< Leviticus 24 >

1 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Instruct the sons of Israel, so that they may bring to you clear oil from the purest olives, in order to supply the lamps continuously
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
3 outside the veil of the testimony in the tabernacle of the covenant. And Aaron shall place these, from evening until morning, before the Lord, as a perpetual worship and ritual in your generations.
Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
4 They shall be placed upon the most pure candlestick in the sight of the Lord always.
Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
5 You shall also receive fine wheat flour, and you shall bake twelve loaves from it, each loaf of which shall have two-tenths.
“Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
6 And you shall arrange them, six on each side, upon the most pure table before the Lord.
Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
7 And you shall place upon them the clearest frankincense, so that the bread may be a memorial of oblation for the Lord.
Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
8 On each Sabbath, they shall be changed before the Lord, having been received from the sons of Israel as an everlasting covenant.
Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
9 And they shall be for Aaron and his sons, so that they may eat these in the holy place; for it is the Holy of holies from the sacrifices of the Lord, as a perpetual right.
Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
10 Then, behold, the son of an Israelite woman, whom she had born of an Egyptian man among the sons of Israel, going out, was quarreling in the camp with a man of Israel.
Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
11 And when he had blasphemed the name, and had cursed it, he was led to Moses. (Now his mother was called Shelomith, the daughter of Dibri from the tribe of Dan.)
Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
12 And they sent him to prison, until they might know what the Lord would command,
Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
13 who spoke to Moses,
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
14 saying: Lead away the blasphemer beyond the camp, and let all who heard him place their hands upon his head, and let the entire people stone him.
“Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
15 And you shall say to the sons of Israel: The man who curses his God shall bear his sin,
Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
16 and whoever will have blasphemed the name of the Lord shall be put to death. The entire multitude shall overwhelm him with stones, whether he be a citizen or a sojourner. Whoever blasphemes the name of the Lord shall be put to death.
Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
17 Whoever will have struck and killed a man shall be put to death.
“‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
18 Whoever will have struck down an animal shall repay its equivalent, that is, a life for a life.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
19 Whoever will have inflicted a blemish on any of his citizens, just as he has done, so shall it be done to him:
Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
20 fracture for fracture, eye for eye, tooth for tooth, shall he repay. Whatever degree of blemish he has inflicted, so shall he be compelled to suffer.
kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
21 Whoever strikes down a beast, shall repay another. Whoever strikes a man shall be punished.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
22 Let there be equal judgment among you, whether it is a sojourner or a citizen who will have sinned. For I am the Lord your God.
Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 And Moses spoke to the sons of Israel. And they led away him who had blasphemed, beyond the camp, and they overwhelmed him with stones. And the sons of Israel did just as the Lord had instructed Moses.
Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.

< Leviticus 24 >