< Acts 5 >

1 But a certain man named Ananias, with his wife Sapphira, sold a field,
Koma munthu wina dzina lake Hananiya, pamodzi ndi mkazi wake Safira, anagulitsanso munda wawo.
2 and he was deceitful about the price of the field, with his wife’s consent. And bringing only part of it, he placed it at the feet of the Apostles.
Mogwirizana ndi mkazi wakeyo anapatulapo pa ndalamazo nazisunga, ndipo anatenga zotsalazo ndi kukapereka kwa atumwi.
3 But Peter said: “Ananias, why has Satan tempted your heart, so that you would lie to the Holy Spirit and be deceitful about the price of the land?
Koma Petro anamufunsa kuti, “Hananiya, chifukwa chiyani Satana anadzaza chotere mu mtima wako kuti unamize Mzimu Woyera ndipo wapatula ndi kusunga ndalama?
4 Did it not belong to you while you retained it? And having sold it, was it not in your power? Why have you set this thing in your heart? You have not lied to men, but to God!”
Kodi sunali wako usanagulitse? Ndipo utagulitsa ndalamazo sizinali mʼmanja mwako kodi? Nʼchiyani chinakuchititsa zimenezi? Iwe sunanamize anthu koma Mulungu.”
5 Then Ananias, upon hearing these words, fell down and expired. And a great fear overwhelmed all who heard of it.
Hananiya atamva mawu amenewa anagwa pansi namwalira. Onse amene anamva zimene zinachitikazi anachita mantha kwambiri.
6 And the young men rose up and removed him; and carrying him out, they buried him.
Kenaka anyamata anafika, nakulunga thupi lake, ndipo anamunyamula ndi kukamuyika mʼmanda.
7 Then about the space of three hours passed, and his wife entered, not knowing what had happened.
Patapita maora atatu mkazi wake analowa, wosadziwa zimene zinachitika.
8 And Peter said to her, “Tell me, woman, if you sold the field for this amount?” And she said, “Yes, for that amount.”
Petro anamufunsa iye kuti, “Tandiwuza, kodi izi ndi ndalama zonse zimene iwe ndi Hananiya munalandira mutagulitsa munda?” Mkaziyo anati, “Inde ndi zimenezo.”
9 And Peter said to her: “Why have you agreed together to test the Spirit of the Lord? Behold, the feet of those who have buried your husband are at the door, and they shall carry you out!”
Petro anati kwa iye, “Bwanji inu munapangana kuyesa Mzimu wa Ambuye? Taona! Anthu amene anakayika mwamuna wako mʼmanda ali pa khomo, ndipo adzakunyamula iwenso.”
10 Immediately, she fell down before his feet and expired. Then the young men entered and found her dead. And they carried her out and buried her next to her husband.
Nthawi yomweyo anagwa pansi pa mapazi a Petro ndipo anamwalira. Ndipo anyamata aja analowa, napeza kuti wafa kale, anamunyamula ndi kukamuyika pafupi ndi mwamuna wake.
11 And a great fear came over the entire Church and over all who heard these things.
Mpingo wonse ndi anthu onse amene anamva zimenezi anachita mantha kwambiri.
12 And through the hands of the Apostles many signs and wonders were accomplished among the people. And they all met with one accord at Solomon’s portico.
Atumwi anachita zizindikiro zodabwitsa ndi zozizwitsa zambiri pakati pa anthu. Ndipo onse okhulupirira ankasonkhana pamodzi mu Khonde la Solomoni.
13 And among the others, no one dared to join himself to them. But the people magnified them.
Palibe ndi mmodzi yemwe analimba mtima kuphatikana nawo, ngakhale kuti anthu onse amawalemekeza kwambiri.
14 Now the multitude of men and women who believed in the Lord was ever increasing,
Ngakhale zinali chotere, anthu ambiri anakhulupirira Ambuye ndipo amawonjezeredwa ku chiwerengero chawo.
15 so much so that they laid the infirm in the streets, placing them on beds and stretchers, so that, as Peter arrived, at least his shadow might fall upon any one of them, and they would be freed from their infirmities.
