< 1 Samuel 1 >

1 There was a certain man from Ramah of Zophim, on Mount Ephraim, and his name was Elkanah, the son of Jeroham, the son of Elihu, the son of Tohu, the son of Zuph, an Ephraimite.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 And he had two wives: the name of one was Hannah, and the name of the second was Peninnah. And Peninnah had sons. But Hannah did not have children.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 And this man went up from his city, on the established days, so that he might adore and sacrifice to the Lord of hosts at Shiloh. Now the two sons of Eli, Hophni and Phinehas, priests of the Lord, were in that place.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 Then the day arrived, and Elkanah immolated. And he gave portions to his wife Peninnah, and to all her sons and daughters.
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 But to Hannah he gave one portion with sorrow. For he loved Hannah, but the Lord had closed her womb.
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 And her rival afflicted her and vehemently distressed her, to a great extent, for she rebuked her that the Lord had closed her womb.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 And she did so every year, when the time returned for them to ascend to the temple of the Lord. And she provoked her in this way. And so, she wept and did not take food.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 Therefore, her husband Elkanah said to her: “Hannah, why are you weeping? And why do you not eat? And for what reason do you afflict your heart? Am I not better to you than ten sons?”
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 And so, after she ate and drank at Shiloh, Hannah rose up. And Eli, the priest, was sitting on the seat before the door of the temple of the Lord.
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 And since Hannah was bitter in soul, she prayed to the Lord, weeping greatly.
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 And she made a vow, saying, “O Lord of hosts, if, in looking with favor, you will see the affliction of your servant and will remember me, and will not forget your handmaid, and if you will give to your servant a male child, then I will give him to the Lord all the days of his life, and no razor shall pass over his head.”
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Then it happened that, while she multiplied prayers before the Lord, Eli observed her mouth.
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 For Hannah was speaking in her heart, and only her lips moved, and her voice was barely heard. Therefore, Eli considered her to be drunk,
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 and so he said to her: “How long will you be inebriated? You should take only a little wine, but instead you are drenched.”
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 Responding, Hannah said: “By no means, my lord. For I am an exceedingly unhappy woman, and I drank neither wine, nor anything that can inebriate. Instead, I have poured out my soul in the sight of the Lord.
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 You should not repute your handmaid as one of the daughters of Belial. For I have been speaking from the abundance of my sorrow and grief, even until now.”
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Then Eli said to her: “Go in peace. And may the God of Israel grant to you your petition, which you have begged of him.”
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 And she said, “I wish that your handmaid may find grace in your eyes.” And the woman went on her way, and she ate, and her countenance was no longer changed for the worse.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 And they rose up in the morning, and they worshipped before the Lord. And they returned and arrived at their own house at Ramah. Then Elkanah knew his wife Hannah. And the Lord remembered her.
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 And it happened that, in the course of days, Hannah conceived and bore a son. And she called his name Samuel, because she had requested him from the Lord.
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 Now her husband Elkanah ascended with his entire house, so that he might immolate to the Lord a solemn sacrifice, with his vow.
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 But Hannah did not go up. For she said to her husband, “I will not go, until the infant has been weaned, and until I may lead him, so that he may appear before the sight of the Lord, and may remain always there.”
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 And her husband Elkanah said to her: “Do what seems good to you, and stay until you wean him. And I pray that the Lord may fulfill his word.” Therefore, the woman remained at home, and she breastfed her son, until she withdrew him from milk.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 And after she had weaned him, she brought him with her, along with three calves, and three measures of flour, and a small bottle of wine, and she led him to the house of the Lord at Shiloh. But the boy was still a young child.
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 And they immolated a calf, and they presented the boy to Eli.
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 And Hannah said: “I beg you, my lord, as your soul lives, my lord: I am that woman, who stood before you here, praying to the Lord.
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 I prayed for this child, and the Lord granted to me my petition, which I asked of him.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Because of this, I have also lent him to the Lord, for all the days when he shall be lent to the Lord.” And they adored the Lord in that place. And Hannah prayed, and she said:
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 1 >