< Ezekiel 22 >

1 Moreover, the worde of the Lord came vnto me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
2 Now thou sonne of man, wilt thou iudge, wilt thou iudge this bloody citie? wilt thou shew her all her abominations?
“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
3 Then say, Thus sayth the Lord God, The citie sheddeth blood in the middes of it, that her time may come, and maketh idols against her selfe to pollute her selfe.
ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
4 Thou hast offended in thy blood, that thou hast shed, and hast polluted thy selfe in thine idols, which thou hast made, and thou hast caused thy dayes to draw neere, and art come vnto thy terme: therefore haue I made thee a reproch to the heathen, and a mocking to all countreys.
wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
5 Those that be neere, and those that be farre from thee, shall mocke thee, which art vile in name and sore in affliction.
Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
6 Beholde, the princes of Israel euery one in thee was ready to his power, to shed blood.
“‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
7 In thee haue they despised father and mother: in the middes of thee haue they oppressed the stranger: in thee haue they vexed the fatherlesse and the widowe.
Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
8 Thou hast despised mine holy things, and hast polluted my Sabbaths.
Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
9 In thee are men that cary tales to shed blood: in thee are they that eate vpon the mountaines: in ye mids of thee they comit abomination.
Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
10 In thee haue they discouered their fathers shame: in thee haue they vexed her that was polluted in her floures.
Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
11 And euery one hath committed abomination with his neighbours wife, and euery one hath wickedly defiled his daughter in lawe, and in thee hath euery man forced his owne sister, euen his fathers daughter.
Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
12 In thee haue they taken giftes to shed blood: thou hast taken vsurie and the encrease, and thou hast defrauded thy neighbours by extortion, and hast forgotten me, saith the Lord God.
Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
13 Beholde, therefore I haue smitten mine hands vpon thy couetousnesse, that thou hast vsed, and vpon the blood, which hath bene in the middes of thee.
“‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
14 Can thine heart endure, or can thine hands be strong, in the dayes that I shall haue to doe with thee? I the Lord haue spoken it, and will doe it.
Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
15 And I wil scatter thee among the heathen, and disperse thee in the countreys, and will cause thy filthines to cease from thee.
Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
16 And thou shalt take thine inheritance in thy selfe in the sight of the heathen, and thou shalt knowe that I am the Lord.
Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
17 And the worde of the Lord came vnto me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
18 Sonne of man, the house of Israel is vnto me as drosse: all they are brasse, and tinne, and yron, and leade in the mids of the fornace: they are euen the drosse of siluer.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
19 Therefore, thus sayth the Lord God, Because ye are all as drosse, beholde, therefore I will gather you in the middes of Ierusalem.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
20 As they gather siluer and brasse, and yron, and leade, and tinne into the middes of the fornace, to blowe the fire vpon it to melt it, so wil I gather you in mine anger and in my wrath, and wil put you there and melt you.
Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
21 I wil gather you, I say, and blowe the fire of my wrath vpon you, and you shalbe melted in the mids thereof.
Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
22 As siluer is melted in the mids of the fornace, so shall ye be melted in the mids thereof, and ye shall knowe, that I the Lord haue powred out my wrath vpon you.
Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
23 And the worde of the Lord came vnto me, saying,
Yehova anandiyankhulanso nati,
24 Sonne of man, say vnto her; Thou art the land, that is vncleane, and not rained vpon in the day of wrath.
“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
25 There is a conspiracie of her prophets in the mids thereof like a roaring lyon, rauening the praye: they haue deuoured soules: they haue taken the riches and precious things: they haue made her many widowes in the mids thereof.
Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
26 Her Priests haue broken my Lawe, and haue defiled mine holy things: they haue put no difference betweene the holy and prophane, neither discerned betweene the vncleane, and the cleane, and haue hid their eyes from my Sabbaths, and I am prophaned among them.
Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
27 Her princes in the mids thereof are like wolues, rauening the praye to shed blood, and to destroy soules for their owne couetous lucre.
Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
28 And her prophets haue dawbed them with vntempered morter, seeing vanities, and diuining lies vnto them, saying, Thus sayth the Lord God, when the Lord had not spoken.
Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
29 The people of the land haue violently oppressed by spoyling and robbing, and haue vexed the poore and the needy: yea, they haue oppressed the stranger against right.
Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
30 And I sought for a man among them, that should make vp the hedge, and stand in the gap before me for the land, that I should not destroy it, but I found none.
“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
31 Therefore haue I powred out mine indignation vpon them, and consumed them with the fire of my wrath: their owne wayes haue I rendred vpon their heads, sayth the Lord God.
Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 22 >