Chifukwa cha zimenezi, anthu anabweretsa odwala mʼmisewu ya mu mzinda nawagoneka pa mabedi ndi pa mphasa kuti chithunzi chokha cha Petro chikhudze ena mwa iwo iye akamadutsa.
16 But a multitude also hurried to Jerusalem from the neighboring cities, carrying the sick and those troubled by unclean spirits, who were all healed.
Anthu ochuluka ochokera ku mizinda yayingʼono ozungulira Yerusalemu amasonkhananso atatenga odwala awo ndi iwo amene amasautsidwa ndi mizimu yoyipa ndipo onsewo amachiritsidwa.
17 Then the high priest and all those who were with him, that is, the heretical sect of the Sadducees, rose up and were filled with jealousy.
Koma mkulu wa ansembe pamodzi ndi onse omuthandiza, amene anali a gulu la Asaduki, anachita nsanje.
18 And they laid hands on the Apostles, and they placed them in the common prison.
Iwo anagwira atumwi ndi kuwatsekera mʼndende ya anthu wamba.
19 But in the night, an Angel of the Lord opened the doors of the prison and led them out, saying,
Koma usiku mngelo wa Ambuye anatsekula zitseko za ndende ndi kuwatulutsa
20 “Go and stand in the temple, speaking to the people all these words of life.”
Mngeloyo anati, “Pitani, ku mabwalo a Nyumba ya Mulungu ndipo mukawuze anthu uthenga onse wamoyo watsopanowu.”
21 And when they had heard this, they entered the temple at first light, and they were teaching. Then the high priest, and those who were with him, approached, and they called together the council and all the elders of the sons of Israel. And they sent to the prison to have them brought.
Kutacha mmawa, atumwi analowa mʼbwalo la mʼNyumba ya Mulungu, monga anawuzidwa ndipo anayamba kuphunzitsa anthu. Mkulu wa ansembe pamodzi ndi omuthandiza ake amene anali naye anafika, anayitanitsa msonkhano wa Bwalo Lalikulu, ndilo bwalo la akulu onse a Israeli. Anatuma alonda kuti akatenge atumwi aja kundende.
22 But when the attendants had arrived, and, upon opening the prison, had not found them, they returned and reported to them,
Koma alonda aja atafika kundende, sanawapezemo. Iwo anabwerera nakawafotokozera
23 saying: “We found the prison certainly locked up with all diligence, and the guards standing before the door. But upon opening it, we found no one within.”
kuti, “Tinakapeza ndende ili chitsekere ndithu, ndi alonda atayimirira pa khomo, koma pamene tinatsekula zitseko, sitinapezemo munthu aliyense mʼkatimo.”
24 Then, when the magistrate of the temple and the chief priests heard these words, they were uncertain about them, as to what should happen.
Mkulu wa alonda a Nyumba ya Mulungu ndi akulu a ansembe atamva zimenezi anathedwa nzeru, osadziwa kuti zimenezi zidzatha bwanji.
25 But someone arrived and reported to them, “Behold, the men whom you placed in prison are in the temple, standing and teaching the people.”
Ndipo wina anabwera ndi kuti, “Taonani! Anthu aja amene munawatsekera mʼndende ali ku Nyumba ya Mulungu ndipo akuphunzitsa anthu.”
26 Then the magistrate, with the attendants, went and brought them without force. For they were afraid of the people, lest they be stoned.
Pamenepo mkulu wa alonda pamodzi ndi alonda anakawatenga atumwi. Sanakawatenge mwaukali, chifukwa amaopa kuti anthu angawaponye miyala.
27 And when they had brought them, they stood them before the council. And the high priest questioned them,
Atafika nawo atumwi aja, anawayimika pamaso pa Bwalo Lalikulu kuti afunsidwe mafunso ndi mkulu wa ansembe.
28 and said: “We strongly order you not to teach in this name. For behold, you have filled Jerusalem with your doctrine, and you wish to bring the blood of this man upon us.”
Iye anati, “Ife tinakuletsani kuti musaphunzitsenso mʼdzina ili, koma inu mwadzaza Yerusalemu ndi chiphunzitso chanu, ndipo mukufuna kutisenzetsa imfa ya munthu ameneyu.”
