< Leviticus 23 >

1 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speak to the sons of Israel, and you shall say to them: These are the feasts of the Lord, which you shall call holy.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
3 For six days you shall do work; the seventh day, because it is the rest of the Sabbath, shall be called holy. You shall do no work on that day; it is the Sabbath of the Lord in all your dwelling places.
“‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
4 Therefore, these are the feasts of the Lord, which you must celebrate in their times.
“‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
5 The first month, the fourteenth day of the month, at evening, is the Passover of the Lord.
Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
6 And the fifteenth day of this month is the solemnity of the unleavened bread of the Lord. For seven days shall you eat unleavened bread.
Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
7 The first day shall be greatly honored and holy to you; you shall do no servile work in it.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
8 But you shall offer a sacrifice with fire, for seven days, to the Lord. Then the seventh day shall be more honored and more holy; and you shall do no servile work in it.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
9 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
10 Speak to the sons of Israel, and you shall say to them: When you will have entered into the land which I will give to you, and you will have harvested your grain fields, you shall carry the sheaves of grain, the first-fruits of your harvest, to the priest.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
11 He shall lift up a sheaf before the Lord, on the day after the Sabbath, so that it may be acceptable for you, and he shall sanctify it.
Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
12 And on the same day that the sheaf is consecrated, a one-year-old immaculate lamb shall be slain as a holocaust of the Lord.
Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
13 And the libations shall be offered with it: two-tenths of fine wheat flour sprinkled with oil, as an incense and a most sweet odor for the Lord; likewise, libations of wine, the fourth part of a hin.
Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
14 Bread, and parched grain, and boiled grain, you shall not eat from the grain field, until the day when you shall offer from it to your God. It is an everlasting precept in your generations and in all of your dwelling places.
Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
15 Therefore, you shall number from the day after the Sabbath, in which you offered a sheaf of the first-fruits, seven full weeks,
“‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
16 all the way to the day after the completion of the seventh week, that is, fifty days, and then you shall offer a new sacrifice to the Lord,
Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
17 from all of your dwelling places: two loaves from the first-fruits, from two-tenths of leavened fine wheat flour, which you shall bake as the first-fruits of the Lord.
Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
18 And you shall offer with the bread: seven immaculate one-year-old lambs, and one calf from the herd, and two rams, and these shall be a holocaust, with their libations, as a most sweet odor to the Lord.
Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
19 You shall also offer a he-goat for sin, and two one-year-old lambs as victims of peace offerings.
Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
20 And when the priest has lifted them up with the loaves of the first-fruits, in the sight of the Lord, they shall fall to his use.
Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
21 And you shall call this day most honored and most holy; you shall do no servile work in it. It shall be an everlasting ordinance in all your dwelling places and generations.
Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
22 And when you will have harvested the grain fields of your land, you shall not cut it down all the way to the ground; neither shall you gather the remnants of the ears of grain, but you shall leave these for paupers and strangers. I am the Lord your God.
“‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
24 Say to the sons of Israel: The seventh month, the first day of the month, shall be a Sabbath for you, a memorial, with the sounding of trumpets, and it shall be called holy.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
25 You shall do no servile work in it, and you shall offer a holocaust to the Lord.
Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
26 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
27 The tenth day of this seventh month shall be the day of atonement; it shall be most honored, and it shall be called holy. And you shall afflict your souls on that day, and you shall offer a holocaust to the Lord.
“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
28 You shall do no servile work in the time of this day; for it is a day of propitiation, so that the Lord your God may be merciful to you.
Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Every soul that has not been afflicted on this day shall perish from his people,
Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
30 and anyone who will have done work, I shall wipe him away from his people.
Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
31 Therefore, you shall do no work on that day. This shall be an everlasting ordinance for you in all your generations and dwelling places.
Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
32 It is a Sabbath of rest, and you shall afflict your souls beginning on the ninth day of the month: from evening until evening you shall celebrate your Sabbaths.
Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
33 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
34 Say to the sons of Israel: From the fifteenth day of this seventh month, there shall be the Feast of Tabernacles: seven days for the Lord.
“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
35 The first day shall be called most honored and most holy; you shall do no servile work in it.
Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
36 And for seven days you shall offer holocausts to the Lord. Likewise, the eighth day shall be most honored and most holy, and you shall offer holocausts to the Lord. For it is the day of assembly and gathering. You shall do no servile work in it.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
37 These are the feasts of the Lord, which you shall call most honored and most holy, and in them you shall offer oblations to the Lord: holocausts and libations according to the rite of each particular day,
(“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
38 aside from the Sabbaths of the Lord, and your donations, and that which you offer by a vow, or which you give to the Lord spontaneously.
Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
39 Therefore, from the fifteenth day of the seventh month, when you will have gathered together all the fruits of your land, you shall celebrate the feast of the Lord for seven days. The first day and the eighth day shall be a Sabbath, that is, a day of rest.
“‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
40 And you shall take for yourselves, on the first day, the fruits of the most beautiful tree, and branches of palm trees, and branches of trees with thick foliage, and willows from the torrent. And you shall rejoice in the sight of the Lord your God.
Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
41 And you shall celebrate its solemnity for seven days each year. This shall be an everlasting ordinance in your generations. In the seventh month, you shall celebrate the feast,
Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
42 and you shall live under shelters for seven days. All who are of the family of Israel shall dwell in tabernacles,
Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
43 so that your posterity may learn that I caused the sons of Israel to live in tabernacles, when I led them away from the land of Egypt. I am the Lord your God.
kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
44 And Moses spoke about the solemnities of the Lord to the sons of Israel.
Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

< Leviticus 23 >