< Ruth 3 >

1 But afterwards, when she returned to her mother-in-law, Naomi said to her: “My daughter, I will seek rest for you, and I will provide so that it may be well with you.
Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
2 This Boaz, whose young women you joined in the field, is our near relative, and this night he will winnow the threshing floor of barley.
Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
3 Therefore, wash and anoint yourself, and put on your decorative garments, and go down to the threshing floor, but do not let the man see you, while he finishes eating and drinking.
Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
4 But when he goes to sleep, observe the place where he sleeps. And you will approach and lift up the covering, the part which covers near his feet, and lay yourself down, and sleep there; but he will tell you what you are obliged to do.”
Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 She answered, “I will do everything as you have instructed.”
Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 And she went down to the threshing floor, and she did everything that her mother-in-law had commanded her.
Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 And when Boaz had finished eating and drinking, and he was merry, and he had gone to sleep by the pile of sheaves, she approached secretly, and, lifting the covering near his feet, she laid herself down.
Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 And behold, when it was the middle of the night, the man became frightened and confused, and he saw a woman lying near his feet.
Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 And he said to her, “Who are you?” And she answered, “I am Ruth, your handmaid. Spread your covering over your servant, for you are a near relative.”
Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 And he said, “You are blessed by the Lord, daughter, and you have excelled beyond your earlier benevolence, because you have not followed young men, whether poor or rich.
Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
11 Therefore, do not be afraid, but whatever you decide about me, I will accomplish for you. For all the people, who dwell within the gates of my city, know that you are a virtuous woman.
Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
12 Neither do I deny myself to be a near relative, but there is another nearer than I.
Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
13 Be at peace for this night. And when morning arrives, if he is willing to uphold the law of kinship for you, things will turn out well; but if he is not willing, then, I will take you, without any doubt, as the Lord lives. Sleep until morning.”
Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
14 And so she slept by his feet until the night was ending. And she arose before men could inquire of one another. And Boaz said, “Be careful, lest someone know that you came here.”
Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
15 And again he said, “Spread your mantle that covers you, and hold it with both hands.” As she extended it and held it, he measured six measures of barley and placed it upon her. Carrying it, she went into the city.
Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
16 And she came to her mother-in-law, who said to her: “What have you been doing, daughter?” And she explained to her all that the man had accomplished for her.
Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
17 And she said, “Behold, he gave me six measures of barley, for he said, ‘I am not willing to have you return empty to your mother-in-law.’”
Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
18 And Naomi said, “Wait, daughter, until we see how things will turn out. For the man will not rest until he has accomplished what he said.”
Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”

< Ruth 3 >