29 But Peter and the Apostles responded by saying: “It is necessary to obey God, more so than men.
Petro ndi atumwi enawo anayankha kuti, “Ife tiyenera kumvera Mulungu osati anthu!
30 The God of our fathers has raised up Jesus, whom you put to death by hanging him on a tree.
Mulungu wa makolo athu anamuukitsa Yesu, amene inu munamupha pomupachika pa mtengo.
31 It is he whom God has exalted at his right hand as Ruler and Savior, so as to offer repentance and the remission of sins to Israel.
Mulungu anamukweza Iye ku dzanja lake lamanja kukhala Mfumu ndi Mpulumutsi kuti Iye apatse Aisraeli mtima wolapa ndi chikhululukiro cha machimo.
32 And we are witnesses of these things, with the Holy Spirit, whom God has given to all who are obedient to him.”
Ife ndife mboni za zimenezi, ndiponso Mzimu Woyera amene Mulungu anapereka kwa iwo akumvera Iye.”
33 When they had heard these things, they were deeply wounded, and they were planning to put them to death.
Akuluakuluwo atamva zimenezi anakwiya kwambiri nafuna kuwapha.
34 But someone in the council, a Pharisee named Gamaliel, a teacher of the law honored by all the people, rose up and ordered the men to be put outside briefly.
Koma Mfarisi wina dzina lake Gamalieli, mphunzitsi wa malamulo, amene anthu onse amamulemekeza, anayimirira ndi kulamula kuti atumwiwo ayambe apita panja.
35 And he said to them: “Men of Israel, you should be careful in your intentions about these men.
Ndipo iye anawuza bwalolo kuti, “Aisraeli, taganizani bwino, zimene mukufuna kuchita kwa anthu awa.
36 For before these days, Theudas stepped forward, asserting himself to be someone, and a number of men, about four hundred, joined with him. But he was killed, and all who believed in him were scattered, and they were reduced to nothing.
Pakuti masiku a mʼmbuyomu kunali Teuda amene anadzitchukitsa, ndipo anthu pafupifupi 400 anamutsatira. Iye anaphedwa ndipo omutsatira akewo anabalalitsidwa, zonse zinatheratu.
37 After this one, Judas the Galilean stepped forward, in the days of the enrollment, and he turned the people toward himself. But he also perished, and all of them, as many as had joined with him, were dispersed.
Pambuyo pake, nthawi ya kalembera kunalinso Yudasi wa ku Galileya, ndipo anatsogolera gulu la anthu amene anawukira, iyenso anaphedwa ndipo anthu ake onse anabalalitsidwa.
38 And now therefore, I say to you, withdraw from these men and leave them alone. For if this counsel or work is of men, it will be broken.
Chifukwa chake pa nkhani iyi ndikuwuzani kuti, alekeni anthuwa ndipo aloleni apite! Pakuti ngati zimene akuganiza kapena kuchita ndi zochokera kwa munthu zidzalephera.
39 Yet truly, if it is of God, you will not be able to break it, and perhaps you might be found to have fought against God.” And they agreed with him.
Koma ngati ndi zochokera kwa Mulungu inu simudzatha kuwaletsa anthu awa: inu mwina muzapezeka kuti mukulimbana ndi Mulungu.”
40 And calling in the Apostles, having beaten them, they warned them not to speak at all in the name of Jesus. And they dismissed them.
Akuluakulu enawo anavomerezana naye. Iwo anayitana atumwi aja ndipo anawakwapula kwambiri. Ndipo anawalamula kuti asayankhulenso mʼdzina la Yesu ndipo anawamasula.
41 And indeed, they went forth from the presence of the council, rejoicing that they were considered worthy to suffer insult on behalf of the name of Jesus.
Iwo anachoka ku Bwalo Lalikulu akukondwa chifukwa anayesedwa oyenera kunyozedwa chifukwa cha dzina la Yesu.
42 And every day, in the temple and among the houses, they did not cease to teach and to evangelize Christ Jesus.
Ndipo tsiku ndi tsiku, sanaleke kuphunzitsa ndi kulalikira mʼNyumba ya Mulungu komanso nyumba ndi nyumba, Uthenga Wabwino wa kuti Yesu ndi Khristu.

< Acts 5 >