names of them were Aholah the elder, and Aholibah her sister: and they were mine, and they bare sonnes and daughters: thus were their names. Samaria is Aholah, and Ierusalem Aholibah.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 And Aholah played the harlot when she was mine, and she was set on fire with her louers, to wit, with the Assyrians her neighbours,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 Which were clothed with blewe silke, both captaines and princes: they were all pleasant yong men, and horsemen riding vpon horses.
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 Thus she committed her whoredome with them, euen with all them that were the chosen men of Asshur, and with all on whome she doted, and defiled her selfe with all their idoles.
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 Neither left she her fornications, learned of the Egyptians: for in her youth they lay with her, and they bruised the breasts of her virginitie, and powred their whoredome vpon her.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 Wherefore I deliuered her into the hands of her louers, euen into the hands of the Assyrians, vpon whome she doted.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 These discouered her shame: they tooke away her sonnes and her daughters, and slewe her with the sworde, and she had an euill name among women: for they had executed iudgement vpon her.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 And when her sister Aholibah sawe this, she marred her selfe with inordinate loue, more then she, and with her fornications more then her sister with her fornications.
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 She doted vpon the Assyrians her neighbours, both captaines and princes clothed with diuers sutes, horsemen ryding vpon horses: they were all pleasant yong men.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 Then I sawe that she was defiled, and that they were both after one sort,
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 And that she encreased her fornications: for when she sawe men painted vpon the wall, the images of the Caldeans painted with vermelon,
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 And girded with girdles vpon their loynes, and with dyed attyre vpon their heads (looking all like princes after the maner of the Babylonians in Caldea, the land of their natiuitie)
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 Assoone, I say, as she sawe them, she doted vpon them, and sent messengers vnto them into Caldea.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 Nowe when the Babylonians came to her into the bed of loue, they defiled her with their fornication, and she was polluted with them, and her lust departed from them.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 So she discouered her fornication, and disclosed her shame: then mine heart forsooke her, like as mine heart had forsaken her sister.
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 Yet she encreased her whoredome more, and called to remembrance ye dayes of her youth, wherein she had played the harlot in the land of Egypt.
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 For she doted vpon their seruants whose members are as the members of asses, and whose yssue is like the yssue of horses.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 Thou calledst to remembrance the wickednes of thy youth, when thy teates were bruised by ye Egyptians: therefore ye paps of thy youth are thus.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 Therefore, O Aholibah, thus sayeth the Lord God, Beholde, I will raise vp thy louers against thee, from whome thine heart is departed, and I will bring them against thee on euery side,
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 To wit, the Babylonians, and all the Caldeans, Peked, and Shoah, and Koa, and all the Assyrians with them: they were all pleasant yong men, captaines and princes: all they were valiant and renoumed, riding vpon horses.
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 Euen these shall come against thee with charets, waggons, and wheeles, and with a multitude of people, which shall set against thee, buckler and shield, and helmet round about: and I will leaue the punishment vnto them, and they shall iudge thee according to their iudgements.
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 And I wil lay mine indignation vpon thee, and they shall deale cruelly with thee: they shall cut off thy nose and thine eares, and thy remnant shall fall by the sword: they shall cary away thy sonnes and thy daughters, and thy residue shall be deuoured by the fire.
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 They shall also strip thee out of thy clothes, and take away thy fayre iewels.
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 Thus wil I make thy wickednes to cease from thee and thy fornication out of the land of Egypt: so that thou shalt not lift vp thine eyes vnto them, nor remember Egypt any more.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 For thus saith the Lord God, Behold, I wil deliuer thee into the hand of them, whome thou hatest: euen into the hands of them from whome thine heart is departed.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 And they shall handle thee despitefully, and shall take away all thy labour, and shall leaue thee naked and bare, and the shame of thy fornications shalbe discouered, both thy wickednes, and thy whoredome.
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 I wil doe these things vnto thee, because thou hast gone a whoring after the heathen, and because thou art polluted with their idoles.
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Thou hast walked in the way of thy sister: therefore wil I giue her cup into thine hand.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 Thus saith ye Lord God, Thou shalt drinke of thy sisters cup, deepe and large: thou shalt be laughed to scorne and had in derision, because it containeth much.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Thou shalt be filled with drunkennes and sorow, euen with the cup of destruction, and desolation, with the cup of thy sister Samaria.
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 Thou shalt euen drinke it, and wring it out to the dregges, and thou shalt breake the sheards thereof, and teare thine owne breasts: for I haue spoken it, sayth the Lord God.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 Therefore thus saith the Lord God, Because thou hast forgotten me, and cast me behinde thy backe, therefore thou shalt also beare thy wickednes and thy whoredome.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 The Lord sayd moreouer vnto me, Sonne of man, wilt thou iudge Aholah and Aholibah? and wilt thou declare to them their abominations?
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 For they haue played the whores, and blood is in their hands, and with their idoles haue they committed adulterie, and haue also caused their sonnes, whome they bare vnto me, to passe by the fire to be their meate.
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 Moreouer, thus haue they done vnto me: they haue defiled my Sanctuarie in the same day, and haue prophaned my Sabbaths.
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 For when they had slaine their children to their idoles, they came the same day into my Sanctuarie to defile it: and loe, thus haue they done in the middes of mine house.
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 And howe much more is it that they sent for men to come from farre vnto whom a messenger was sent, and loe, they came? for whome thou diddest wash thy selfe, and paintedst thine eyes, and deckedst thee with ornaments,
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 And satest vpon a costly bed, and a table prepared before it, whereupon thou hast set mine incense and mine oyle.
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 And a voyce of a multitude being at ease, was with her: and with the men to make the company great were brought men of Saba from the wildernes, which put bracelets vpon their hands, and beautifull crownes vpon their heads.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 Then I sayd vnto her, that was olde in adulteries, Now shall she and her fornications come to an end.
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 And they went in vnto her as they goe to a common harlot: so went they to Aholah and Aholibah the wicked women.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 And ye righteous men they shall iudge them, after the maner of harlots, and after the maner of murtherers: for they are harlots, and blood is in their hands.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 Wherefore thus sayth the Lord God, I will bring a multitude vpon them, and will giue them vnto the tumult, and to the spoyle,
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 And the multitude shall stone them with stones, and cut them with their swordes: they shall slay their sonnes, and their daughters, and burne vp their houses with fire.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 Thus will I cause wickednesse to cease out of the land, that all women may be taught not to doe after your wickednesse.
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 And they shall laye your wickednesse vpon you, and ye shall beare the sinnes of your idoles, and ye shall knowe that I am the Lord God.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 23 >